< 1 Samuel 21 >

1 Et David vint à Nob, auprès d’Akhimélec, le sacrificateur; et Akhimélec trembla en rencontrant David, et lui dit: Pourquoi es-tu seul et n’y a-t-il personne avec toi?
Davide anapita ku Nobi kwa wansembe Ahimeleki. Ahimelekiyo ankanjenjemera pamene ankamuchingamira, ndipo anafunsa kuti, “Muli nokha chifukwa chiyani? Chifukwa chiyani mulibe wokuperekezani?”
2 Et David dit à Akhimélec, le sacrificateur: Le roi m’a commandé quelque chose, et m’a dit: Que personne ne sache rien de l’affaire pour laquelle je t’envoie, ni de ce que je t’ai commandé. Et j’ai indiqué à mes jeunes hommes un certain lieu.
Davide anayankha Ahimeleki kuti, “Mfumu yandituma zinthu zina ndipo yandiwuza kuti, ‘Munthu aliyense asadziwe za zimene ndakutumazo.’ Kunena za anthu anga, ndawawuza kuti tikakumane pamalo pena pake.
3 Et maintenant, qu’as-tu sous la main? Donne-moi dans la main cinq pains, ou ce qui se trouvera.
Kodi muli ndi chakudya? Patseniko malofu a buledi asanu, kapena chilichonse muli nacho.”
4 Et le sacrificateur répondit à David, et dit: Je n’ai point sous la main de pain commun, il n’y a que du pain sacré; si seulement les jeunes hommes se sont gardés des femmes!
Koma wansembeyo anamuyankha Davide kuti, “Ine ndilibe buledi wamba woti ndikupatseni. Koma pali buledi wachipembedzo yekha. Ngati anthu amene muli nawo sanagone ndi akazi awo mukhoza kudya.”
5 Et David répondit au sacrificateur, et lui dit: Oui, nous avons été privés des femmes depuis deux ou trois jours que je suis sorti, et les vases de mes jeunes hommes sont saints; et le [pain] est en quelque sorte commun, vu qu’on en consacre [de nouveau] dans les vases aujourd’hui.
Davide anayankha kuti, “Kunena zoona sitinakhudzane ndi mkazi monga timachitira nthawi zonse tikakhala pa ulendo. Anthu anga salola kudziyipitsa ndi mkazi ngakhale pa ulendo wamba. Nanji lero tili pa ulendo woterewu!”
6 Et le sacrificateur lui donna du [pain] sacré, car il n’y avait point là d’autre pain que le pain de proposition qui avait été ôté de devant l’Éternel pour remettre du pain chaud le jour où on levait l’autre.
Choncho wansembe uja anamupatsa buledi wachipembedzo popeza kunalibeko buledi wina aliyense koma yekhayo amene amaperekedwa kwa Yehova. Uyu ndi amene anachotsedwa tsiku limenelo kuti ayikepo wina wotentha.
7 Et il y avait là un homme d’entre les serviteurs de Saül, retenu ce jour-là devant l’Éternel, et son nom était Doëg, l’Édomite; il était le chef des bergers de Saül.
Koma tsiku limenelo mmodzi wa antchito a Sauli anali pomwepo kudikirira kuti achite mwambo wa chipembedzo mʼnyumba ya Mulungu. Munthuyu dzina lake anali Doegi Mwedomu, munthu wamphamvu pakati pa abusa a Sauli.
8 Et David dit à Akhimélec: N’as-tu pas ici sous la main une lance ou une épée? car je n’ai pris dans ma main ni mon épée ni mes armes, parce que l’affaire du roi était pressante.
Davide anafunsa Ahimeleki kuti, “Kodi muli ndi mkondo kapena lupanga pano? Ine sindinatenge lupanga langa kapena chida china chilichonse chifukwa zimene andituma amfumu ndi zamsangamsanga.”
9 Et le sacrificateur dit: L’épée de Goliath, le Philistin, que tu as frappé dans la vallée d’Éla, la voilà, enveloppée dans un manteau derrière l’éphod: si tu veux la prendre, prends-la; car il n’y en a point d’autre ici que celle-là. Et David dit: Il n’y en a point de pareille; donne-la-moi.
Wansembeyo anayankha kuti, “Kuno kuli lupanga la Goliati Mfilisiti uja amene unamupha mʼchigwa cha Ela, lakulungidwa mʼnsalu paseli pa Efodi. Ngati mufuna kulitenga, tengani popeza kuno kulibe lina koma lokhalo.” Davide anati, “Palibe lina lofanana nalo. Ndipatseni lomwelo.”
10 Et David se leva et s’enfuit ce jour-là de devant Saül, et vint vers Akish, roi de Gath.
Tsiku lomwelo Davide ananyamuka kuthawa Sauli ndipo anapita kwa Akisi, mfumu wa ku Gati.
11 Et les serviteurs d’Akish lui dirent: N’est-ce pas là David, le roi du pays? N’est-ce pas au sujet de celui-ci qu’on s’entre-répondait dans les danses, en disant: Saül a frappé ses 1 000, et David ses 10 000?
Koma nduna za Akisi zinafunsa mfumuyo kuti, “Kodi uyu si Davide mfumu ya dzikoli? Kodi iyeyu si uja pomuvinira ankayimba kuti, “Sauli wapha 1,000, koma Davide wapha miyandamiyanda?”
12 Et David prit à cœur ces paroles, et il eut très peur d’Akish, roi de Gath.
Mawu amenewa anamulowa kwambiri Davide mu mtima ndipo anayamba kuopa kwambiri Akisi mfumu ya ku Gati.
13 Et il se contrefit devant eux, et fit l’insensé entre leurs mains; il marquait les battants de la porte, et laissait couler sa salive sur sa barbe.
Choncho anasintha makhalidwe ake pamaso pawo, nʼkudzisandutsa ngati wamisala. Iye ankangolembalemba pa zitseko za chipata ndi kumangotuluka dovi, nʼkumayenderera mʼndevu zake.
14 Et Akish dit à ses serviteurs: Voici, vous voyez que cet homme est fou. Pourquoi me l’avez-vous amené?
Akisi anawuza nduna zake kuti, “Mukumuona munthu uyu kuti ndi wamisala! Nʼchifukwa chiyani mukubwera naye kwa ine?
15 Manqué-je de fous, moi, que vous m’ayez amené celui-ci pour faire le fou devant moi? Celui-ci entrerait-il dans ma maison?
Kodi ine ndikusowa anthu amisala kuti muzibwera naye munthuyu kwa ine kuti azidzachita zamisala zake pamaso panga? Kodi munthu ameneyu nʼkulowa mʼnyumba mwanga?”

< 1 Samuel 21 >