< Psaumes 85 >

1 Au maître de chant. Psaume des fils de Coré. Tu as été favorable à ton pays, Yahweh, tu as ramené les captifs de Jacob;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 tu as pardonné l’iniquité à ton peuple, tu as couvert tous ses péchés; — Séla.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 tu as retiré toute ton indignation, tu es revenu de l’ardeur de ta colère.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Rétablis-nous, Dieu de notre salut; mets fin à ton sentiment contre nous.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Seras-tu toujours irrité contre nous, prolongeras-tu ton courroux éternellement?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Ne nous feras-tu pas revenir à la vie, afin que ton peuple se réjouisse en toi?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Yahweh, fais-nous voir ta bonté, et accorde-nous ton salut.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Je veux écouter ce que dira le Dieu Yahweh: — Il a des paroles de paix pour son peuple et pour ses fidèles; pourvu qu’ils ne retournent pas à leur folie. —
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Oui, son salut est proche de ceux qui le craignent, et la gloire habitera de nouveau dans notre pays.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 La bonté et la vérité vont se rencontrer, la justice et la paix s’embrasseront.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 La vérité germera de la terre, et la justice regardera du haut du ciel.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Yahweh lui-même accordera tout bien, et notre terre donnera son fruit.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 La justice marchera devant lui, et tracera le chemin à ses pas.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psaumes 85 >