< Proverbes 29 >
1 L’homme qui, étant souvent repris, roidit son cou, sera brisé subitement, et il n’y a pas de remède.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Quand les justes se multiplient, le peuple se réjouit; mais quand le méchant gouverne, le peuple gémit.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 L’homme qui aime la sagesse est la joie de son père, mais le compagnon des prostituées dissipera son bien.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Un roi, par le juste jugement, affermit le pays, mais l’homme qui accepte des présents le ruine.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 L’homme qui flatte son prochain étend un filet devant ses pas.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 Dans la transgression de l’homme mauvais, il y a un piège; mais le juste chantera et se réjouira.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Le juste prend connaissance de la cause des pauvres; le méchant ne comprend aucune connaissance.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Les hommes moqueurs mettent en feu une ville, mais les sages détournent la colère.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Un homme sage qui plaide avec un homme insensé, qu’il s’irrite ou qu’il rie, n’a point de repos.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Les hommes de sang haïssent l’homme intègre, mais les hommes droits tiennent à sa vie.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 Le sot met dehors tout son esprit, mais le sage le calme et le retient.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Qu’un gouverneur prête attention à la parole de mensonge, tous ses serviteurs seront méchants.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Le pauvre et l’oppresseur se rencontrent, l’Éternel éclaire les yeux de tous deux.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 Le roi qui juge les pauvres selon la vérité, … son trône sera affermi pour toujours.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 La verge et la répréhension donnent la sagesse, mais le jeune garçon abandonné à lui-même fait honte à sa mère.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Quand les méchants se multiplient, la transgression se multiplie; mais les justes verront leur chute.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Corrige ton fils, et il te donnera du repos et procurera des délices à ton âme.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Quand il n’y a point de vision, le peuple est sans frein; mais bienheureux celui qui garde la loi!
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Un serviteur n’est pas corrigé par des paroles; car il comprend, mais il ne répond pas.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 As-tu vu un homme précipité dans ses paroles? Il y a plus d’espoir pour un sot que pour lui.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Celui qui gâte son serviteur dès sa jeunesse, le verra fils à la fin.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 L’homme colère excite les querelles, et l’homme qui se met en fureur abonde en transgressions.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 L’orgueil d’un homme l’abaisse, mais celui qui est humble d’esprit acquiert la gloire.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Qui partage avec un voleur hait son âme; il entend l’adjuration, et ne déclare pas [la chose].
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 La crainte des hommes tend un piège, mais qui se confie en l’Éternel est élevé dans une haute retraite.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Plusieurs cherchent la face du gouverneur, mais le juste jugement d’un homme vient de l’Éternel.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 L’homme inique est l’abomination des justes, et celui qui est droit dans sa voie, l’abomination du méchant.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.