< 1 Chroniques 13 >

1 Et David tint conseil avec les chefs de milliers et de centaines, avec tous les princes.
Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100.
2 Et David dit à toute la congrégation d’Israël: Si cela est bon devant vous, et que cela vienne de l’Éternel, notre Dieu, envoyons de tous côtés vers nos autres frères qui restent dans tous les pays d’Israël, et, en même temps, vers les sacrificateurs et les lévites, dans leurs villes et leurs banlieues, afin qu’ils se rassemblent auprès de nous,
Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe.
3 et ramenons à nous l’arche de notre Dieu; car nous ne l’avons pas consultée aux jours de Saül.
Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.”
4 Et toute la congrégation dit qu’on fasse ainsi; car la chose était bonne aux yeux de tout le peuple.
Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.
5 Et David assembla tout Israël, depuis le Shikhor d’Égypte jusqu’à l’entrée de Hamath, pour faire venir de Kiriath-Jéarim l’arche de Dieu.
Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu.
6 Et David monta, et tout Israël, à Baala, à Kiriath-Jéarim, qui appartient à Juda, pour en faire monter l’arche de Dieu, l’Éternel, qui siège entre les chérubins, duquel le nom est placé [là].
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.
7 Et ils montèrent l’arche de Dieu sur un chariot neuf, [et l’emmenèrent] de la maison d’Abinadab; et Uzza et Akhio conduisaient le chariot.
Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo.
8 Et David et tout Israël s’égayaient devant Dieu de toute leur force, avec des cantiques, et des harpes, et des luths, et des tambourins, et des cymbales, et des trompettes.
Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.
9 Et ils arrivèrent à l’aire de Kidon, et Uzza étendit sa main pour saisir l’arche, parce que les bœufs avaient bronché.
Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa.
10 Et la colère de l’Éternel s’embrasa contre Uzza, et il le frappa, parce qu’il avait étendu sa main sur l’arche; et il mourut là devant Dieu.
Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.
11 Alors David fut irrité, car l’Éternel avait fait une brèche en [la personne d’]Uzza; et il appela ce lieu-là du nom de Pérets-Uzza, [qui lui est resté] jusqu’à ce jour.
Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.
12 Et David eut peur de Dieu en ce jour-là, disant: Comment ferais-je entrer chez moi l’arche de Dieu?
Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?”
13 Et David ne retira pas l’arche chez lui dans la ville de David, mais il la fit détourner dans la maison d’Obed-Édom, le Guitthien.
Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti.
14 Et l’arche de Dieu demeura trois mois avec la famille d’Obed-Édom, dans sa maison; et l’Éternel bénit la maison d’Obed-Édom et tout ce qui lui appartenait.
Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.

< 1 Chroniques 13 >