< 2 Chroniques 19 >
1 Et Josaphat, roi de Juda, s’en retourna dans sa maison, en paix, à Jérusalem.
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 Et Jéhu, fils de Hanani, le voyant, sortit au-devant de lui, et dit au roi Josaphat: Aides-tu au méchant, et aimes-tu ceux qui haïssent l’Éternel? À cause de cela il y a colère sur toi de la part de l’Éternel.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Cependant il s’est trouvé de bonnes choses en toi, car tu as ôté du pays les ashères, et tu as appliqué ton cœur à rechercher Dieu.
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 Et Josaphat habita à Jérusalem. Et de nouveau il sortit parmi le peuple, depuis Beër-Shéba jusqu’à la montagne d’Éphraïm; et il les ramena à l’Éternel, le Dieu de leurs pères.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 Et il établit des juges dans le pays, dans toutes les villes fortes de Juda, de ville en ville.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 Et il dit aux juges: Voyez ce que vous ferez; car ce n’est pas pour l’homme que vous jugerez, mais pour l’Éternel, et il sera avec vous dans ce qui concerne le jugement.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Et maintenant, que la frayeur de l’Éternel soit sur vous: prenez garde en agissant; car auprès de l’Éternel, notre Dieu, il n’y a point d’iniquité, ni acception de personnes, ni acceptation de présents.
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 Et à Jérusalem aussi, Josaphat établit des lévites, et des sacrificateurs, et des chefs des pères d’Israël, pour le jugement de l’Éternel et pour les procès. Et ils étaient revenus à Jérusalem.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 Et il leur commanda, disant: Vous agirez ainsi dans la crainte de l’Éternel, avec fidélité et d’un cœur parfait.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 Et quelque procès qui vienne devant vous de la part de vos frères qui habitent dans leurs villes, entre sang et sang, entre loi et commandement, statuts et ordonnances, vous les avertirez afin qu’ils ne se rendent pas coupables envers l’Éternel, et qu’il n’y ait pas de la colère contre vous et contre vos frères: vous agirez ainsi, et vous ne vous rendrez pas coupables.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 Et voici, Amaria, le principal sacrificateur, est [préposé] sur vous dans toutes les affaires de l’Éternel, et Zebadia, fils d’Ismaël, prince de la maison de Juda, dans toutes les affaires du roi; et vous avez devant vous, pour officiers, les lévites. Fortifiez-vous, et agissez, et l’Éternel sera avec l’[homme] de bien.
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”