< Nombres 29 >
1 Et au septième mois, le premier [jour] du mois, vous aurez une sainte convocation; vous ne ferez aucune œuvre de service; ce sera pour vous le jour du son éclatant [des trompettes].
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Et vous offrirez un holocauste en odeur agréable à l’Éternel, un jeune taureau, un bélier, sept agneaux âgés d’un an, sans défaut;
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 et leur offrande de gâteau de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 et un dixième pour un agneau, pour les sept agneaux;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 et un bouc en sacrifice pour le péché, afin de faire propitiation pour vous,
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 – outre l’holocauste du mois, et son gâteau, et l’holocauste continuel et son gâteau, et leurs libations, selon leur ordonnance, en odeur agréable, un sacrifice par feu à l’Éternel.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Et le dixième [jour] de ce septième mois, vous aurez une sainte convocation, et vous affligerez vos âmes; vous ne ferez aucune œuvre.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Et vous présenterez à l’Éternel un holocauste d’odeur agréable, un jeune taureau, un bélier, sept agneaux âgés d’un an (vous les prendrez sans défaut);
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 et leur offrande de gâteau de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 un dixième par agneau, pour les sept agneaux;
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 [et] un bouc en sacrifice pour le péché, – outre le sacrifice de péché des propitiations, et l’holocauste continuel et son gâteau, et leurs libations.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Et le quinzième jour du septième mois, vous aurez une sainte convocation; vous ne ferez aucune œuvre de service, et vous célébrerez une fête à l’Éternel pendant sept jours.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Et vous présenterez un holocauste, un sacrifice par feu d’odeur agréable à l’Éternel, 13 jeunes taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an (ils seront sans défaut);
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 et leur offrande de gâteau de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes par taureau, pour les 13 taureaux, deux dixièmes par bélier, pour les deux béliers,
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 et un dixième par agneau, pour les 14 agneaux;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel, son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Et le second jour, [vous présenterez] douze jeunes taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 et leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel et son gâteau, et leurs libations.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Et le troisième jour, onze taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 et leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel et son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Et le quatrième jour, dix taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel, son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Et le cinquième jour, neuf taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 et leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel et son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Et le sixième jour, huit taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 et leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel, son gâteau et ses libations.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Et le septième jour, sept taureaux, deux béliers, 14 agneaux âgés d’un an, sans défaut;
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 et leur offrande de gâteau et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon leur ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel, son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Le huitième jour, vous aurez une fête solennelle; vous ne ferez aucune œuvre de service.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Et vous présenterez un holocauste, un sacrifice par feu d’odeur agréable à l’Éternel, un taureau, un bélier, sept agneaux âgés d’un an, sans défaut;
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 leur offrande de gâteau et leurs libations pour le taureau, pour le bélier, et pour les agneaux, d’après leur nombre, selon l’ordonnance;
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 et un bouc en sacrifice pour le péché, – outre l’holocauste continuel et son gâteau et sa libation.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Vous offrirez ces choses à l’Éternel dans vos jours solennels, outre vos vœux et vos offrandes volontaires en vos holocaustes et vos offrandes de gâteau, et vos libations, et vos sacrifices de prospérités.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Et Moïse parla aux fils d’Israël selon tout ce que l’Éternel avait commandé à Moïse.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.