< Isaïe 41 >

1 Faites silence devant moi, îles; et que les peuples renouvellent leur force! Qu’ils s’approchent; … alors, qu’ils parlent! Approchons ensemble en jugement!
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Qui, du levant, réveilla [celui] dont la justice accompagne les pas? Il livra les nations devant lui, et lui soumit les rois; il les livra à son épée comme de la poussière, et à son arc comme du chaume chassé [par le vent].
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Il les poursuivit; il passa en sûreté par un chemin où il n’était pas allé de ses pieds.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Qui a opéré et fait [cela], appelant les générations dès le commencement? Moi, l’Éternel, le premier; et, avec les derniers, je suis le Même.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Les îles le virent et eurent peur, les bouts de la terre tremblèrent: ils s’approchèrent et vinrent;
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 ils s’entraidèrent l’un l’autre, et [chacun] dit à son frère: Sois fort.
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Et l’ouvrier fortifiait le fondeur; celui qui polit au marteau [fortifiait] celui qui frappe sur l’enclume, disant de la soudure: Elle est bonne; … et il l’a affermi avec des clous, afin qu’il ne branle pas.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Et toi, Israël, mon serviteur, Jacob, que j’ai choisi, semence d’Abraham mon ami,
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 toi que j’ai pris des bouts de la terre et appelé de ses extrémités, et à qui j’ai dit: Tu es mon serviteur, je t’ai choisi et je ne t’ai pas rejeté; …
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 ne crains point, car je suis avec toi; ne sois pas inquiet, car moi je suis ton Dieu. Je te fortifierai; oui, je t’aiderai; oui, je te soutiendrai par la droite de ma justice.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Voici, tous ceux qui s’irritent contre toi, seront honteux et confondus; ils seront comme un rien, et les hommes qui contestent contre toi périront.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Tu les chercheras, et tu ne les trouveras pas, les hommes qui ont querelle avec toi; ils seront comme un rien et comme néant, les hommes qui te font la guerre.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Car moi, l’Éternel, ton Dieu, je tiens ta droite, [moi] qui te dis: Ne crains point, moi je t’aiderai.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Ne crains point, toi Jacob, vermisseau! [et vous], hommes d’Israël! Moi je t’aiderai, dit l’Éternel, et ton rédempteur, le Saint d’Israël.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Voici, j’ai fait de toi un traîneau à battre, tranchant, neuf, à doubles dents: tu battras les montagnes et tu les réduiras en poussière, et tu rendras les collines comme de la balle;
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 tu les vanneras, et le vent les emportera, et le tourbillon les dispersera; et toi, tu t’égaieras en l’Éternel, tu te glorifieras dans le Saint d’Israël.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Les affligés et les nécessiteux chercheront de l’eau, et il n’y en a pas, leur langue est desséchée par la soif: moi, l’Éternel, je leur répondrai, [moi], le Dieu d’Israël, je ne les abandonnerai pas.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Je ferai couler des rivières sur les hauteurs, et des fontaines au milieu des vallées; je changerai le désert en un étang d’eau, et la terre aride en des sources jaillissantes.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Je ferai croître dans le désert le cèdre, l’acacia, et le myrte, et l’olivier; je mettrai dans le lieu stérile le cyprès, le pin et le buis ensemble;
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 afin qu’ils voient, et qu’ils sachent, et qu’ils considèrent, et qu’ils comprennent tous ensemble, que la main de l’Éternel a fait cela, et que le Saint d’Israël l’a créé.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Produisez votre cause, dit l’Éternel; apportez ici vos arguments, dit le roi de Jacob.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Qu’ils les apportent, et qu’ils nous déclarent ce qui arrivera. Déclarez les premières choses, ce qu’elles sont, afin que nous [y] fassions attention, et que nous en connaissions le résultat; ou faites-nous savoir celles qui viendront;
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 – déclarez les choses qui vont arriver dans la suite, et nous saurons que vous êtes des dieux; oui, faites du bien et faites du mal, afin que nous le considérions et le voyions ensemble.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Voici, vous êtes moins que rien, et votre œuvre est du néant: qui vous choisit est une abomination…
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Je l’ai réveillé du nord, et il vient, – du lever du soleil, celui qui invoquera mon nom. Et il marchera sur les princes comme sur de la boue, et comme le potier foule l’argile.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Qui l’a déclaré dès le commencement, afin que nous le sachions, et d’avance, afin que nous disions: C’est juste? Non, il n’y a personne qui le déclare; non, personne qui le fasse entendre; non, personne qui entende vos paroles.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Le premier, [j’ai dit] à Sion: Voici, les voici! et à Jérusalem: Je donnerai un messager de bonnes nouvelles!
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Et j’ai regardé, et il n’y avait personne – même parmi eux – et point de conseiller, pour leur demander, et avoir d’eux une réponse.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Voici, tous sont la vanité, leurs œuvres sont un néant, leurs images de fonte sont le vent et le vide.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

< Isaïe 41 >