< Ézéchiel 23 >

1 Et la parole de l’Éternel vint à moi, disant:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils d’homme, il y avait deux femmes, filles d’une même mère;
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 et elles se prostituèrent en Égypte, elles se prostituèrent dans leur jeunesse: là leurs mamelles furent froissées, là les seins de leur virginité furent pressés.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Et leurs noms étaient: Ohola, l’aînée, et Oholiba, sa sœur; et elles étaient à moi, et elles enfantèrent des fils et des filles. Et leurs noms: Samarie est Ohola, et Jérusalem, Oholiba.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Et Ohola, étant à moi, se prostitua et se passionna pour ses amants, pour les Assyriens, ses voisins,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 vêtus de bleu, gouverneurs et chefs, tous beaux jeunes hommes, cavaliers montés sur des chevaux;
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 et elle se livra à ses prostitutions avec eux, tous l’élite des fils d’Assur; et, avec tous ceux pour lesquels elle se passionna, avec toutes leurs idoles, elle se rendit impure.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Et elle n’abandonna pas ses prostitutions [qui datent] de l’Égypte, car ils avaient couché avec elle dans sa jeunesse, et ils avaient pressé les seins de sa virginité, et avaient versé sur elle leur prostitution.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 C’est pourquoi je la livrai en la main de ses amants, en la main des fils d’Assur pour lesquels elle s’était passionnée.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Ils découvrirent sa nudité, prirent ses fils et ses filles, et la tuèrent elle-même par l’épée; et elle devint renommée parmi les femmes, et ils exécutèrent des jugements sur elle.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 Et sa sœur Oholiba vit [cela], et se corrompit plus qu’elle dans ses amours passionnées; et ses prostitutions furent plus [grandes] que les débauches de sa sœur.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Elle se passionna pour les fils d’Assur, gouverneurs et chefs, ses voisins, vêtus magnifiquement, cavaliers montés sur des chevaux, tous beaux jeunes hommes.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 Et je vis qu’elle s’était rendue impure: elles suivaient toutes deux la même voie.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Et elle avait ajouté à ses prostitutions, et elle avait vu des hommes dessinés sur le mur, des images de Chaldéens tracés au vermillon,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 portant des ceintures sur leurs reins, avec des tiares flottantes sur leurs têtes, tous ayant l’aspect de grands seigneurs, à la ressemblance des fils de Babel, de la Chaldée, pays de leur naissance;
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 et elle se passionna pour eux en les voyant de ses yeux, et envoya des messagers vers eux en Chaldée.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Et les fils de Babel vinrent vers elle dans le lit des amours, et la rendirent impure par leur prostitution, et elle se rendit impure avec eux; puis son âme se détacha d’eux.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Et elle découvrit ses prostitutions, et elle découvrit sa nudité; et mon âme se détacha d’elle, comme mon âme s’était détachée de sa sœur.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Et elle multiplia ses prostitutions, se souvenant des jours de sa jeunesse, où elle s’était prostituée dans le pays d’Égypte;
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 et elle se passionna pour ses concubins, dont la chair est [comme] la chair des ânes, et dont le flux est [comme] le flux des chevaux.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Tu te rappelas l’infamie de ta jeunesse, lorsque les Égyptiens pressaient tes seins à cause des mamelles de ta jeunesse.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 C’est pourquoi, Oholiba! ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: Voici, je réveille contre toi tes amants, desquels ton âme s’est détachée, et je les ferai venir contre toi de tous côtés:
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 les fils de Babel, et tous les Chaldéens, Pekod et Shoa et Koa, tous les fils d’Assur avec eux, tous beaux jeunes hommes, gouverneurs et chefs, grands seigneurs et gens de renom, tous montés sur des chevaux.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 Et ils viendront contre toi avec des armes, des chars et des roues, et avec un rassemblement de peuples; ils se placeront contre toi, tout autour, avec le bouclier et l’écu et le casque; et je leur commettrai le jugement, et ils te jugeront selon leurs jugements.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 Et je mettrai ma jalousie contre toi, et ils agiront envers toi avec fureur: ils te couperont le nez et les oreilles; et ce qui restera de toi tombera par l’épée. Ils prendront tes fils et tes filles, et ce qui restera de toi sera dévoré par le feu.
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 Et ils te dépouilleront de tes vêtements, et prendront les objets dont tu te pares;
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 et je ferai cesser en toi ton infamie et ta prostitution [qui date] du pays d’Égypte; et tu ne lèveras plus tes yeux vers eux, et tu ne te souviendras plus de l’Égypte.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Car ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: Voici, je te livre en la main de ceux que tu hais, en la main de ceux dont ton âme s’est détachée;
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 et ils agiront envers toi avec haine, et prendront tout ton travail, et te laisseront nue et découverte; et la nudité de tes débauches, et ton infamie, et tes prostitutions, seront découvertes.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 Ces choses t’arriveront, parce que tu t’es prostituée après les nations, parce que tu t’es rendue impure par leurs idoles.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Tu as marché dans le chemin de ta sœur; et j’ai mis sa coupe dans ta main.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: Tu boiras la coupe de ta sœur, profonde et large; tu seras en risée et en raillerie, [car] elle contient beaucoup.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Tu seras remplie d’ivresse et de chagrin; ce sera une coupe d’étonnement et de désolation, la coupe de ta sœur Samarie.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Tu la boiras, et tu la suceras, et tu en rongeras les tessons, et tu te déchireras les seins; car j’ai parlé, dit le Seigneur, l’Éternel.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 C’est pourquoi, ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: Parce que tu m’as oublié et que tu m’as jeté derrière ton dos, toi aussi porte ton infamie et tes prostitutions.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 Et l’Éternel me dit: Fils d’homme, jugeras-tu Ohola et Oholiba? Déclare-leur leurs abominations.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 Car elles ont commis adultère, et il y a du sang à leurs mains; elles ont commis adultère avec leurs idoles; et même leurs fils qu’elles m’avaient enfantés, elles les leur ont consacrés pour être dévorés.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Elles m’ont fait encore ceci: elles ont rendu impur mon sanctuaire en ce jour-là, et elles ont profané mes sabbats;
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 quand elles avaient égorgé leurs fils à leurs idoles, elles venaient ce même jour dans mon sanctuaire, pour le profaner; et voici, elles ont fait ainsi au milieu de ma maison.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Et bien plus, elles ont envoyé vers des hommes venant de loin, auxquels un messager avait été envoyé; et voici, ils sont venus, ceux pour lesquels tu t’es lavée, tu as peint tes yeux et tu t’es parée d’ornements;
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 et tu t’es assise sur un lit somptueux devant lequel était dressée une table, et tu as placé sur elle mon encens et mon huile.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 Et il y avait en elle le bruit d’une multitude à l’aise; et, vers la foule des hommes, on fit venir du désert des buveurs, qui leur mirent des bracelets aux mains et une couronne de beauté sur la tête.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Et j’ai dit de celle qui était usée par l’adultère: Maintenant commettra -t-elle ses prostitutions, elle aussi?
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 Et on est venu vers elle comme on vient vers une femme prostituée. Ainsi ils sont venus vers Ohola et vers Oholiba, femmes criminelles.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Et des hommes justes, eux, les jugeront du jugement des femmes adultères et du jugement de celles qui versent le sang; car elles sont adultères, et il y a du sang à leurs mains.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Car ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: On fera monter contre elles un rassemblement [d’hommes], et on les livrera à la vexation et au pillage;
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 et le rassemblement les lapidera avec des pierres, et ils les transperceront avec leurs épées; ils tueront leurs fils et leurs filles, et ils brûleront leurs maisons par le feu.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Et je ferai cesser l’infamie dans le pays; et toutes les femmes seront enseignées, et ne feront pas selon votre infamie.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 Et ils mettront vos infamies sur vous, et vous porterez les péchés de vos idoles; et vous saurez que je suis le Seigneur, l’Éternel.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 23 >