< Job 19 >

1 Et Job répondit et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jusques à quand affligerez-vous mon âme, et m’accablerez-vous de paroles?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Voilà dix fois que vous m’avez outragé, vous n’avez pas honte de m’étourdir.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Mais si vraiment j’ai erré, mon erreur demeure avec moi.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Si réellement vous voulez vous élever contre moi et faire valoir mon opprobre contre moi,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Sachez donc que c’est Dieu qui me renverse et qui m’entoure de son filet.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Voici, je crie à la violence, et je ne suis pas exaucé; je pousse des cris, et il n’y a pas de jugement.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Il a fermé mon chemin et je ne puis passer, et il a mis des ténèbres sur mes sentiers;
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Il m’a dépouillé de ma gloire et a ôté la couronne de dessus ma tête;
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Il m’a détruit de tous côtés, et je m’en vais; il a arraché mon espérance comme un arbre.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Il a allumé contre moi sa colère, et il m’a tenu pour l’un de ses ennemis.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ses troupes sont venues ensemble, et elles ont dressé en chaussée leur chemin contre moi et se sont campées autour de ma tente.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Il a éloigné de moi mes frères, et ceux de ma connaissance me sont devenus entièrement étrangers;
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Mes proches m’ont délaissé, et ceux que je connaissais m’ont oublié.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Ceux qui séjournent dans ma maison et mes servantes me tiennent pour un étranger; je suis à leurs yeux comme un homme du dehors.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 J’ai appelé mon serviteur, et il n’a pas répondu; de ma bouche je l’ai supplié.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Mon haleine est étrangère à ma femme, et ma supplication, aux fils du sein de ma mère.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Même les petits enfants me méprisent; je me lève, et ils parlent contre moi.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Tous les hommes de mon intimité m’ont en horreur, et ceux que j’aimais se sont tournés contre moi.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Mes os s’attachent à ma peau et à ma chair, et j’ai échappé avec la peau de mes dents!
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Ayez pitié de moi, ayez pitié de moi, vous mes amis! car la main de Dieu m’a atteint.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Pourquoi, comme Dieu, me poursuivez-vous et n’êtes-vous pas rassasiés de ma chair?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Oh! si seulement mes paroles étaient écrites! si seulement elles étaient inscrites dans un livre,
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Avec un style de fer et du plomb, et gravées dans le roc pour toujours!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Et moi, je sais que mon rédempteur est vivant, et que, le dernier, il sera debout sur la terre;
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Et après ma peau, ceci sera détruit, et de ma chair je verrai Dieu,
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Que je verrai, moi, pour moi-même; et mes yeux [le] verront, et non un autre: – mes reins se consument dans mon sein.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Si vous dites: Comment le poursuivrons-nous? et que la racine de la chose se trouve en moi,
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Tremblez pour vous-mêmes devant l’épée! car l’épée est l’instrument de la fureur contre les iniquités; afin que vous sachiez qu’il y a un jugement!
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >