< Proverbes 6 >
1 Mon fils, si tu t’es porté caution pour ton prochain, si tu as engagé ta main pour un étranger,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 tu es enlacé dans les paroles de ta bouche, tu es pris dans les paroles de ta bouche.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Mon fils, fais donc ceci, et délivre-toi, puisque tu es tombé en la main de ton prochain: va, humilie-toi, et insiste auprès de ton prochain.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Ne permets pas à tes yeux de dormir, ni à tes paupières de sommeiller;
Usagone tulo, usawodzere.
5 dégage-toi, comme la gazelle, de la main [du chasseur], et comme l’oiseau, de la main de l’oiseleur.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Va vers la fourmi, paresseux; regarde ses voies, et sois sage.
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Elle qui n’a ni chef, ni surveillant, ni gouverneur,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 elle prépare en été son pain, elle amasse pendant la moisson sa nourriture.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Jusques à quand, paresseux, resteras-tu couché? Quand te lèveras-tu de ton sommeil?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Un peu de sommeil, un peu d’assoupissement, un peu croiser les mains pour dormir…,
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 et ta pauvreté viendra comme un voyageur, et ton dénuement comme un homme armé.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 Celui qui marche, la perversité dans sa bouche, est un homme de Bélial, un homme inique;
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 il cligne de ses yeux, il parle de ses pieds, il enseigne de ses doigts;
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 il y a des pensées perverses dans son cœur, il machine du mal en tout temps, il sème des querelles.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 C’est pourquoi sa calamité viendra subitement; il sera tout à coup brisé, et il n’y a pas de remède.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 L’Éternel hait ces six choses, et il y en a sept qui sont en abomination à son âme:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 les yeux hautains, la langue fausse, et les mains qui versent le sang innocent,
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 le cœur qui machine des projets d’iniquité, les pieds qui se hâtent de courir au mal,
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 le faux témoin qui profère des mensonges, et celui qui sème des querelles entre des frères.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Mon fils, garde le commandement de ton père, et n’abandonne pas l’enseignement de ta mère;
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 tiens-les continuellement liés sur ton cœur, attache-les à ton cou.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Quand tu marcheras, il te conduira; quand tu dormiras, il te gardera; et quand tu te réveilleras, il s’entretiendra avec toi.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Car le commandement est une lampe et l’enseignement une lumière, et les répréhensions de la discipline sont le chemin de la vie,
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 pour te garder de la mauvaise femme, des flatteries de la langue d’une étrangère.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Ne désire pas sa beauté dans ton cœur, et qu’elle ne te prenne pas par ses paupières;
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 car par la femme prostituée [on en vient] jusqu’à un morceau de pain, et la femme d’autrui chasse après l’âme précieuse.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Un homme prendra-t-il du feu dans son sein sans que ses vêtements brûlent?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Si un homme marche sur des charbons ardents, ses pieds ne seront-ils pas brûlés?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 Ainsi celui qui entre vers la femme de son prochain…, quiconque la touchera ne sera point innocent.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 On ne méprise pas un voleur s’il vole pour satisfaire son âme quand il a faim;
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 et s’il est trouvé, il rendra le septuple, il donnera tous les biens de sa maison.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Celui qui commet adultère avec une femme manque de sens; celui qui le fait détruit son âme:
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 il trouvera plaie et mépris, et son opprobre ne sera pas effacé;
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 car dans l’homme, la jalousie est une fureur, et il n’épargnera pas au jour de la vengeance;
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 il n’acceptera aucune propitiation, et ne se tiendra pas pour satisfait, quand tu multiplierais les présents.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.