< Psaumes 96 >
1 Chantez à Yahweh un cantique nouveau! Chantez à Yahweh, vous habitants de toute la terre!
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Chantez à Yahweh, bénissez son nom! Annoncez de jour en jour son salut,
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Racontez sa gloire parmi les nations, ses merveilles parmi tous les peuples.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Car Yahweh est grand et digne de toute louange, il est redoutable par dessus tous les dieux,
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 car tous les dieux des peuples sont néant. Mais Yahweh a fait les cieux.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 La splendeur et la magnificence sont devant lui, la puissance et la majesté sont dans son sanctuaire.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Rendez à Yahweh, famille des peuples, rendez à Yahweh gloire et puissance!
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Rendez à Yahweh la gloire due à son nom! Apportez l’offrande et venez dans ses parvis.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Prosternez-vous devant Yahweh avec l’ornement sacré; tremblez devant lui, vous, habitants de toute la terre!
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Dites parmi les nations: « Yahweh est roi; aussi le monde sera stable et ne chancellera pas; il jugera les peuples avec droiture. »
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Que les cieux se réjouissent et que la terre soit dans l’allégresse! Que la mer s’agite avec tout ce qu’elle contient!
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Que la campagne s’égaie avec tout ce qu’elle renferme, que tous les arbres des forêts poussent des cris de joie,
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 devant Yahweh, car il vient! Car il vient pour juger la terre; il jugera le monde avec justice, et les peuples selon sa fidélité.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.