< Psaumes 58 >
1 Au maître de chant. Ne détruis pas. Hymne de David. Est-ce donc en restant muets que vous rendez la justice? Est-ce selon le droit que vous jugez, fils des hommes?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Non: au fond du cœur vous tramez vos desseins iniques, dans le pays vous vendez au poids la violence de vos mains.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Les méchants sont pervertis dès le sein maternel, dès leur naissance, les fourbes se sont égarés.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Leur venin est semblable au venin du serpent, de la vipère sourde qui ferme ses oreilles,
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 et n’entend pas la voix de l’enchanteur, du charmeur habile dans son art.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Ô Dieu brise leurs dents dans leur bouche; Yahweh, arrache les mâchoires des lionceaux!
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Qu’ils se dissipent comme le torrent qui s’écoule! S’ils ajustent des flèches, qu’elles s’émoussent!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Qu’ils soient comme la limace qui va en se fondant! Comme l’avorton d’une femme, qu’ils ne voient point le soleil!
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Avant que vos chaudières sentent l’épine, verte ou enflammée, l’ouragan l’emportera.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Le juste sera dans la joie, à la vue de la vengeance, il baignera ses pieds dans le sang des méchants.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Et l’on dira: « Oui, il y a une récompense pour le juste; oui, il y a un Dieu qui juge sur la terre! »
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”