< Job 20 >

1 Et Tsophar, le Naamathite, répondit et dit:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 C’est pourquoi mes pensées m’inspirent une réponse, et à cause de ceci l’ardeur de mon esprit [agit] en moi:
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 J’entends une réprimande qui me couvre de honte, et mon esprit me répond par mon intelligence.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Sais-tu bien que, de tout temps, depuis que l’homme a été mis sur la terre,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 L’exultation des méchants est courte, et la joie de l’impie n’est que pour un moment?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Si sa hauteur s’élève jusqu’aux cieux, et que sa tête touche les nuées,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 Il périra pour toujours comme ses ordures; ceux qui l’ont vu diront: Où est-il?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Il s’envole comme un songe, et on ne le trouve pas; il s’enfuit comme une vision de la nuit.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 L’œil l’a regardé et ne l’aperçoit plus, et son lieu ne le revoit plus.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Ses fils rechercheront la faveur des pauvres, et ses mains restitueront [ce que] sa violence [a ravi].
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Ses os étaient pleins de sa jeunesse: elle se couchera avec lui sur la poussière.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Si le mal est doux dans sa bouche, [et] qu’il le cache sous sa langue,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 S’il l’épargne et ne l’abandonne pas, mais qu’il le retienne dans sa bouche,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 Son pain sera changé dans ses entrailles en un fiel d’aspic au-dedans de lui.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Il a avalé les richesses, et il les vomira; Dieu les chassera de son ventre.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Il sucera le venin des aspics, la langue de la vipère le tuera.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 Il ne verra pas des ruisseaux, des rivières, des torrents de miel et de beurre.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Il rendra le fruit de son travail, et ne l’avalera pas; il le restituera selon sa valeur, et ne s’en réjouira pas.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Car il a opprimé, délaissé les pauvres; il a pillé une maison qu’il n’avait pas bâtie.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Parce qu’il n’a pas connu de repos dans son désir, il ne sauvera rien de ce qu’il a de plus cher.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Rien n’a échappé à sa voracité: c’est pourquoi son bien-être ne durera pas.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Dans la plénitude de son abondance, il sera dans la détresse; toutes les mains des malheureux viendront sur lui.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Il arrivera que, pour remplir son ventre, [Dieu] enverra sur lui l’ardeur de sa colère, et la fera pleuvoir sur lui dans sa chair.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 S’il fuit devant les armes de fer, un arc d’airain le transpercera.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Il arrache [la flèche] et elle sort de son corps, et le fer étincelant de son fiel: les terreurs sont sur lui.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Toutes les ténèbres sont réservées pour ses trésors; un feu qu’on ne souffle pas le dévorera, [et] se repaîtra de ce qui reste dans sa tente.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Les cieux révéleront son iniquité, et la terre s’élèvera contre lui.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Le revenu de sa maison sera emporté; il s’écoulera au jour de Sa colère.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Telle est, de la part de Dieu, la portion de l’homme méchant, et l’héritage qui lui est assigné par Dieu.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >