< Job 34 >

1 Et Élihu reprit la parole et dit:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Sages, écoutez mes paroles, et vous qui avez de la connaissance, prêtez-moi l’oreille;
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Car l’oreille éprouve les discours, comme le palais goûte les aliments.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Choisissons pour nous ce qui est juste, et reconnaissons entre nous ce qui est bon.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Car Job a dit: Je suis juste, et Dieu a écarté mon droit;
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Mentirai-je contre ma droiture? ma blessure est incurable, sans qu’il y ait de transgression.
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Qui est l’homme qui soit comme Job? Il boit la moquerie comme l’eau;
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Il marche dans la compagnie des ouvriers d’iniquité, et il chemine avec les hommes méchants.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Car il a dit: Il ne profite de rien à l’homme de trouver son plaisir en Dieu.
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 C’est pourquoi, hommes de sens, écoutez-moi: Loin de Dieu la méchanceté, et loin du Tout-puissant l’iniquité!
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Car il rendra à l’homme ce qu’il aura fait, et il fera trouver à chacun selon sa voie.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Certainement Dieu n’agit pas injustement, et le Tout-puissant ne pervertit pas le droit.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Qui a confié la terre à ses soins, et qui a placé le monde entier [sous lui]?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 S’il ne pensait qu’à lui-même et retirait à lui son esprit et son souffle,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 Toute chair expirerait ensemble et l’homme retournerait à la poussière.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Si [tu as] de l’intelligence, écoute ceci; prête l’oreille à la voix de mes paroles.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Celui qui hait la justice gouvernera-t-il donc? Et condamneras-tu le juste par excellence?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Dira-t-on Bélial, au roi? – Méchants, aux nobles?
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 [Combien moins] à celui qui ne fait pas acception de la personne des princes, et qui n’a pas égard au riche plutôt qu’au pauvre; car ils sont tous l’œuvre de ses mains.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 Ils mourront en un moment; au milieu de la nuit les peuples chancellent et s’en vont, et les puissants sont retirés sans main.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 Car ses yeux sont sur les voies de l’homme, et il voit tous ses pas.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Il n’y a pas de ténèbres, il n’y a pas d’ombre de la mort, où puissent se cacher les ouvriers d’iniquité.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Car il ne pense pas longtemps à un homme pour le faire venir devant Dieu en jugement.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Il brise les puissants, sans examen, et il fait que d’autres se tiennent à leur place;
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 En effet il connaît leurs œuvres: il les renverse de nuit, et ils sont écrasés.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Il les frappe comme des méchants dans le lieu où ils sont en vue,
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Parce qu’ils se sont retirés de lui, et qu’ils n’ont pas considéré toutes ses voies,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Pour faire monter vers lui le cri du pauvre, en sorte qu’il entende le cri des malheureux.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Quand il donne la tranquillité, qui troublera? Il cache sa face, et qui le verra? [Il fait] ainsi, soit à une nation, soit à un homme,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 Pour empêcher l’homme impie de régner, pour écarter du peuple les pièges.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Car a-t-il [jamais] dit à Dieu: Je porte ma peine, je ne ferai plus de mal;
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Ce que je ne vois pas, montre-le-moi; si j’ai commis l’iniquité, je ne le referai pas?
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Rétribuera-t-il selon tes pensées? car tu as rejeté [son jugement], car toi, tu as choisi, et non pas moi; ce que tu sais, dis-le donc.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Les hommes de sens me diront, et un homme sage qui m’écoute:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 Job n’a pas parlé avec connaissance, et ses paroles ne sont pas intelligentes;
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Je voudrais que Job soit éprouvé jusqu’au bout, parce qu’il a répondu à la manière des hommes iniques;
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Car il a ajouté à son péché la transgression; il bat des mains parmi nous, et multiplie ses paroles contre Dieu.
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >