< 2 Rois 17 >

1 La douzième année d’Achaz, roi de Juda, Osée, fils d’Éla, commença de régner à Samarie sur Israël; [il régna] neuf ans.
Mʼchaka cha 12 cha Ahazi mfumu ya Yuda, Hoseya mwana wa Ela anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka zisanu ndi zinayi.
2 Et il fit ce qui est mauvais aux yeux de l’Éternel, non pas toutefois comme les rois d’Israël qui avaient été avant lui.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi mafumu a Israeli amene ankalamulira iye asanalowe ufumuwo.
3 Shalmanéser, roi d’Assyrie, monta contre lui, et Osée devint son serviteur, et lui envoya des présents.
Salimenezeri mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo Hoseya amene anali pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iyeyo.
4 Et le roi d’Assyrie découvrit qu’Osée conspirait; car [Osée] avait envoyé des messagers à Sô, roi d’Égypte, et il n’envoyait pas de présents au roi d’Assyrie comme [il avait fait] d’année en année; et le roi d’Assyrie l’enferma dans une prison et le lia.
Koma mfumu ya ku Asiriya inazindikira kuti Hoseya akuwukira, pakuti Hoseyayo anali atatumiza nthumwi kwa So mfumu ya Igupto ndiponso analeka kukhoma msonkho kwa mfumu ya ku Asiriya, monga ankachitira chaka ndi chaka. Choncho Salimenezeri anagwira Hoseya ndi kumuyika mʼndende.
5 Et le roi d’Assyrie monta par tout le pays, et monta à Samarie, et l’assiégea trois ans.
Mfumu ya ku Asiriya inapita kukathira nkhondo dziko lonse la Israeli ndipo inapita mpaka ku Samariya ndipo inazinga mzindawo kwa zaka zitatu.
6 La neuvième année d’Osée, le roi d’Assyrie prit Samarie, et il transporta Israël en Assyrie, et les fit habiter à Khalakh, et sur le Khabor, fleuve de Gozan, et dans les villes des Mèdes.
Mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya, mfumu ya ku Asiriya inalanda Samariya ndipo inatenga Aisraeli ndi kupita nawo ku Asiriya. Anakawakhazika ku Hala ndi Habori mʼmbali mwa mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
7 Et il était arrivé que les fils d’Israël avaient péché contre l’Éternel, leur Dieu, qui les avait fait monter du pays d’Égypte, de dessous la main du Pharaon, roi d’Égypte, et qu’ils avaient révéré d’autres dieux.
Zonsezi zinachitika chifukwa Aisraeli anachimwira Yehova Mulungu wawo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto pansi pa ulamuliro wa Farao mfumu ya Igupto. Iwo ankapembedza milungu ina,
8 Et ils marchèrent dans les statuts des nations que l’Éternel avait dépossédées devant les fils d’Israël, et [dans ceux] que les rois d’Israël avaient établis.
ndiponso ankatsatira miyambo ya anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika mʼdzikomo pamodzinso ndi miyambo yonse imene mafumu a Israeli anayambitsa.
9 Et les fils d’Israël firent en secret contre l’Éternel, leur Dieu, des choses qui ne sont pas droites; et ils se bâtirent des hauts lieux dans toutes leurs villes, depuis la tour des gardes jusqu’à la ville forte;
Ndipo Aisraeli ankachita zoyipa mwamseri kutsutsana ndi Yehova Mulungu wawo. Kuchokera ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa, mʼmizinda yawo yonse anamangamo malo opembedzeramo mafano.
10 et ils se dressèrent des statues et des ashères sur toute haute colline et sous tout arbre vert,
Anayimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya mafano a Asera pa phiri lililonse lalitali ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
11 et firent fumer là de l’encens sur tous les hauts lieux, comme les nations que l’Éternel avait transportées de devant eux; et ils firent des choses mauvaises, pour provoquer à colère l’Éternel;
Pa malo aliwonse opembedzera mafano, anthuwa ankafukiza lubani monga momwe ankachitira anthu a mitundu imene Yehova anayichotsa pamene iwo ankafika. Iwo anachita zinthu zoyipa zomwe zinaputa mkwiyo wa Yehova.
12 et ils servirent les idoles, au sujet desquelles l’Éternel leur avait dit: Vous ne ferez point cela.
Ndipo iwowo ankapembedza mafano ngakhale Yehova ananena kuti, “Musadzachite zimenezi.”
13 Et l’Éternel rendit témoignage contre Israël et contre Juda par tous les prophètes, tous les voyants, disant: Détournez-vous de vos mauvaises voies; et gardez mes commandements, mes statuts, selon toute la loi que j’ai commandée à vos pères et que je vous ai envoyée par mes serviteurs les prophètes.
Yehova anachenjeza Israeli ndi Yuda kudzera mwa aneneri ake onse ndi alosi kuti, “Lekani mchitidwe wanu woyipawo. Mverani malamulo anga ndi malangizo anga potsatira zonse zolembedwa mʼmalamulo a Mose, zimene ndinalamulira makolo anu kuti azimvere, kudzera mwa aneneri, atumiki anga.”
14 Et ils n’écoutèrent pas, et roidirent leur cou comme le cou de leurs pères, qui n’avaient pas cru l’Éternel, leur Dieu.
Koma anthuwa sanamvere ndipo anawumitsa khosi ngati momwe analili makolo awo, amene sanadalire Yehova Mulungu wawo.
15 Et ils rejetèrent ses statuts, et son alliance qu’il avait faite avec leurs pères, et ses témoignages qu’il leur avait donnés, et ils marchèrent après la vanité, et agirent vainement, et en suivant les nations qui étaient autour d’eux, touchant lesquelles l’Éternel leur avait commandé de ne pas faire comme elles.
Anakana malangizo ake ndi pangano anachita ndi makolo awo ndipo ananyoza zochenjeza za Yehova. Iwo anatsatira mafano achabechabe nasanduka achabechabe. Anthuwa anatsanzira mitundu ya anthu owazungulira ngakhale kuti Yehova anawalamula kuti, “Musamachite zomwe iwo amachita,” koma iwo anachita zomwe Yehova anawaletsa.
16 Et ils abandonnèrent tous les commandements de l’Éternel, leur Dieu, et se firent des images de fonte, deux veaux, et se firent des ashères, et se prosternèrent devant toute l’armée des cieux, et servirent Baal.
Iwowo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wawo, nadzipangira mafano awiri osungunula a ana angʼombe ndiponso fano la Asera, napembedza zonse zamlengalenga ndi kutumikira Baala.
17 Et ils firent passer leurs fils et leurs filles par le feu, et pratiquèrent la divination et s’adonnèrent aux enchantements, et se vendirent pour faire ce qui est mauvais aux yeux de l’Éternel, pour le provoquer à colère.
Ndipo anadutsitsa mʼmoto ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo ankawombeza mawula, namachitanso zanyanga ndipo anadzipereka kuchita zoyipa pamaso pa Yehova namukwiyitsa.
18 Et l’Éternel fut très irrité contre Israël, et les ôta de devant sa face; il n’en resta que la seule tribu de Juda.
Choncho Yehova anakwiya nawo kwambiri Aisraeli ndipo anawachotsa pamaso pake. Palibe amene anatsala kupatula fuko la Yuda lokha.
19 Et Juda non plus ne garda pas les commandements de l’Éternel, son Dieu; et ils marchèrent dans les statuts qu’Israël avait établis.
Yuda nayenso sanasunge malamulo a Yehova Mulungu wawo. Iwo ankatsatira machitidwe amene Israeli anayambitsa.
20 Et l’Éternel rejeta toute la semence d’Israël, et il les affligea, et les livra en la main des pillards, jusqu’à ce qu’il les ait rejetés de devant sa face.
Motero Yehova anakana Aisraeli onse. Iye anawazunza nawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha mpaka Iye atawachotseratu pamaso pake.
21 Car Israël s’était séparé de la maison de David, et avait fait roi Jéroboam, fils de Nebath; et Jéroboam avait détourné violemment Israël de suivre l’Éternel, et les avait fait commettre un grand péché.
Yehova atangʼamba Israeli kumuchotsa ku nyumba ya Davide, Aisraeliwo anasankha Yeroboamu mwana wa Nebati kukhala mfumu yawo. Yeroboamu ananyengerera Aisraeli kuti asatsatire Yehova ndipo anawachimwitsa tchimo lalikulu.
22 Et les fils d’Israël marchèrent dans tous les péchés que Jéroboam avait commis; ils ne s’en détournèrent point,
Aisraeli anakakamira machimo onse amene Yeroboamu anachita ndipo sanawasiye
23 jusqu’à ce que l’Éternel ôta Israël de devant sa face, comme il avait dit par tous ses serviteurs les prophètes; et Israël fut transporté de dessus sa terre en Assyrie, [où il est] jusqu’à ce jour.
mpaka pamene Yehova anawachotsa pamaso pake monga anawachenjezera kudzera mwa atumiki ake onse, aneneri. Choncho Aisraeli anachotsedwa mʼdziko lawo kupita ku ukapolo ku Asiriya ndipo ali komweko mpaka lero lino.
24 Et le roi d’Assyrie fit venir [des gens] de Babel, et de Cuth, et d’Avva, et de Hamath, et de Sepharvaïm, et [les] fit habiter dans les villes de la Samarie, à la place des fils d’Israël; et ils possédèrent la Samarie, et habitèrent dans ses villes.
Mfumu ya ku Asiriya inabweretsa anthu a ku Babuloni, Kuta, Awa, Hamati ndi a ku Sefaravaimu kudzawakhazika mʼmizinda ya Samariya kulowa mʼmalo mwa Aisraeli. Iwo anatenga Samariya ndi kukhala mʼmizinda yake.
25 Et il arriva, quand ils commencèrent d’y habiter, qu’ils ne craignaient pas l’Éternel, et l’Éternel envoya contre eux des lions qui les tuaient.
Iwo atayamba kukhala kumeneko, sanapembedze Yehova choncho Yehova anatumiza mikango pakati pawo ndipo inapha ena mwa iwo.
26 Et on parla au roi d’Assyrie, disant: Les nations que tu as transportées et que tu as fait habiter dans les villes de Samarie ne connaissent pas la coutume du dieu du pays, et il a envoyé contre elles des lions, et voici, [ces lions] les font mourir, parce qu’elles ne connaissent pas la coutume du dieu du pays.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inawuzidwa za nkhaniyi kuti, “Anthu amene munawatumiza ndi kuwakhazika mʼmizinda ya Samariya sakudziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna. Choncho Iye watumiza mikango pakati pawo imene ikuwapha chifukwa anthuwo sadziwa chimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
27 Et le roi d’Assyrie commanda, disant: Faites aller là quelqu’un des sacrificateurs que vous en avez transportés; et qu’il aille et qu’il demeure là, et qu’il leur enseigne la coutume du dieu du pays.
Tsono mfumu ya ku Asiriya inalamula kuti, “Tengani wansembe mmodzi mwa amene munawagwira ukapolo, mupite naye kumeneko ndipo akakhale komweko nakaphunzitse anthu zimene Mulungu wa dzikolo amafuna.”
28 Et un des sacrificateurs qu’on avait transportés de Samarie, vint et habita à Béthel, et il leur enseignait comment ils devaient craindre l’Éternel.
Choncho mmodzi mwa ansembe amene anawatenga ku Samariya anabwera kudzakhala ku Beteli ndipo ankaphunzitsa anthuwo kupembedza Yehova.
29 Et chaque nation se fit ses dieux, et elles les placèrent dans les maisons des hauts lieux que les Samaritains avaient faites, chaque nation dans ses villes où elle habitait.
Koma mtundu uliwonse wa anthu unkapangabe mafano a milungu yawoyawo mʼmizinda yambiri imene anthuwo ankakhala, ndipo anayika milunguyo mʼnyumba za milungu zimene anthu a ku Samariya anamanga ku malo opembedzera mafano.
30 Et les hommes de Babel firent Succoth-Benoth; et les hommes de Cuth firent Nergal; et les hommes de Hamath firent Ashima;
Anthu a ku Babuloni anapanga Sukoti-Benoti, anthu a ku Kuti anapanga Nerigali, ndipo anthu a ku Hamati anapanga Asima;
31 et les Avviens firent Nibkhaz et Tharthak; et les Sepharviens brûlaient au feu leurs fils à Adrammélec et à Anammélec, les dieux de Sepharvaïm.
Aava anapanga Nibihazi ndi Taritaki, ndipo Asefaravaimu ankawotcha ana awo pa moto ngati nsembe kwa Adirameleki ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.
32 Et ils craignaient l’Éternel, et se firent d’entre toutes les classes [du peuple] des sacrificateurs des hauts lieux, qui offraient [des sacrifices] pour eux dans les maisons des hauts lieux:
Iwo ankapembedza Yehova, koma ankadzisankhira okha pakati pawo anthu wamba kuti akhale ansembe awo ku nyumba za milungu za ku malo opembedzera mafano.
33 ils craignaient l’Éternel, et ils servaient leurs dieux selon la coutume des nations d’où ils avaient été transportés.
Iwowo ankapembedza Yehova, komanso ankatumikira milungu yawo molingana ndi miyambo ya mitundu ya kumene ankachokera.
34 Jusqu’à ce jour ils font selon leurs premières coutumes: ils ne craignent pas l’Éternel, et ils ne font pas selon leurs statuts et selon leurs coutumes, ni selon la loi et selon le commandement que l’Éternel avait commandés aux fils de Jacob, qu’il nomma Israël.
Mpaka lero lino iwo akupitirizabe kuchita zimene ankachita poyamba. Sapembedza Yehova kapenanso kutsata malangizo ake ndi malamulo ake, chiphunzitso chake monga mwa malamulo amene Yehova anawapereka kwa zidzukulu za Yakobo, amene anamutcha Israeli.
35 Et l’Éternel avait fait alliance avec eux, et il leur avait commandé, disant: Vous ne craindrez point d’autres dieux, et vous ne vous prosternerez point devant eux; et vous ne les servirez point, et ne leur sacrifierez point.
Pamene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli, Iye anawalamula kuti, “Musapembedze milungu ina kapena kuyigwadira iyo, kuyitumikira kapena kupereka nsembe kwa iyoyo.
36 Mais l’Éternel seul, qui vous a fait monter du pays d’Égypte par une grande force et à bras étendu, lui, vous le craindrez, et vous vous prosternerez devant lui, et à lui vous sacrifierez.
Koma Yehova amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndiye amene muyenera kumupembedza.
37 Et les statuts, et les ordonnances, et la loi, et le commandement, qu’il a écrits pour vous, vous prendrez garde à les pratiquer tous les jours; et vous ne craindrez pas d’autres dieux.
Muyenera kusamalitsa nthawi zonse kusunga malangizo anga ndi malemba anga, chiphunzitso ndi malamulo amene anakulemberani. Musapembedze milungu ina.
38 Et vous n’oublierez pas l’alliance que j’ai faite avec vous, et vous ne craindrez pas d’autres dieux;
Musayiwale pangano limene ndinapangana nanu ndipo musamapembedze milungu ina.
39 mais vous craindrez l’Éternel, votre Dieu, et lui vous délivrera de la main de tous vos ennemis.
Mʼmalo mwake muzipembedza Yehova Mulungu wanu pakuti ndiye amene adzakulanditsani mʼdzanja la adani anu onse.”
40 Et ils n’écoutèrent pas, mais ils firent selon leur première coutume.
Komabe iwo sanamvere ndipo anapitiriza kuchita zomwe ankachita kale.
41 Et ces nations-là craignaient l’Éternel, et servaient leurs images; leurs fils aussi, et les fils de leurs fils, font jusqu’à ce jour comme leurs pères ont fait.
Ngakhale anthuwo ankapembedza Yehova, ankatumikiranso mafano awo. Mpaka lero lino ana awo ndi zidzukulu zawo zikupitiriza kuchita zomwe ankachita makolo awo.

< 2 Rois 17 >