< Job 4 >

1 Et Éliphaz, le Thémanite, répondit et dit:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Si nous essayons de t’adresser une parole, en seras-tu irrité? Mais qui pourrait se retenir de parler?
“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe? Koma ndani angakhale chete wosayankhula?
3 Voici, tu en as enseigné beaucoup, et tu as fortifié les mains languissantes;
Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri, momwe walimbitsira anthu ofowoka.
4 Tes paroles ont tenu droit celui qui chancelait, et tu as affermi les genoux qui ployaient;
Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa; unachirikiza anthu wotha mphamvu.
5 Mais maintenant [le malheur] est venu sur toi, et tu es irrité; il t’atteint, et tu es troublé.
Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima, zakukhudza ndipo uli ndi mantha.
6 Ta crainte [de Dieu] n’est-elle pas ta confiance, et l’intégrité de tes voies, ton espérance?
Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako? Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?
7 Souviens-toi, je te prie, qui a péri étant innocent? et où les hommes droits ont-ils été détruits?
“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse? Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?
8 Selon ce que j’ai vu, ceux qui labourent l’iniquité et qui sèment la misère, la moissonnent.
Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa, ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.
9 Ils périssent par le souffle de Dieu, et sont consumés par le souffle de ses narines.
Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu; amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.
10 Le rugissement du lion et la voix du [lion] rugissant [sont étouffés], et les dents des jeunes lions sont brisées;
Mikango imabangula ndi kulira, komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.
11 Le lion fort périt faute de proie, et les petits de la lionne sont dispersés.
Mkango umafa chifukwa chosowa nyama, ndipo ana amkango amamwazikana.
12 Une parole vint à moi secrètement, et mon oreille en saisit la susurration,
“Mawu anabwera kwa ine mwamseri, makutu anga anamva kunongʼona kwake.
13 Au milieu des pensées que font naître les visions de la nuit, quand un sommeil profond tombe sur les hommes;
Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku, nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,
14 La frayeur vint sur moi, et le frisson, et elle fit trembler la multitude de mes os;
ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.
15 Et un esprit passa devant moi: les cheveux de ma chair se dressèrent.
Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga, ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.
16 Il se tint là; je ne reconnus pas son apparence: une forme était devant mes yeux. J’entendis un léger murmure et une voix:
Chinthucho chinayimirira koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani. Chinthu chinayima patsogolo panga, kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,
17 Un mortel sera-t-il plus juste que Dieu, l’homme sera-t-il plus pur que celui qui l’a fait?
‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu? Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?
18 Voici, il ne se fie pas à ses serviteurs, et ses anges il les charge de folie;
Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe, ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,
19 Combien plus à ceux qui habitent dans des maisons d’argile dont le fondement est dans la poussière, qui sont écrasés comme la teigne!
nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi, amene maziko awo ndi fumbi, amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!
20 Du matin au soir, ils sont frappés; ils périssent pour toujours sans qu’on y fasse attention.
Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa; mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.
21 Leurs cordes ne leur sont-elles pas arrachées? Ils meurent, et sans sagesse.
Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu, kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

< Job 4 >