< Genèse 5 >
1 C’est ici le livre des générations d’Adam. Au jour où Dieu créa Adam, il le fit à la ressemblance de Dieu.
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 Il les créa mâle et femelle, et les bénit; et il appela leur nom Adam, au jour où ils furent créés.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 Et Adam vécut 130 ans, et engendra [un fils] à sa ressemblance, selon son image, et appela son nom Seth.
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 Et les jours d’Adam, après qu’il eut engendré Seth, furent 800 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 Et tous les jours qu’Adam vécut furent 930 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 Et Seth vécut 105 ans, et engendra Énosh.
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 Et Seth, après qu’il eut engendré Énosh, vécut 807 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 Et tous les jours de Seth furent 912 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 Et Énosh vécut 90 ans, et engendra Kénan.
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 Et Énosh, après qu’il eut engendré Kénan, vécut 815 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 Et tous les jours d’Énosh furent 905 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 Et Kénan vécut 70 ans, et engendra Mahalaleël.
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 Et Kénan, après qu’il eut engendré Mahalaleël, vécut 840 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Et tous les jours de Kénan furent 910 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 Et Mahalaleël vécut 65 ans, et engendra Jéred.
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 Et Mahalaleël, après qu’il eut engendré Jéred, vécut 830 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 Et tous les jours de Mahalaleël furent 895 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 Et Jéred vécut 162 ans, et engendra Hénoc.
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 Et Jéred, après qu’il eut engendré Hénoc, vécut 800 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Et tous les jours de Jéred furent 962 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 Et Hénoc vécut 65 ans, et engendra Methushélah.
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 Et Hénoc, après qu’il eut engendré Methushélah, marcha avec Dieu 300 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 Et tous les jours de Hénoc furent 365 ans.
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 Et Hénoc marcha avec Dieu; et il ne fut plus, car Dieu le prit.
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 Et Methushélah vécut 187 ans, et engendra Lémec.
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 Et Methushélah, après qu’il eut engendré Lémec, vécut 782 ans; et il engendra des fils et des filles.
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 Et tous les jours de Methushélah furent 969 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 Et Lémec vécut 182 ans, et engendra un fils;
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 et il appela son nom Noé, disant: Celui-ci nous consolera à l’égard de notre ouvrage et du travail de nos mains, à cause du sol que l’Éternel a maudit.
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 Et Lémec, après qu’il eut engendré Noé, vécut 595 ans; et il engendra des fils et des filles.
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 Et tous les jours de Lémec furent 777 ans; et il mourut.
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 Et Noé était âgé de 500 ans, et Noé engendra Sem, Cham, et Japheth.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.