< Proverbes 22 >

1 Une bonne renommée est préférable à de grandes richesses, et la bonne grâce à l’argent et à l’or.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Le riche et le pauvre se rencontrent: l’Éternel les a tous faits.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 L’homme avisé voit le mal et se cache; mais les simples passent outre et en portent la peine.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 La fin de la débonnaireté, de la crainte de l’Éternel, c’est la richesse, et la gloire, et la vie.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Il y a des épines, des pièges, sur la voie du pervers; celui qui garde son âme s’en éloigne.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Élève le jeune garçon selon la règle de sa voie; même lorsqu’il vieillira, il ne s’en détournera point.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Le riche gouverne les pauvres, et celui qui emprunte est serviteur de l’homme qui prête.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Qui sème l’injustice moissonnera le malheur, et la verge de son courroux prendra fin.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 [Celui qui a] l’œil bienveillant sera béni, car il donne de son pain au pauvre.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Chasse le moqueur, et la querelle s’en ira, et les disputes et la honte cesseront.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Celui qui aime la pureté de cœur a la grâce sur les lèvres, [et] le roi est son ami.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Les yeux de l’Éternel gardent la connaissance, mais il renverse les paroles du perfide.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Le paresseux dit: Il y a un lion là dehors, je serai tué au milieu des rues!
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 La bouche des étrangères est une fosse profonde; celui contre qui l’Éternel est irrité y tombera.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 La folie est liée au cœur du jeune enfant; la verge de la correction l’éloignera de lui.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Celui qui opprime le pauvre, ce sera pour l’enrichir; celui qui donne au riche, ce sera pour le faire tomber dans l’indigence.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Incline ton oreille et écoute les paroles des sages, et applique ton cœur à ma science;
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 car c’est une chose agréable si tu les gardes au-dedans de toi: elles seront disposées ensemble sur tes lèvres.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Afin que ta confiance soit en l’Éternel, je te [les] ai fait connaître à toi, aujourd’hui.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Ne t’ai-je pas écrit des choses excellentes en conseils et en connaissance,
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 pour te faire connaître la sûre norme des paroles de vérité, afin que tu répondes des paroles de vérité à ceux qui t’envoient?
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Ne pille pas le pauvre, parce qu’il est pauvre, et ne foule pas l’affligé à la porte;
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 car l’Éternel prendra en main leur cause, et dépouillera l’âme de ceux qui les dépouillent.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Ne sois pas l’ami de l’homme colère, et n’entre pas chez l’homme violent;
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 de peur que tu n’apprennes ses sentiers, et que tu n’emportes un piège dans ton âme.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Ne sois point parmi ceux qui frappent dans la main, parmi ceux qui se rendent caution pour des dettes:
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 si tu n’avais pas de quoi payer, pourquoi voudrais-tu qu’on prenne ton lit de dessous toi?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Ne recule pas la borne ancienne que tes pères ont faite.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 As-tu vu un homme diligent dans son travail? il se tiendra devant les rois, il ne se tiendra pas devant des gens obscurs.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

< Proverbes 22 >