< Proverbes 20 >

1 Le vin est moqueur, la boisson forte est tumultueuse, et quiconque s’y égare n’est pas sage.
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 La terreur du roi est comme le rugissement d’un jeune lion: qui l’irrite, pèche contre sa propre âme.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 C’est la gloire d’un homme que de s’abstenir des contestations, mais chaque fou s’y engage.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 À cause de l’hiver, le paresseux ne laboure pas; lors de la moisson, il mendiera et n’aura rien.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 Le conseil dans le cœur d’un homme est une eau profonde, et l’homme intelligent y puise.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Nombre d’hommes proclament chacun sa bonté; mais un homme fidèle, qui le trouvera?
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 Le juste marche dans son intégrité; heureux ses fils après lui!
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Le roi siège sur le trône du jugement; il dissipe tout mal par son regard.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Qui dira: J’ai purifié mon cœur, je suis net de mon péché?
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 Poids et poids, épha et épha, sont tous deux en abomination à l’Éternel.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 Même un jeune garçon se fait connaître par ses actions, si sa conduite est pure et si elle est droite.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 Et l’oreille qui entend et l’œil qui voit, l’Éternel les a faits tous les deux.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 N’aime pas le sommeil, de peur que tu ne deviennes pauvre; ouvre tes yeux, [et] rassasie-toi de pain.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 Mauvais, mauvais! dit l’acheteur; puis il s’en va et se vante.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 Il y a de l’or et beaucoup de rubis; mais les lèvres de la connaissance sont un vase précieux.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Prends son vêtement, car il a cautionné autrui; et prends de lui un gage, à cause des étrangers.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Le pain du mensonge est agréable à l’homme; mais ensuite, sa bouche est pleine de gravier.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 Les plans s’affermissent par le conseil; et fais la guerre avec prudence.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Qui va rapportant révèle le secret; aussi ne te mêle pas avec le bavard.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 Qui maudit son père et sa mère, – sa lampe s’éteindra au sein des ténèbres.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 L’héritage acquis avec hâte au commencement, ne sera pas béni à la fin.
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Ne dis point: Je rendrai le mal. Attends-toi à l’Éternel, et il te sauvera.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Poids et poids est en abomination à l’Éternel, et la fausse balance n’est pas une chose bonne.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 Les pas de l’homme viennent de l’Éternel; et comment un homme comprendrait-il sa propre voie?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 C’est un piège pour l’homme que de dire précipitamment: Chose sainte! – et, après des vœux, d’examiner.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Un roi sage disperse les méchants, et ramène sur eux la roue.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 L’esprit de l’homme est une lampe de l’Éternel; il sonde toutes les profondeurs du cœur.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 La bonté et la vérité préservent le roi, et il soutient son trône par la bonté.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 L’ornement des jeunes gens, c’est leur force; et la gloire des vieillards, ce sont les cheveux blancs.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Les meurtrissures [et] les plaies nettoient le mal, et les coups, les profondeurs de l’âme.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

< Proverbes 20 >