< Jérémie 19 >
1 Ainsi dit l’Éternel: Va, et achète un vase de potier, et [prends] des anciens du peuple et des anciens des sacrificateurs,
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
2 et sors vers la vallée du fils de Hinnom, qui est à l’entrée de la porte de la poterie, et crie là les paroles que je te dirai,
ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
3 et dis: Écoutez la parole de l’Éternel, vous, rois de Juda, et vous, habitants de Jérusalem: Ainsi dit l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël: Voici, je fais venir sur ce lieu-ci un mal tel, que quiconque l’entendra, les oreilles lui tinteront;
Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
4 parce qu’ils m’ont abandonné, et qu’ils m’ont aliéné ce lieu, et qu’ils y ont brûlé de l’encens à d’autres dieux que n’ont connus ni eux, ni leurs pères, ni les rois de Juda, et qu’ils ont rempli ce lieu du sang des innocents,
Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
5 et ont bâti les hauts lieux de Baal, pour brûler au feu leurs fils en holocauste à Baal; ce que je n’ai point commandé, et dont je n’ai point parlé, et qui ne m’est point monté au cœur.
Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
6 C’est pourquoi, voici, des jours viennent, dit l’Éternel, où ce lieu-ci ne sera plus appelé Topheth, ni la vallée du fils de Hinnom, mais la vallée de la tuerie.
Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
7 Et je rendrai vain le conseil de Juda et de Jérusalem dans ce lieu-ci, et je les ferai tomber par l’épée devant leurs ennemis et par la main de ceux qui cherchent leur vie, et je donnerai leurs cadavres en pâture aux oiseaux des cieux et aux bêtes de la terre.
“‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
8 Et je ferai de cette ville un sujet d’étonnement et de sifflement: quiconque passera à côté d’elle s’étonnera et sifflera sur toutes ses plaies.
Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
9 Et je leur ferai manger la chair de leurs fils et la chair de leurs filles; et ils mangeront chacun la chair de son prochain, dans le siège et dans la détresse dont les enserreront leurs ennemis et ceux qui cherchent leur vie.
Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
10 Et tu briseras le vase devant les yeux des hommes qui sont allés avec toi,
“Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
11 et tu leur diras: Ainsi dit l’Éternel des armées: Je briserai ainsi ce peuple et cette ville, comme on brise un vase de potier qui ne peut être raccommodé; et on enterrera à Topheth, jusqu’à ce qu’il n’y ait plus de place pour enterrer.
ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
12 Je ferai ainsi à ce lieu, dit l’Éternel, et à ses habitants, pour rendre cette ville semblable à Topheth;
Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
13 et les maisons de Jérusalem et les maisons des rois de Juda seront, comme le lieu de Topheth, impures, – toutes les maisons sur les toits desquelles ils ont brûlé de l’encens à toute l’armée des cieux, et ont répandu des libations à d’autres dieux.
Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
14 Et Jérémie vint de Topheth, où l’Éternel l’avait envoyé pour prophétiser; et il se tint dans le parvis de la maison de l’Éternel, et dit à tout le peuple:
Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
15 Ainsi dit l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël: Voici, je fais venir sur cette ville, et sur toutes ses villes, tout le mal que j’ai prononcé contre elle, parce qu’ils ont roidi leur cou pour ne point écouter mes paroles.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”