< Jérémie 14 >

1 La parole de l’Éternel qui vint à Jérémie au sujet de la sécheresse.
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 Juda mène deuil, et ses portes défaillent; elles sont en deuil, par terre; et le cri de Jérusalem est monté.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Et ses nobles ont envoyé à l’eau les petits; ils sont allés aux citernes, ils n’ont pas trouvé d’eau; ils sont revenus, leurs vases vides; ils ont eu honte, ils ont été confus, et ils ont couvert leur tête.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Parce que la terre est crevassée, parce qu’il n’y a point eu de pluie dans le pays, les cultivateurs sont honteux, ils ont couvert leur tête;
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 car aussi la biche a mis bas dans les champs, et a abandonné [son faon], parce qu’il n’y a point d’herbe verte;
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 et les ânes sauvages se sont tenus sur les hauteurs, ils ont humé l’air comme des chacals; leurs yeux se sont consumés, parce qu’il n’y a point d’herbe.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 Éternel! si nos iniquités rendent témoignage contre nous, agis à cause de ton nom; car nos infidélités sont multipliées, nous avons péché contre toi.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Attente d’Israël, celui qui le sauve au temps de la détresse! pourquoi serais-tu comme un étranger dans le pays, comme un voyageur qui se détourne pour passer la nuit?
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Pourquoi serais-tu comme un homme stupéfait, comme un homme fort qui ne peut sauver? Toutefois tu es au milieu de nous, ô Éternel, et nous sommes appelés de ton nom; ne nous délaisse pas!
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Ainsi dit l’Éternel à ce peuple: C’est ainsi qu’ils ont aimé à aller çà et là, ils n’ont pas retenu leurs pieds; et l’Éternel ne prend point plaisir en eux: maintenant il se souviendra de leurs iniquités et il visitera leurs péchés.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Et l’Éternel me dit: Ne prie pas pour ce peuple pour leur bien.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 S’ils jeûnent, je n’écouterai pas leur cri, et s’ils offrent un holocauste et une offrande de gâteau, je ne les agréerai pas; car je les consumerai par l’épée, et par la famine, et par la peste.
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 Et je dis: Ah, Seigneur Éternel! voici, les prophètes leur disent: Vous ne verrez pas l’épée, et la famine ne viendra pas sur vous; car je vous donnerai une vraie paix en ce lieu-ci.
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 Et l’Éternel me dit: Les prophètes prophétisent le mensonge en mon nom; je ne les ai pas envoyés, et je ne leur ai pas commandé, et je ne leur ai pas parlé; ils vous prophétisent une vision de mensonge, et la divination, et la vanité, et la tromperie de leur cœur.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 C’est pourquoi, ainsi dit l’Éternel au sujet des prophètes qui prophétisent en mon nom, et que je n’ai point envoyés, et qui disent: L’épée et la famine ne seront pas dans ce pays: Ces prophètes-là seront consumés par l’épée et par la famine.
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 Et le peuple auquel ils prophétisent sera jeté dans les rues de Jérusalem à cause de la famine et de l’épée, et il n’y aura personne pour les enterrer, eux, leurs femmes, et leurs fils, et leurs filles; et je verserai sur eux leur iniquité.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 Et tu leur diras cette parole: Que mes yeux se fondent en larmes, nuit et jour, et qu’ils ne cessent pas, car la vierge, fille de mon peuple, est ruinée d’une grande ruine, d’un coup très douloureux.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 Si je sors aux champs, voici des gens tués par l’épée, et si j’entre dans la ville, voici des gens alanguis par la faim; car prophète et sacrificateur s’en iront dans un pays qu’ils ne connaissent pas.
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Aurais-tu entièrement rejeté Juda? Ton âme serait-elle dégoûtée de Sion? Pourquoi nous as-tu frappés sans qu’il y ait de guérison pour nous? On attendait la paix, et il n’y a rien de bon, – et le temps de la guérison, et voici l’épouvante.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Nous reconnaissons, ô Éternel! notre méchanceté, l’iniquité de nos pères; car nous avons péché contre toi.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 À cause de ton nom, ne [nous] dédaigne point, n’avilis pas le trône de ta gloire; souviens-toi, ne romps pas ton alliance avec nous.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Parmi les vanités des nations, en est-il qui donnent la pluie? ou les cieux donnent-ils des ondées? N’est-ce pas toi, Éternel! notre Dieu? Et nous nous attendons à toi; car c’est toi qui as fait toutes ces choses.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jérémie 14 >