< Osée 9 >
1 Ne te réjouis pas, Israël, jusqu’à l’exultation, comme les peuples; car tu t’es prostitué, abandonnant ton Dieu. Tu as aimé les présents dans toutes les aires à froment.
Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 L’aire et la cuve ne les nourriront pas, et le moût les trompera.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
3 Ils ne demeureront pas dans le pays de l’Éternel; mais Éphraïm retournera en Égypte, et mangera en Assyrie ce qui est impur.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 Ils ne feront pas de libations de vin à l’Éternel, et leurs sacrifices ne lui seront pas agréables: ce sera pour eux comme le pain de deuil; tous ceux qui en mangeront se souilleront; car leur pain est pour eux-mêmes; il n’entrera pas dans la maison de l’Éternel.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Que ferez-vous au jour de l’assemblée, et au jour de fête de l’Éternel?
Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 Car voici, ils s’en sont allés à cause de la dévastation: l’Égypte les rassemblera, Moph les enterrera. Ce qu’ils ont de précieux [en objets] d’argent, l’ortie les héritera; le chardon est dans leurs tentes.
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Ils arrivent, les jours de la visitation; ils arrivent, les jours de la récompense! Israël le saura. Le prophète est insensé, l’homme inspiré est fou, à cause de la grandeur de ton iniquité et de la grandeur de ton hostilité.
Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 Éphraïm est aux aguets, [regardant à d’autres] à côté de mon Dieu. Le prophète est un piège d’oiseleur sur tous ses chemins, une hostilité dans la maison de son Dieu.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Ils se sont enfoncés dans la corruption comme aux jours de Guibha. Il se souviendra de leur iniquité, il visitera leurs péchés.
Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 J’ai trouvé Israël comme des raisins dans le désert; j’ai vu vos pères au commencement comme le premier fruit du figuier. Ils sont allés à Baal-Péor, et ils se sont voués à cette honteuse [idole], et sont devenus abominables comme leur amant.
“Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Quant à Éphraïm, leur gloire s’envolera comme un oiseau; … point d’enfantement, point de grossesse, point de conception!
Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Quand même ils élèveraient leurs fils, je les priverais de fils, en sorte qu’il n’y ait pas d’homme. Car aussi, malheur à eux, lorsque je me serai retiré d’eux!
Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Éphraïm, comme je l’ai vu, a été une Tyr plantée dans une campagne agréable; mais Éphraïm doit mener dehors ses fils au meurtrier.
Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
14 Donne-leur, Éternel! Que donneras-tu? Donne-leur un sein qui avorte et des mamelles desséchées.
Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
15 Toute leur méchanceté est à Guilgal, car là, je les ai haïs; à cause de la méchanceté de leurs actions, je les chasserai de ma maison. Je ne les aimerai plus. Tous leurs princes sont des rebelles.
“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Éphraïm a été frappé: leur racine a séché, ils ne produiront pas de fruit. Si même ils enfantent, je ferai mourir le fruit précieux de leur sein.
Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Mon Dieu les a rejetés, car ils ne l’ont pas écouté, et ils seront errants parmi les nations.
Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.