< 2 Chroniques 24 >

1 Joas était âgé de sept ans lorsqu’il commença de régner; et il régna 40 ans à Jérusalem; et le nom de sa mère était Tsibia, de Beër-Shéba.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. Dzina la amayi ake linali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 Et Joas fit ce qui est droit aux yeux de l’Éternel, tous les jours de Jehoïada, le sacrificateur.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova nthawi yonse ya moyo wa wansembe Yehoyada.
3 Et Jehoïada prit deux femmes pour [Joas], et il engendra des fils et des filles.
Yehoyada anamupezera iye akazi awiri, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi.
4 Et il arriva, après cela, que Joas eut à cœur de restaurer la maison de l’Éternel.
Patapita nthawi Yowasi anatsimikiza zokonzanso Nyumba ya Yehova.
5 Et il assembla les sacrificateurs et les lévites, et leur dit: Allez par les villes de Juda, et recueillez de l’argent de tout Israël, pour réparer la maison de votre Dieu, d’année en année, et hâtez cette affaire. Mais les lévites ne la hâtèrent point.
Iye anayitanitsa pamodzi ansembe ndi Alevi ndipo anawawuza kuti, “Pitani ku mizinda ya Yuda ndi kukasonkhetsa ndalama za pa chaka kwa Aisraeli onse zokonzera Nyumba ya Mulungu wanu. Chitani zimenezi tsopano.” Koma Alevi sanachite zimenezi mwachangu.
6 Et le roi appela Jehoïada, le chef, et lui dit: Pourquoi n’as-tu pas exigé des lévites qu’ils apportent, de Juda et de Jérusalem, le tribut de Moïse, serviteur de l’Éternel, [imposé à] la congrégation d’Israël pour la tente du témoignage?
Choncho mfumu inayitanitsa Yehoyada, mkulu wa ansembe ndipo inati kwa iye, “Kodi nʼchifukwa chiyani simunawuze Alevi kuti asonkhetse ndalama ku Yuda ndi Yerusalemu, msonkho umene anakhazikitsa Mose mtumiki wa Yehova ndiponso gulu lonse la Aisraeli mu tenti yaumboni?”
7 Car Athalie, cette méchante femme, [et] ses fils, avaient dévasté la maison de Dieu, et, toutes les choses saintes de la maison de l’Éternel, ils les avaient aussi employées pour les Baals.
Ana a mkazi woyipa, Ataliya, anathyola chitseko cha Nyumba ya Mulungu ndipo anagwiritsa ntchito zinthu zopatulika popembedza Baala.
8 Et le roi commanda, et on fit un coffre, et on le mit à la porte de la maison de l’Éternel, en dehors.
Mfumu italamulira, bokosi linapangidwa ndipo linayikidwa panja pa chipata cha Nyumba ya Yehova.
9 Et on publia dans Juda et dans Jérusalem qu’on apporte à l’Éternel le tribut de Moïse, serviteur de Dieu, [imposé] à Israël, dans le désert.
Ndipo analengeza kwa anthu a mu Yuda ndi mu Yerusalemu kuti abweretse kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu analamulira Aisraeli mʼchipululu.
10 Et tous les princes et tout le peuple s’en réjouirent; et ils apportèrent [l’argent] et le jetèrent dans le coffre, jusqu’à ce qu’on ait fini.
Akuluakulu onse ndi anthu onse anabweretsa zopereka zawo mokondwera ndipo anaziponya mʼbokosi mpaka linadzaza.
11 Et il arrivait que, lorsque c’était le temps d’apporter le coffre au contrôle du roi, par la main des lévites, et qu’on voyait qu’il y avait beaucoup d’argent, le secrétaire du roi et l’officier du principal sacrificateur venaient et vidaient le coffre; et ils le reportaient et le remettaient à sa place. Ils faisaient ainsi jour par jour, et on recueillit de l’argent en abondance.
Nthawi ina iliyonse imene Alevi abweretsa bokosilo kwa akuluakulu a mfumu ndipo akaona kuti muli ndalama zambiri, mlembi waufumu ndi nduna yayikulu ya mkulu wa ansembe amabwera ndi kuchotsa ndalama mʼbokosi muja ndipo amalitenga kukaliyika pamalo pake. Iwo amachita izi nthawi ndi nthawi ndipo anapeza ndalama zambiri.
12 Et le roi et Jehoïada le donnaient à ceux qui faisaient l’ouvrage du service de la maison de l’Éternel, et ceux-ci prenaient à gage des tailleurs de pierres et des charpentiers pour restaurer la maison de l’Éternel, et aussi des ouvriers en fer et en airain pour réparer la maison de l’Éternel.
Mfumu pamodzi ndi Yehoyada anapereka ndalamazo kwa anthu oyangʼanira ntchito ku Nyumba ya Yehova. Analemba ntchito amisiri a miyala ndi a matabwa kuti akonzenso Nyumba ya Yehova. Analembanso ntchito amisiri a zitsulo ndi mkuwa kuti akonze Nyumba ya Mulungu.
13 Et ceux qui faisaient l’ouvrage travaillèrent, et l’œuvre de restauration se fit par leur moyen, et ils rétablirent la maison de Dieu en son état, et la consolidèrent.
Anthu amene ankagwira ntchito anali odziwa bwino, ndipo ntchitoyo inagwiridwa bwino ndi manja awo. Iwo anamanganso Nyumba ya Mulungu motsatira mapangidwe ake oyamba ndipo anayilimbitsa.
14 Et quand ils eurent achevé, ils apportèrent devant le roi et devant Jehoïada le reste de l’argent; et on en fit des ustensiles pour la maison de l’Éternel, des ustensiles pour le service et pour les holocaustes, et des coupes, et des ustensiles d’or et d’argent. Et on offrit des holocaustes dans la maison de l’Éternel continuellement, tous les jours de Jehoïada.
Atamaliza, iwo anabweretsa ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, ndipo anazigwiritsira ntchito popangira zida za mʼNyumba ya Yehova: ziwiya zogwiritsa ntchito potumikira ndi popereka nsembe zopsereza, komanso mbale ndi ziwiya zagolide ndi siliva. Nthawi yonse ya moyo wa Yehoyada, nsembe zopsereza zinkaperekedwa mosalekeza mʼNyumba ya Yehova.
15 Et Jehoïada devint vieux et rassasié de jours, et il mourut. Il était âgé de 130 ans quand il mourut.
Tsono Yehoyada anakalamba ndipo anali ndi zaka zambiri. Pambuyo pake iye anamwalira ali ndi zaka 130.
16 Et on l’enterra dans la ville de David avec les rois, car il avait fait du bien en Israël, et pour Dieu et pour sa maison.
Iyeyo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu mu mzinda wa Davide chifukwa cha zabwino zimene anachita mu Israeli, kuchitira Mulungu ndi Nyumba yake.
17 Et après la mort de Jehoïada, les chefs de Juda vinrent et s’inclinèrent devant le roi; alors le roi les écouta.
Atamwalira Yehoyada, akuluakulu a Yuda anabwera kudzapereka ulemu kwa mfumu, ndipo mfumu inawamvera.
18 Et ils abandonnèrent la maison de l’Éternel, le Dieu de leurs pères, et servirent les ashères et les idoles; et il y eut de la colère contre Juda et contre Jérusalem, parce qu’ils s’étaient rendus coupables en cela.
Iwo anasiya Nyumba ya Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anapembedza Asera ndi mafano. Chifukwa cha kulakwa kwawo, mkwiyo wa Yehova unabwera pa Yuda ndi Yerusalemu.
19 Et l’Éternel envoya parmi eux, pour les ramener à lui, des prophètes qui témoignèrent contre eux; mais ils n’écoutèrent point.
Ngakhale Yehova anatumiza aneneri kwa anthuwo kuti awabweze kwa Iye, ngakhale aneneri ananenera mowatsutsa, anthuwo sanamvere.
20 Et l’Esprit de Dieu revêtit Zacharie, fils de Jehoïada, le sacrificateur, et il se tint debout au-dessus du peuple, et leur dit: Ainsi dit Dieu: Pourquoi transgressez-vous les commandements de l’Éternel? Vous ne réussirez point; car vous avez abandonné l’Éternel, et il vous abandonnera aussi.
Kenaka Mzimu wa Mulungu unabwera pa Zekariya mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anayimirira pamaso pa anthu ndipo anati, “Zimene Mulungu akunena ndi Izi: ‘Chifukwa chiyani simukumvera Malamulo a Yehova? Simudzapindula. Chifukwa mwasiya Yehova, Iyenso wakusiyani.’”
21 Et ils conspirèrent contre lui, et le lapidèrent avec des pierres par l’ordre du roi, dans le parvis de la maison de l’Éternel.
Koma anthuwo anamuchitira chiwembu molamulidwa ndi mfumu ndipo anamugenda miyala ndi kumupha mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
22 Et le roi Joas ne se souvint pas de la bonté dont Jehoïada, père de Zacharie, avait usé envers lui, et il tua son fils. Et comme il mourait, il dit: Que l’Éternel regarde et redemande!
Mfumu Yowasi sinakumbukire zabwino zimene Yehoyada abambo ake a Zekariya anamuchitira, koma anapha mwana wake. Pamene amafa, iye ananena kuti, “Yehova aone zimenezi ndipo abwezere chilango.”
23 Et il arriva, quand l’année fut révolue, que l’armée de Syrie monta contre Joas, et entra en Juda et à Jérusalem; et ils détruisirent d’entre le peuple tous les chefs du peuple, et envoyèrent toutes leurs dépouilles au roi, à Damas.
Pakutha kwa chaka, gulu lankhondo la Aramu linadzamenyana ndi Yowasi. Linalowa mu Yuda ndi mu Yerusalemu ndi kupha atsogoleri onse a anthu. Zonse zimene analanda anazitumiza kwa mfumu ya ku Damasiko.
24 Car l’armée de Syrie vint avec un petit nombre d’hommes, et l’Éternel livra en leurs mains une très grande armée, parce qu’ils avaient abandonné l’Éternel, le Dieu de leurs pères. Ainsi [les Syriens] firent justice de Joas.
Ngakhale kuti gulu lankhondo la Aramu linabwera ndi anthu ochepa okha, Yehova anapereka mʼmanja mwawo gulu lalikulu lankhondo. Chifukwa Yuda anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, chiweruzo chinachitika pa Yowasi.
25 Et quand ils l’eurent quitté, (or ils l’avaient laissé dans de grandes maladies, ) ses serviteurs conspirèrent contre lui, à cause du sang des fils de Jehoïada, le sacrificateur; et ils le tuèrent sur son lit, et il mourut; et on l’enterra dans la ville de David, mais on ne l’enterra pas dans les sépulcres des rois.
Pamene Aaramu amachoka, anasiya Yowasi atavulazidwa kwambiri. Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu chifukwa anapha mwana wa wansembe Yehoyada, ndipo anamupha ali pa bedi pake. Choncho anafa ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati manda a mafumu.
26 Et ce sont ici ceux qui conspirèrent contre lui: Zabad, fils de Shimhath, l’Ammonite, et Jozabad, fils de Shimrith, la Moabite.
Iwo amene anamuchitira chiwembu anali Zabadi mwana wa Simeati, mkazi wa ku Amoni, ndi Yehozabadi mwana wa Simiriti, mkazi wa ku Mowabu.
27 Et quant à ses fils, et à la grandeur du tribut qui lui fut imposé, et aux constructions de la maison de Dieu, voici, ces choses sont écrites dans les commentaires du livre des rois. Et Amatsia, son fils, régna à sa place.
Za ana ake aamuna, uneneri wonena za iye, mbiri ya kumanganso Nyumba ya Mulungu, zalembedwa mʼbuku lofotokoza za mafumu. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Chroniques 24 >