< Proverbes 3 >

1 Mon fils, n’oublie pas mon enseignement, et que ton cœur garde mes commandements;
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 car ils t’ajouteront un prolongement de jours, et des années de vie, et la paix.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Que la bonté et la vérité ne t’abandonnent pas; lie-les à ton cou, écris-les sur la tablette de ton cœur,
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 et tu trouveras la faveur et la bonne sagesse aux yeux de Dieu et des hommes.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confie-toi de tout ton cœur à l’Éternel, et ne t’appuie pas sur ton intelligence;
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 dans toutes tes voies connais-le, et il dirigera tes sentiers.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Ne sois pas sage à tes propres yeux; crains l’Éternel et éloigne-toi du mal:
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 ce sera la santé pour ton nombril, et un arrosement pour tes os.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honore l’Éternel de tes biens et des prémices de tout ton revenu;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 et tes greniers se rempliront d’abondance, et tes cuves regorgeront de moût.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Mon fils, ne méprise pas l’instruction de l’Éternel, et n’aie pas en aversion sa réprimande;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 car celui que l’Éternel aime, il le discipline, comme un père le fils auquel il prend plaisir.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Bienheureux l’homme qui trouve la sagesse, et l’homme qui obtient l’intelligence!
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 car son acquisition est meilleure que l’acquisition de l’argent, et son revenu [est meilleur] que l’or fin.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Elle est plus précieuse que les rubis, et aucune des choses auxquelles tu prends plaisir ne l’égale:
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 longueur de jours est dans sa droite, dans sa gauche richesse et honneur;
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 ses voies sont des voies agréables, et tous ses sentiers sont paix.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Elle est un arbre de vie pour ceux qui la saisissent; et qui la tient ferme est rendu bienheureux.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 L’Éternel a fondé la terre par la sagesse, il a établi les cieux par l’intelligence.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Par sa connaissance les abîmes se fendirent, et les nuées distillent la rosée.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Mon fils, que [ces choses] ne s’éloignent point de tes yeux: garde le sain conseil et la réflexion,
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 et ils seront la vie de ton âme et la grâce de ton cou.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Alors tu iras ton chemin en sécurité, et ton pied ne se heurtera point.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Si tu te couches tu n’auras point de crainte; mais tu te coucheras et ton sommeil sera doux.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Ne crains pas la frayeur subite, ni la ruine des méchants quand elle surviendra;
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 car l’Éternel sera ta confiance, et il gardera ton pied d’être pris.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Ne refuse pas le bien à celui à qui il est dû, quand il est au pouvoir de ta main de le faire.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Ne dis pas à ton prochain: Va et reviens, et je te le donnerai demain, quand tu as la chose par-devers toi.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Ne machine pas du mal contre ton prochain, puisqu’il habite en sécurité près de toi.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Ne conteste pas sans sujet avec un homme, s’il ne t’a pas fait de tort.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Ne porte pas envie à un homme violent, et ne choisis aucune de ses voies;
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Car l’Éternel a en abomination le pervers, et son secret est avec les hommes droits.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 La malédiction de l’Éternel est dans la maison du méchant, et il bénit l’habitation des justes.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Certes il se moque des moqueurs, et il donne la grâce aux débonnaires.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Les sages hériteront la gloire, mais la honte est l’élévation des sots.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbes 3 >