< Nombres 8 >

1 Et l’Éternel parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Parle à Aaron et dis-lui: Quand tu allumeras les lampes, les sept lampes éclaireront sur le devant, vis-à-vis du chandelier.
“Yankhula ndi Aaroni kuti pamene uyimika nyale zisanu ndi ziwiri, nyalezo ziziyaka kutsogolo kwa choyikapo nyale.”
3 Et Aaron fit ainsi; il alluma les lampes [pour éclairer] sur le devant, vis-à-vis du chandelier, comme l’Éternel l’avait commandé à Moïse.
Aaroni anachitadi zomwezo. Anayimika nyale ndi kuziyangʼanitsa kumene kunali choyikapo nyale monga Yehova analamulira Mose.
4 Et le chandelier était fait ainsi: il était d’or battu; depuis son pied jusqu’à ses fleurs, il était [d’or] battu. Selon la forme que l’Éternel avait montrée à Moïse, ainsi il avait fait le chandelier.
Choyikapo nyalecho chinapangidwa motere: chinasulidwa kuchokera ku golide, kuyambira pa tsinde pake mpaka ku maluwa ake. Choyikapo nyalecho chinapangidwa monga momwe Yehova anaonetsera Mose.
5 Et l’Éternel parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
6 Prends les Lévites du milieu des fils d’Israël, et purifie-les.
“Tenga Alevi pakati pa Aisraeli ndipo uwayeretse.
7 Et tu leur feras ainsi pour les purifier: tu feras aspersion sur eux de l’eau de purification du péché; et ils feront passer le rasoir sur toute leur chair, et ils laveront leurs vêtements, et se purifieront.
Powayeretsa uchite izi: uwawaze madzi oyeretsa ndipo amete thupi lawo lonse ndi kuchapa zovala zawo kuti adziyeretse.
8 Et ils prendront un jeune taureau, et son offrande de gâteau de fleur de farine pétrie à l’huile; et tu prendras un second jeune taureau, pour sacrifice pour le péché.
Atenge ngʼombe yayimuna yayingʼono ndi chopereka cha chakudya cha ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Atengenso ngʼombe ina yayimuna, yayingʼono, ya chopereka chopepesera machimo.
9 Et tu feras approcher les Lévites devant la tente d’assignation, et tu réuniras toute l’assemblée des fils d’Israël;
Ubwere nawo Aleviwo kutsogolo kwa tenti ya msonkhano ndipo usonkhanitse gulu la Aisraeli.
10 et tu feras approcher les Lévites devant l’Éternel, et les fils d’Israël poseront leurs mains sur les Lévites;
Ubwere nawo pamaso pa Yehova, ndipo Aisraeli asanjike manja awo pa iwo.
11 et Aaron offrira les Lévites en offrande tournoyée devant l’Éternel, de la part des fils d’Israël, et ils seront employés au service de l’Éternel.
Aaroni apereke Alevi aja pamaso pa Yehova ngati chopereka choweyula kuchokera kwa Aisraeli kuti akhale okonzeka kugwira ntchito ya Yehova.
12 Et les Lévites poseront leurs mains sur la tête des taureaux; et tu offriras l’un en sacrifice pour le péché, et l’autre en holocauste à l’Éternel, afin de faire propitiation pour les Lévites.
“Alevi akatsiriza kusanjika manja awo pa mitu ya ngʼombe zazimuna, imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza ya kwa Yehova, kupepesera machimo a Alevi.
13 Et tu feras tenir les Lévites devant Aaron et devant ses fils, et tu les offriras en offrande tournoyée à l’Éternel.
Uyimiritse Aleviwo pamaso pa Aaroni ndi ana ake aamuna ndipo uwapereke ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.
14 Et tu sépareras les Lévites du milieu des fils d’Israël, et les Lévites seront à moi.
Pochita zimenezi mudzapatula Alevi pakati pa Aisraeli ndipo Aleviwo adzakhala anga.
15 – Après cela les Lévites viendront pour faire le service de la tente d’assignation, et tu les purifieras, et tu les offriras en offrande tournoyée;
“Utatha kuyeretsa ndi kupereka Aleviwo monga nsembe yoweyula, apite kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano.
16 car ils me sont entièrement donnés du milieu des fils d’Israël: je les ai pris pour moi à la place de tous ceux qui ouvrent la matrice, de tous les premiers-nés d’entre les fils d’Israël.
Iwo ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwathunthu kwa Ine. Ndawatenga kuti akhale anga mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa wa Mwisraeli aliyense wamkazi.
17 Car tout premier-né parmi les fils d’Israël est à moi, tant les hommes que les bêtes; je me les suis sanctifiés le jour où je frappai tout premier-né dans le pays d’Égypte.
Mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa mu Israeli, kaya wa munthu kapena wa ziweto, ndi wanga. Pamene ndinakantha ana oyamba kubadwa ku Igupto, ndinawapatulira kwa Ine mwini.
18 Et j’ai pris les Lévites à la place de tous les premiers-nés parmi les fils d’Israël.
Ndipo ndatenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna onse oyamba kubadwa mu Israeli.
19 Et j’ai donné les Lévites en don à Aaron et à ses fils, du milieu des fils d’Israël, pour s’employer au service des fils d’Israël à la tente d’assignation, et pour faire propitiation pour les fils d’Israël, afin qu’il n’y ait pas de plaie au milieu des fils d’Israël quand les fils d’Israël s’approcheraient du lieu saint.
Mwa Aisraeli onse, ndapereka Alevi kuti akhale mphatso kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kugwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti azikapereka nsembe yopepesera machimo, kuti mliri usadzaphe Aisraeli pamene ayandikira ku malo wopatulika.”
20 – Et Moïse et Aaron, et toute l’assemblée des fils d’Israël, firent à l’égard des Lévites tout ce que l’Éternel avait commandé à Moïse touchant les Lévites; les fils d’Israël firent ainsi à leur égard.
Mose, Aaroni pamodzi ndi gulu lonse la Israeli anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
21 Et les Lévites se purifièrent, et lavèrent leurs vêtements; et Aaron les offrit en offrande tournoyée devant l’Éternel; et Aaron fit propitiation pour eux, pour les purifier.
Alevi anadziyeretsa ndi kuchapa zovala zawo. Kenaka Aaroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe yopepesera machimo yowayeretsa.
22 Et après cela, les Lévites vinrent pour faire leur service à la tente d’assignation, devant Aaron et devant ses fils. Comme l’Éternel avait commandé à Moïse touchant les Lévites, ainsi on fit à leur égard.
Zitatha zimenezi, Alevi anapita kukagwira ntchito yawo ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Anachita kwa Alevi monga momwe Yehova analamulira Mose.
23 Et l’Éternel parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
24 C’est ici ce qui concerne les Lévites: Depuis l’âge de 25 ans et au-dessus, [le Lévite] entrera en service pour être employé à la tente d’assignation;
“Ntchito za Alevi ndi izi: Amuna a zaka 24 kapena kuposera pamenepa ndiye azibwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
25 et depuis l’âge de 50 ans, il se retirera du labeur du service, et ne servira plus;
Koma akakwana zaka makumi asanu, apume pa ntchito yawo ya tsiku ndi tsiku ndi kulekeratu kugwira ntchitoyo.
26 et il s’emploiera avec ses frères à la tente d’assignation, pour garder ce qui doit être gardé, mais il ne fera pas de service. Tu feras ainsi à l’égard des Lévites touchant leurs charges.
Atha kuthandiza abale awo kugwira ntchito za ku tenti ya msonkhano, koma iwowo asamagwire ntchitoyo. Mmenemu ndimo ugawire ntchito yomwe azigwira Alevi.”

< Nombres 8 >