< 2 Chroniques 23 >
1 Et la septième année, Jehoïada se fortifia, et fit un pacte avec les chefs de centaines, Azaria, fils de Jerokham, et Ismaël, fils de Jokhanan, et Azaria, fils d’Obed, et Maascéïa, fils d’Adaïa, et Élishaphat, fils de Zicri.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 Et ils firent le tour de Juda, et assemblèrent les lévites de toutes les villes de Juda, et les chefs des pères d’Israël; et ils vinrent à Jérusalem.
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 Et toute la congrégation fit alliance avec le roi dans la maison de Dieu; et [Jehoïada] leur dit: Voici, le fils du roi régnera, selon ce que l’Éternel a dit touchant les fils de David.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 C’est ici ce que vous ferez: un tiers d’entre vous qui entrez le [jour du] sabbat, sacrificateurs et lévites, sera chargé de la garde des seuils;
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 et un tiers sera dans la maison du roi; et un tiers à la porte de Jesod; et tout le peuple sera dans les parvis de la maison de l’Éternel.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Et que personne n’entre dans la maison de l’Éternel, sauf les sacrificateurs et les lévites qui feront le service: eux, ils entreront, car ils sont saints; et tout le peuple fera l’acquit de la charge de l’Éternel.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Et les lévites entoureront le roi de tous côtés, chacun ses armes à la main; et celui qui entrera dans la maison sera mis à mort; et soyez avec le roi quand il entrera et quand il sortira.
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Et les lévites et tout Juda firent selon tout ce que Jehoïada, le sacrificateur, avait commandé; et ils prirent chacun ses hommes, ceux qui entraient le [jour du] sabbat et ceux qui sortaient le [jour du] sabbat; car Jehoïada, le sacrificateur, n’avait pas renvoyé les classes.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Et Jehoïada, le sacrificateur, donna aux chefs de centaines les lances, et les écus, et les boucliers, qui avaient appartenu au roi David, et qui étaient dans la maison de Dieu.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 Et il fit tenir là tout le peuple, chacun sa javeline à la main, depuis le côté droit de la maison jusqu’au côté gauche de la maison, vers l’autel et vers la maison, auprès du roi, tout autour.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Et ils firent sortir le fils du roi, et mirent sur lui la couronne et le témoignage; et ils le firent roi; et Jehoïada et ses fils l’oignirent, et dirent: Vive le roi!
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 Et Athalie entendit le cri du peuple qui courait et acclamait le roi, et elle entra vers le peuple dans la maison de l’Éternel.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 Et elle regarda, et voici, le roi se tenait sur son estrade, à l’entrée, et les chefs et les trompettes étaient auprès du roi, et tout le peuple du pays se réjouissait et sonnait des trompettes, et les chantres [étaient là] avec des instruments de musique, et ceux qui enseignaient à louer [Dieu]. Et Athalie déchira ses vêtements, et dit: Conspiration! Conspiration!
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Et Jehoïada, le sacrificateur, fit sortir les chefs de centaines qui étaient préposés sur l’armée, et leur dit: Faites-la sortir en dehors des rangs, et que celui qui la suivra soit mis à mort par l’épée; car le sacrificateur dit: Ne la mettez pas à mort dans la maison de l’Éternel.
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 Et ils lui firent place; et elle alla par l’entrée de la porte des chevaux dans la maison du roi, et là ils la mirent à mort.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Et Jehoïada fit une alliance entre lui et tout le peuple et le roi, qu’ils seraient le peuple de l’Éternel.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Et tout le peuple entra dans la maison de Baal, et ils la démolirent; et ils brisèrent ses autels et ses images, et tuèrent devant les autels Matthan, sacrificateur de Baal.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Et Jehoïada mit les charges de la maison de l’Éternel entre les mains des sacrificateurs lévites, que David avait établis par classes sur la maison de l’Éternel pour offrir les holocaustes à l’Éternel, comme il est écrit dans la loi de Moïse, avec joie et avec des cantiques, selon les directions de David.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 Et il plaça les portiers aux portes de la maison de l’Éternel, afin qu’il n’y entre aucune personne impure en quoi que ce soit.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 Et il prit les chefs de centaines, et les nobles, et ceux qui avaient autorité sur le peuple, et tout le peuple du pays, et il fit descendre le roi de la maison de l’Éternel, et ils entrèrent dans la maison du roi par la porte supérieure; et ils firent asseoir le roi sur le trône du royaume.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Et tout le peuple du pays se réjouit, et la ville fut tranquille: et ils avaient mis à mort Athalie par l’épée.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.