< Josué 13 >

1 Et Josué était vieux, avancé en âge, et l’Éternel lui dit: Tu es devenu vieux, tu avances en âge, et il reste un très grand pays à posséder.
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 C’est ici le pays qui reste: tous les districts des Philistins et tous les Gueshuriens,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 depuis le Shikhor qui est devant l’Égypte, jusqu’à la frontière d’Ékron, vers le nord; il est réputé appartenir aux Cananéens: cinq princes des Philistins, celui de Gaza, et celui d’Asdod, celui d’Askalon, celui de Gath, et celui d’Ékron, et les Avviens;
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 au sud, tout le pays des Cananéens, et Méara, qui est aux Sidoniens, jusqu’à Aphek, jusqu’à la frontière de l’Amoréen;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 et le pays des Guibliens, et tout le Liban, vers le soleil levant, depuis Baal-Gad, au pied de la montagne de l’Hermon, jusqu’à l’entrée de Hamath;
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 tous les habitants de la montagne, depuis le Liban jusqu’à Misrephoth-Maïm, tous les Sidoniens. Moi, je les déposséderai devant les fils d’Israël. Seulement, répartis par le sort [ce pays] en héritage à Israël, comme je te l’ai commandé.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Et maintenant, distribue ce pays en héritage aux neuf tribus, et à la demi-tribu de Manassé.
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Avec l’autre moitié de Manassé, les Rubénites et les Gadites ont reçu leur héritage, que Moïse leur a donné au-delà du Jourdain, vers le levant, selon ce que Moïse, serviteur de l’Éternel, leur a donné,
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 depuis Aroër, qui est sur le bord du torrent de l’Arnon, et la ville qui est au milieu du torrent, et tout le plateau de Médeba, jusqu’à Dibon;
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 et toutes les villes de Sihon, roi des Amoréens, qui régnait à Hesbon, jusqu’à la frontière des fils d’Ammon;
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 et Galaad, et les confins des Gueshuriens et des Maacathiens, et toute la montagne de l’Hermon; et tout Basan, jusqu’à Salca,
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 tout le royaume d’Og, en Basan, qui régnait à Ashtaroth et à Édréhi; (il était demeuré du reste des Rephaïm); et Moïse les frappa et les déposséda.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 – Mais les fils d’Israël ne dépossédèrent pas les Gueshuriens et les Maacathiens; et Gueshur et Maaca habitent au milieu d’Israël jusqu’à ce jour.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 À la tribu de Lévi seule il ne donna point d’héritage; les sacrifices de l’Éternel, le Dieu d’Israël, faits par feu, c’est là son héritage, comme il le lui avait dit.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Et Moïse donna [une part] à la tribu des fils de Ruben, selon leurs familles.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Et leur territoire était depuis Aroër, qui est sur le bord du torrent de l’Arnon, et la ville qui est au milieu du torrent, et tout le plateau près de Médeba;
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hesbon et toutes ses villes, qui étaient sur le plateau: Dibon, et Bamoth-Baal, et Beth-Baal-Méon,
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 et Jahtsa, et Kedémoth, et Méphaath,
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 et Kiriathaïm, et Sibma, et Tséreth-Shakhar dans la montagne de la vallée,
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 et Beth-Péor, et les pentes du Pisga, et Beth-Jeshimoth,
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 toutes les villes du plateau et tout le royaume de Sihon, roi des Amoréens, qui régnait à Hesbon, que Moïse frappa, lui et les princes de Madian: Évi, et Rékem, et Tsur, et Hur, et Réba, seigneurs de Sihon, habitants du pays.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 Et les fils d’Israël tuèrent par l’épée Balaam, fils de Béor, le devin, avec les autres qui furent tués.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Et la frontière des fils de Ruben fut le Jourdain et [sa] rive. Ce fut là l’héritage des fils de Ruben, selon leurs familles: les villes et leurs hameaux.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Et Moïse donna [une part] à la tribu de Gad, aux fils de Gad, selon leurs familles.
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Et leur territoire était Jahzer, et toutes les villes de Galaad, et la moitié du pays des fils d’Ammon, jusqu’à Aroër, qui est vis-à-vis de Rabba;
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 et depuis Hesbon jusqu’à Ramath-Mitspé et Betonim, et depuis Mahanaïm jusqu’à la frontière de Debir;
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 et, dans la vallée, Beth-Haram, et Beth-Nimra, et Succoth, et Tsaphon, le reste du royaume de Sihon, roi de Hesbon, le Jourdain et [sa] rive, jusqu’au bout de la mer de Kinnéreth, au-delà du Jourdain, vers le levant.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Ce fut là l’héritage des fils de Gad, selon leurs familles: les villes et leurs hameaux.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Et Moïse donna [une part] à la demi-tribu de Manassé; et pour la demi-tribu des fils de Manassé, selon leurs familles,
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 leur territoire était depuis Mahanaïm: tout Basan, tout le royaume d’Og, roi de Basan, et tous les bourgs de Jaïr, qui sont en Basan, 60 villes;
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 et la moitié de Galaad, et Ashtaroth, et Édréhi, villes du royaume d’Og, en Basan, furent aux fils de Makir, fils de Manassé, à la moitié des fils de Makir, selon leurs familles.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 C’est là ce que Moïse distribua en héritage dans les plaines de Moab, au-delà du Jourdain de Jéricho, vers le levant.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Mais Moïse ne donna point d’héritage à la tribu de Lévi; l’Éternel, le Dieu d’Israël, était leur héritage, comme il le leur avait dit.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Josué 13 >