< Job 27 >

1 Et Job reprit son discours sentencieux et dit:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Dieu qui a écarté mon droit, le Tout-puissant qui met l’amertume dans mon âme, est vivant:
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 Tant que mon souffle est en moi et l’esprit de Dieu dans mes narines,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Mes lèvres ne diront pas d’iniquité, et ma langue ne prononcera pas de fausseté.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Loin de moi que je vous justifie! Jusqu’à ce que j’expire, je ne lâcherai pas ma perfection;
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Je tiendrai ferme ma justice et je n’en ferai pas abandon; mon cœur ne me reproche aucun de mes jours.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Que mon ennemi soit comme le méchant, et celui qui s’élève contre moi comme l’inique!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Car quelle est l’espérance de l’impie quand [Dieu le] retranche, quand Dieu retire son âme?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Dieu entendra-t-il son cri quand la détresse viendra sur lui?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Trouvera-t-il ses délices dans le Tout-puissant? Invoquera-t-il Dieu en tout temps?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Je vous enseignerai comment Dieu agit, je ne cacherai pas ce qui est par-devers le Tout-puissant.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Voici, vous-mêmes, vous l’avez tous vu: et pourquoi entretenez-vous ces vaines pensées?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Voici quelle est, par-devers Dieu, la part de l’homme méchant et l’héritage que les violents reçoivent du Tout-puissant:
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Si ses fils se multiplient, c’est pour l’épée, et ses descendants ne sont pas rassasiés de pain.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Ceux qui restent après lui seront enterrés dans la mort, et ses veuves ne pleureront pas.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 S’il entasse l’argent comme la poussière et se prépare des vêtements comme de la boue,
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 Il se les prépare, mais le juste s’en vêtira; et l’argent, c’est l’innocent qui se le partagera.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Il a bâti sa maison comme la teigne, comme une cabane que fait celui qui garde [les vignes].
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Il se couche riche, et il ne le refera pas; il ouvre ses yeux, et il n’est plus.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Les frayeurs le surprennent comme des eaux; l’ouragan l’emporte de nuit;
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Le vent d’orient l’enlève, et il s’en va, et dans un tourbillon il l’emporte de son lieu.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 [Dieu] lance [ses dards] sur lui et ne l’épargne pas; il voudrait fuir loin de sa main.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 On battra des mains sur lui, et on le chassera de son lieu avec des sifflements.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< Job 27 >