< Amos 5 >
1 Écoutez cette parole, une complainte que j’élève sur vous, maison d’Israël!
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 Elle est tombée, elle ne se relèvera pas, la vierge d’Israël; elle est étendue sur sa terre, il n’y a personne qui la relève.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Car ainsi dit le Seigneur, l’Éternel: La ville qui allait en campagne avec 1 000, en aura 100 de reste; et celle qui allait en campagne avec 100, en aura dix de reste, pour la maison d’Israël.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Car ainsi dit l’Éternel à la maison d’Israël: Cherchez-moi, et vous vivrez;
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 et ne cherchez pas Béthel, et n’allez pas à Guilgal, et ne passez pas à Beër-Shéba; car Guilgal ira certainement en captivité, et Béthel sera réduite à rien.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Cherchez l’Éternel, et vous vivrez, de peur qu’il n’envahisse comme le feu la maison de Joseph, et ne la dévore, et qu’il n’y ait personne à Béthel qui éteigne.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 Vous qui changez en absinthe le droit, et qui couchez par terre la justice,
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 [cherchez-le], lui qui a fait les Pléiades et Orion; qui change en matin l’ombre de la mort, et transforme le jour en ténèbres de la nuit; qui appelle les eaux de la mer, et les verse sur la face de la terre: l’Éternel est son nom.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 Il fait lever subitement la destruction sur le fort, et la destruction vient sur la forteresse.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Ils haïssent celui qui reprend à la porte, et ont en abomination celui qui parle avec intégrité.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 C’est pourquoi, parce que vous foulez aux pieds le pauvre, et que vous prenez de lui des charges de blé: vous avez bâti des maisons de pierres de taille, mais vous n’y habiterez pas; vous avez planté des vignes excellentes, et vous n’en boirez pas le vin;
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 car je connais vos nombreuses transgressions et vos grands péchés: ils oppriment le juste, prennent des présents, et font fléchir à la porte le droit des pauvres.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 C’est pourquoi, en ce temps-ci, le sage gardera le silence, car c’est un temps mauvais.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Recherchez le bien, et non le mal, afin que vous viviez; et ainsi l’Éternel, le Dieu des armées, sera avec vous, comme vous le dites.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Haïssez le mal, et aimez le bien, et établissez dans la porte le juste jugement; peut-être l’Éternel, le Dieu des armées, usera-t-il de grâce envers le reste de Joseph.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 C’est pourquoi, ainsi dit l’Éternel, le Dieu des armées, le Seigneur: Dans toutes les places, la lamentation! et dans toutes les rues, on dira: Hélas, hélas! Et on appellera le laboureur au deuil, et à la lamentation ceux qui s’entendent aux chants de douleur.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 Et dans toutes les vignes, la lamentation! car je passerai au milieu de toi, dit l’Éternel.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Malheur à vous qui désirez le jour de l’Éternel! À quoi vous [servira] le jour de l’Éternel? Il sera ténèbres, et non lumière,
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 comme si un homme s’enfuyait de devant un lion, et qu’un ours le rencontre; ou qu’il entre dans la maison et appuie sa main contre le mur, et qu’un serpent le morde.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Le jour de l’Éternel n’est-il pas ténèbres, et non lumière? et profonde obscurité, et non splendeur?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Je hais, je méprise vos fêtes, et je ne flairerai pas [de bonne odeur] dans vos assemblées solennelles;
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 si vous m’offrez des holocaustes et vos offrandes de gâteau, je ne les agréerai pas, et je ne regarderai pas le sacrifice de prospérités de vos bêtes grasses.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Ôte de devant moi le bruit de tes cantiques; et la musique de tes luths, je ne l’écouterai pas.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Mais que le jugement roule comme des eaux, et la justice comme un fleuve qui ne tarit pas!
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 M’avez-vous offert des sacrifices et des offrandes dans le désert, pendant 40 ans, maison d’Israël?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Mais vous avez porté le tabernacle de votre Moloc, et le Kiun de vos images, l’étoile de votre dieu, que vous vous êtes fait;
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 et je vous transporterai au-delà de Damas, dit l’Éternel; son nom est le Dieu des armées.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.