< 2 Rois 22 >

1 Josias était âgé de huit ans lorsqu’il commença de régner; et il régna 31 ans à Jérusalem; et le nom de sa mère était Jedida, fille d’Adaïa, de Botskath.
Yosiya anakhala mfumu ali ndi zaka zisanu ndi zitatu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 31. Amayi ake anali Yedida mwana wa Adaiya wochokera ku Bozikati.
2 Et il fit ce qui est droit aux yeux de l’Éternel, et marcha dans toute la voie de David, son père, et ne s’en écarta ni à droite ni à gauche.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo anayenda mʼnjira zonse za Davide kholo lake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.
3 Et il arriva, la dix-huitième année du roi Josias, que le roi envoya Shaphan, le scribe, fils d’Atsalia, fils de Meshullam, à la maison de l’Éternel, disant:
Mʼchaka cha 18 cha ufumu wake, Mfumu Yosiya anatuma mlembi wa nyumba ya mfumu, Safani, mwana wa Azariya, mwana wa Mesulamu, ku Nyumba ya Yehova. Iye anati,
4 Monte vers Hilkija, le grand sacrificateur, et qu’on relève l’argent qui a été apporté dans la maison de l’Éternel [et] que les gardiens du seuil ont recueilli de la part du peuple;
“Pita kwa mkulu wa ansembe Hilikiya ndipo ukamuwuze kuti awerenge ndalama zimene anthu abwera nazo ku Nyumba ya Yehova, zimene alonda a pa khomo anasonkhanitsa kwa anthu.
5 et qu’on le remette en la main de ceux qui font l’ouvrage, qui sont préposés [sur le travail] dans la maison de l’Éternel; et que ceux-ci le remettent à ceux qui font l’ouvrage dans la maison de l’Éternel, pour réparer les brèches de la maison:
Ndalamazo azipereke kwa anthu amene asankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Ndipo anthu amenewa azilipira antchito amene akukonzanso Nyumba ya Yehova,
6 aux charpentiers, et aux constructeurs, et aux maçons, et afin d’acheter des bois et des pierres de taille, pour réparer la maison;
amisiri a matabwa, amisiri omanga ndi amisiri a miyala. Iwo akagulenso matabwa ndi miyala yosemedwa kuti akonzere Nyumba ya Yehova.
7 toutefois qu’on ne compte pas avec eux l’argent remis entre leurs mains, car ils agissent avec fidélité.
Koma anthu amene apatsidwa ndalama zolipira antchito okonza Nyumbayo asawafunse za kagwiritsidwe ntchito ka ndalamazo, popeza ndi anthu wokhulupirika.”
8 Et Hilkija, le grand sacrificateur, dit à Shaphan, le scribe: J’ai trouvé le livre de la loi dans la maison de l’Éternel. Et Hilkija donna le livre à Shaphan, et il le lut.
Mkulu wa ansembe Hilikiya anawuza Safani, mlembiyo kuti, “Ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Anapereka bukulo kwa Safani amene analiwerenga.
9 Et Shaphan, le scribe, vint vers le roi, et rendit compte au roi, et dit: Tes serviteurs ont versé l’argent qui s’est trouvé dans la maison, et l’ont remis entre les mains de ceux qui font l’ouvrage, qui sont préposés [sur le travail] dans la maison de l’Éternel.
Ndipo Safani mlembi uja, anapita nakafotokozera mfumu kuti, “Atumiki anu apereka ndalama zija zinali mʼNyumba ya Yehova kwa anthu amene akugwira ntchito ndi kuyangʼanira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova.”
10 Et Shaphan, le scribe, raconta au roi, disant: Hilkija, le sacrificateur, m’a donné un livre. Et Shaphan le lut devant le roi.
Kenaka Safani mlembiyo, anafotokozera mfumu kuti, “Wansembe Hilikiya wandipatsa buku.” Ndipo Safani analiwerenga pamaso pa mfumu.
11 Et il arriva que, quand le roi entendit les paroles du livre de la loi, il déchira ses vêtements.
Mfumu itamva mawu a mʼBuku la Malamulo, inangʼamba zovala zake.
12 Et le roi commanda à Hilkija, le sacrificateur, et à Akhikam, fils de Shaphan, et à Acbor, fils de Michée, et à Shaphan, le scribe, et à Asçaïa, serviteur du roi, disant:
Iyo inalamula wansembe Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Akibo mwana wa Mikaya, Safani mlembi uja ndi Asaiya mtumiki wa mfumu, kuti,
13 Allez, consultez l’Éternel pour moi, et pour le peuple, et pour tout Juda, touchant les paroles de ce livre qui a été trouvé; car grande est la fureur de l’Éternel, qui s’est allumée contre nous, parce que nos pères n’ont pas écouté les paroles de ce livre, pour faire selon tout ce qui y est écrit pour nous.
“Pitani mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa anthu onse a mʼdziko la Yuda, za zomwe zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu kwambiri pa ife ndipo watiyakira chifukwa makolo athu sanamvere mawu a buku ili. Iwo sanachite molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼmenemu zokhudza ife.”
14 Et Hilkija, le sacrificateur, et Akhikam, et Acbor, et Shaphan, et Asçaïa, allèrent vers Hulda, la prophétesse, femme de Shallum, fils de Thikva, fils de Harkhas, qui avait la garde des vêtements; et elle habitait à Jérusalem dans le second quartier de la ville; et ils lui parlèrent.
Choncho Hilikiya wansembe, Ahikamu, Akibo, Safani ndi Asaiya anapita kukayankhula ndi Hulida, mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tikiva, mwana wa Harihasi, wosunga zovala zaufumu. Mneneri wamkaziyu ankakhala mu Yerusalemu, ku chigawo chachiwiri cha mzindawo.
15 Et elle leur dit: Ainsi dit l’Éternel, le Dieu d’Israël: Dites à l’homme qui vous a envoyés vers moi:
Ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Kamuwuzeni munthu amene wakutumani kwa ine kuti,
16 Ainsi dit l’Éternel: Voici, je fais venir du mal sur ce lieu et sur ses habitants, toutes les paroles du livre qu’a lu le roi de Juda.
‘Ichi ndi chimene Yehova akunena: Taonani, ndidzabweretsa mavuto pa malo ano ndi pa anthu ake, molingana ndi zonse zimene zalembedwa mʼbuku limene mfumu ya Yuda yawerenga.
17 Parce qu’ils m’ont abandonné et qu’ils ont brûlé de l’encens à d’autres dieux, pour me provoquer à colère par toute l’œuvre de leurs mains, ma fureur s’est allumée contre ce lieu, et elle ne s’éteindra point.
Chifukwa anthuwo andisiya Ine ndi kumafukiza lubani kwa milungu ina nandikwiyitsa ndi mafano onse amene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzayaka pa malo ano ndipo sudzazimitsidwa.’
18 Et au roi de Juda, qui vous a envoyés pour consulter l’Éternel, vous lui direz ainsi: Ainsi dit l’Éternel, le Dieu d’Israël, quant aux paroles que tu as entendues:
Koma mfumu ya Yuda imene inakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova kayiwuzeni kuti, ‘Ichi ndi chimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena molingana ndi mawu amene unamva:
19 Parce que ton cœur a été sensible, et que tu t’es humilié devant l’Éternel quand tu as entendu ce que j’ai prononcé contre ce lieu et contre ses habitants, [savoir] qu’ils seraient [livrés] à la destruction et à la malédiction, et parce que tu as déchiré tes vêtements et que tu as pleuré devant moi, moi aussi j’ai entendu, dit l’Éternel.
Chifukwa unasweka mtima ndi kudzichepetsa wekha pamaso pa Yehova, pamene unamva zomwe zinayankhulidwa zotsutsana ndi malo ano ndi anthu ake, kuti adzakhala otembereredwa nasanduka bwinja, ndiponso chifukwa unangʼamba zovala ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, akutero Yehova.
20 C’est pourquoi, voici, je vais te recueillir auprès de tes pères, et tu seras recueilli en paix dans tes sépulcres, et tes yeux ne verront pas tout le mal que je fais venir sur ce lieu. Et ils rapportèrent au roi [cette] parole.
Choncho taona, Ine ndidzakutenga kupita kwa makolo ako ndipo udzayikidwa mʼmanda mwako mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene ndidzabweretse pamalo pano.’” Ndipo anthu aja anabwerera nakafotokoza mawu amenewa kwa mfumu.

< 2 Rois 22 >