< Nombres 7 >

1 Et il arriva, le jour où Moïse eut achevé de dresser le tabernacle, et qu’il l’eut oint et sanctifié avec tous ses ustensiles, et l’autel avec tous ses ustensiles, et qu’il les eut oints et sanctifiés,
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 que les princes d’Israël, chefs de leurs maisons de pères, princes des tribus, qui avaient été préposés sur ceux qui furent dénombrés, présentèrent [leur offrande].
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 Ils amenèrent leur offrande devant l’Éternel: six chariots couverts et douze bœufs, un chariot pour deux princes, et un bœuf pour un [prince]; et ils les présentèrent devant le tabernacle.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 Et l’Éternel parla à Moïse, disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 Prends d’eux [ces choses], et elles seront employées au service de la tente d’assignation, et tu les donneras aux Lévites, à chacun en proportion de son service.
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 Et Moïse prit les chariots et les bœufs, et les donna aux Lévites.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Il donna deux chariots et quatre bœufs aux fils de Guershon, en proportion de leur service;
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 et il donna quatre chariots et huit bœufs aux fils de Merari, en proportion de leur service, – sous la main d’Ithamar, fils d’Aaron, le sacrificateur.
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 Et il n’en donna pas aux fils de Kehath, car le service du lieu saint leur appartenait: ils portaient sur l’épaule.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 Et les princes présentèrent [leur offrande pour] la dédicace de l’autel, le jour où il fut oint: les princes présentèrent leur offrande devant l’autel.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 Et l’Éternel dit à Moïse: Ils présenteront, un prince un jour, et un prince l’autre jour, leur offrande pour la dédicace de l’autel.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 Et celui qui présenta son offrande le premier jour, fut Nakhshon, fils d’Amminadab, de la tribu de Juda;
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 et son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande de Nakhshon, fils d’Amminadab.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 Le second jour, Nethaneël, fils de Tsuar, prince d’Issacar, présenta [son offrande].
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 Il présenta son offrande: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande de Nethaneël, fils de Tsuar.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 Le troisième jour, le prince des fils de Zabulon, Éliab, fils de Hélon.
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Éliab, fils de Hélon.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 Le quatrième jour, le prince des fils de Ruben, Élitsur, fils de Shedéur.
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Élitsur, fils de Shedéur.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 Le cinquième jour, le prince des fils de Siméon, Shelumiel, fils de Tsurishaddaï.
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande de Shelumiel, fils de Tsurishaddaï.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 Le sixième jour, le prince des fils de Gad, Éliasaph, fils de Dehuel.
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Éliasaph, fils de Dehuel.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 Le septième jour, le prince des fils d’Éphraïm, Élishama, fils d’Ammihud.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Élishama, fils d’Ammihud.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 Le huitième jour, le prince des fils de Manassé, Gameliel, fils de Pedahtsur.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande de Gameliel, fils de Pedahtsur.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 Le neuvième jour, le prince des fils de Benjamin, Abidan, fils de Guidhoni.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Abidan, fils de Guidhoni.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 Le dixième jour, le prince des fils de Dan, Akhiézer, fils d’Ammishaddaï.
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Akhiézer, fils d’Ammishaddaï.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 Le onzième jour, le prince des fils d’Aser, Paghiel, fils d’Ocran.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande de Paghiel, fils d’Ocran.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 Le douzième jour, le prince des fils de Nephthali, Akhira, fils d’Énan.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 Son offrande fut: un plat d’argent du poids de 130 [sicles], un bassin d’argent de 70 sicles, selon le sicle du sanctuaire, tous deux pleins de fleur de farine pétrie à l’huile, pour une offrande de gâteau;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 une coupe d’or de dix [sicles], pleine d’encens;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 un jeune taureau, un bélier, un agneau âgé d’un an, pour l’holocauste;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 un bouc, en sacrifice pour le péché;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 et, pour le sacrifice de prospérités, deux taureaux, cinq béliers, cinq boucs, cinq agneaux âgés d’un an. Telle fut l’offrande d’Akhira, fils d’Énan.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 Telle fut, de la part des princes d’Israël, [l’offrande pour] la dédicace de l’autel, au jour où il fut oint: douze plats d’argent, douze bassins d’argent, douze coupes d’or;
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 chaque plat d’argent était de 130 [sicles], et chaque bassin de 70: tout l’argent des vases fut de 2 400 [sicles], selon le sicle du sanctuaire.
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 Douze coupes d’or, pleines d’encens, chacune de dix [sicles], selon le sicle du sanctuaire: tout l’or des coupes, de 120 [sicles].
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 Tout le bétail pour l’holocauste fut: douze taureaux, douze béliers, douze agneaux âgés d’un an, et leurs offrandes de gâteau; et douze boucs, en sacrifice pour le péché.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 Et tout le bétail pour le sacrifice de prospérités fut: 24 taureaux, 60 béliers, 60 boucs, 60 agneaux âgés d’un an. Telle fut [l’offrande pour] la dédicace de l’autel, après qu’il fut oint.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Et quand Moïse entrait dans la tente d’assignation pour parler avec Lui, il entendait la voix qui lui parlait de dessus le propitiatoire qui était sur l’arche du témoignage, d’entre les deux chérubins; et il Lui parlait.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< Nombres 7 >