< Job 40 >

1 Et l’Éternel répondit à Job et dit:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Celui qui conteste avec le Tout-puissant l’instruira-t-il? Celui qui reprend Dieu, qu’il réponde à cela!
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Et Job répondit à l’Éternel et dit:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Voici, je suis une créature de rien, que te répliquerai-je? Je mettrai ma main sur ma bouche.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 J’ai parlé une fois, et je ne répondrai plus; et deux fois, et je n’ajouterai rien.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Et l’Éternel répondit à Job du milieu du tourbillon et dit:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Ceins tes reins comme un homme; je t’interrogerai, et tu m’instruiras!
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Veux-tu donc anéantir mon jugement? Me démontreras-tu inique afin de te justifier?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 As-tu un bras comme Dieu, et tonneras-tu de ta voix comme lui?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Pare-toi, je te prie, de grandeur et de magnificence; revêts-toi de majesté et de gloire!
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Répands les fureurs de ta colère, et regarde tout ce qui s’élève et abaisse-le;
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Regarde tout ce qui s’élève [et] humilie-le, et écrase sur place les méchants;
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Cache-les ensemble dans la poussière, lie leurs faces dans un lieu caché:
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Alors moi aussi je te célébrerai, parce que ta droite te sauve!
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Vois le béhémoth, que j’ai fait avec toi: il mange l’herbe comme le bœuf.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Regarde donc: sa force est dans ses reins, et sa puissance dans les muscles de son ventre.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Il courbe sa queue comme un cèdre; les nerfs de sa cuisse sont entrelacés;
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Ses os sont des tubes d’airain, ses membres sont des barres de fer!
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Il est la première des voies de Dieu: celui qui l’a fait lui a fourni son épée.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Car les montagnes lui apportent [sa] pâture, là où se jouent toutes les bêtes des champs.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Il se couche sous les lotus dans une retraite de roseaux et de marécages;
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Les lotus le couvrent de leur ombre, les saules de la rivière l’environnent.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Voici, que le fleuve déborde avec violence, il ne se précipite pas; il est plein d’assurance si un Jourdain se jette contre sa gueule.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Le prendra-t-on en face? Lui percera-t-on le nez dans une trappe?
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?

< Job 40 >