< Job 33 >

1 Mais toutefois, Job, je te prie, écoute ce que je dis, et prête l’oreille à toutes mes paroles.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Voici, j’ai ouvert ma bouche, ma langue parle dans mon palais.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Mes paroles seront selon la droiture de mon cœur, et ce que je sais mes lèvres le diront avec pureté.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 L’Esprit de Dieu m’a fait, et le souffle du Tout-puissant m’a donné la vie.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Si tu le peux, réponds-moi; arrange [des paroles] devant moi, tiens-toi là!
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Voici, je suis comme toi quant à Dieu, je suis fait d’argile, moi aussi.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Voici, ma terreur ne te troublera pas, et mon poids ne t’accablera pas.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Certainement tu as dit à mes propres oreilles, et j’ai entendu le son de [tes] discours:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Moi, je suis net, sans transgression; je suis pur, et il n’y a pas d’iniquité en moi;
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Voici, il trouve des occasions d’inimitié contre moi, il me considère comme son ennemi;
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Il a mis mes pieds dans les ceps, il observe toutes mes voies.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Voici, je te répondrai qu’en cela tu n’as pas été juste, car Dieu est plus grand que l’homme.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Pourquoi contestes-tu avec lui? car d’aucune de ses actions il ne rend compte.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Car Dieu parle une fois, et deux fois – [et] l’on n’y prend pas garde –
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Dans un songe, dans une vision de nuit, quand un profond sommeil tombe sur les hommes, quand ils dorment sur leurs lits:
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Alors il ouvre l’oreille aux hommes et scelle l’instruction qu’il leur donne,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Pour détourner l’homme de ce qu’il fait; et il cache l’orgueil à l’homme;
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 Il préserve son âme de la fosse, et sa vie de se jeter sur l’épée.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Il est châtié aussi sur son lit par la douleur, et la lutte de ses os est continuelle,
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Et sa vie prend en dégoût le pain, et son âme l’aliment qu’il aimait;
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Sa chair est consumée et ne se voit plus, et ses os, qu’on ne voyait pas, sont mis à nu;
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Et son âme s’approche de la fosse, et sa vie, de ceux qui font mourir.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 S’il y a pour lui un messager, un interprète, un entre mille, pour montrer à l’homme ce qui, pour lui, est la droiture,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Il lui fera grâce, et il dira: Délivre-le pour qu’il ne descende pas dans la fosse: j’ai trouvé une propitiation.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 [Alors] sa chair aura plus de fraîcheur que dans l’enfance; il reviendra aux jours de sa jeunesse;
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Il suppliera Dieu, et [Dieu] l’aura pour agréable; et il verra sa face avec des chants de triomphe, et [Dieu] rendra à l’homme sa justice.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Il chantera devant les hommes, et dira: J’ai péché et j’ai perverti la droiture, et il ne me l’a pas rendu;
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Il a délivré mon âme pour qu’elle n’aille pas dans la fosse, et ma vie verra la lumière.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Voilà, Dieu opère toutes ces choses deux fois, trois fois, avec l’homme,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Pour détourner son âme de la fosse, pour qu’il soit illuminé de la lumière des vivants.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Sois attentif, Job, écoute-moi; tais-toi, et moi je parlerai.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 S’il y a quelque chose à dire, réponds-moi; parle, car je désire que tu sois trouvé juste;
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Sinon, écoute-moi; tais-toi, et je t’enseignerai la sagesse.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >