< Psaumes 41 >

1 Au maître de chant. Psaume de David. Heureux celui qui prend souci du pauvre! Au jour du malheur, Yahweh le délivrera.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
2 Yahweh le gardera et le fera vivre; il sera heureux sur la terre, et tu ne le livreras pas au désir de ses ennemis.
Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
3 Yahweh l'assistera sur son lit de douleur; tu retourneras toute sa couche dans sa maladie.
Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
4 Moi, je dis: " Yahweh, aie pitié de moi! guéris mon âme, car j'ai péché contre toi! "
Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
5 Et mes ennemis profèrent contre moi des malédictions: " Quand mourra-t-il? Quand périra son nom? "
Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
6 Si quelqu'un vient me visiter, il ne profère que mensonges; son cœur recueille l'iniquité; quand il s'en va, il parle au dehors.
Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
7 Tous mes ennemis chuchotent ensemble contre moi, contre moi ils méditent le malheur.
Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
8 " Un mal irrémédiable, disent-ils, a fondu sur lui; le voilà couché, il ne se relèvera plus! "
“Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
9 Même l'homme qui était mon ami, qui avait ma confiance et qui mangeait mon pain, lève le talon contre moi.
Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
10 Toi, Yahweh, aie pitié de moi et relève-moi, et je leur rendrai ce qu'ils méritent.
Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 Je connaîtrai que tu m'aimes, si mon ennemi ne triomphe pas de moi.
Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 A cause de mon innocence, tu m'as soutenu, et tu m'as établi pour toujours en ta présence.
Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
13 Béni soit Yahweh, le Dieu d'Israël, dans les siècles des siècles! Amen! Amen!
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.

< Psaumes 41 >