< Psaumes 37 >

1 De David. ALEPH. Ne t’irrite pas au sujet des méchants, ne porte pas envie à ceux qui font le mal.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Car, comme l’herbe, ils seront vite coupés; comme la verdure du gazon, ils se dessécheront. BETH.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Mets ta confiance en Yahweh, et fais le bien; habite le pays, et jouis de sa fidélité.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Fais de Yahweh tes délices, et il te donnera ce que ton cœur désire. GHIMEL.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Remets ton sort à Yahweh et confie-toi en lui: il agira:
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 il fera resplendir ta justice comme la lumière, et ton droit comme le soleil à son midi. DALETH.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Tiens-toi en silence devant Yahweh, et espère en lui; ne t’irrite pas au sujet de celui qui prospère dans ses voies; de l’homme qui réussit en ses intrigues. HÉ.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Laisse la colère, abandonne la fureur; ne t’irrite pas, pour n’aboutir qu’au mal.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Car les méchants seront retranchés, mais ceux qui espèrent en Yahweh posséderont le pays. VAV.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Encore un peu de temps, et le méchant n’est plus; tu regardes sa place, et il a disparu.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Mais les doux posséderont la terre, ils goûteront les délices d’une paix profonde. ZAÏN.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Le méchant forme des projets contre le juste, il grince les dents contre lui.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 Le Seigneur se rit du méchant, car il voit que son jour arrive. HETH.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Les méchants tirent le glaive, ils bandent leur arc; pour abattre le malheureux et le pauvre, pour égorger ceux dont la voie est droite.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Leur glaive entrera dans leur propre cœur, et leurs arcs se briseront. TETH.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Mieux vaut le peu du juste, que l’abondance de nombreux méchants;
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 car les bras des méchants seront brisés, et Yahweh soutient les justes. YOD.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Yahweh connaît les jours des hommes intègres, et leur héritage dure à jamais.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Ils ne sont pas confondus au jour du malheur, et ils sont rassasiés aux jours de la famine. CAPH.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Car les méchants périssent; les ennemis de Yahweh sont comme la gloire des prairies; ils s’évanouissent en fumée, ils s’évanouissent. LAMED.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Le méchant emprunte, et il ne rend pas;
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Car ceux que bénit Yahweh possèdent le pays, et ceux qu’il maudit sont retranchés. MEM.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Yahweh affermit les pas de l’homme juste, et il prend plaisir à sa voie.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 S’il tombe, il n’est pas étendu par terre, car Yahweh soutient sa main. NUN.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 J’ai été jeune, me voilà vieux, et je n’ai point vu le juste abandonné; ni sa postérité mendiant son pain.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Toujours il est compatissant, et il prête, et sa postérité est en bénédiction. SAMECH.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Détourne-toi du mal et fais le bien; et habite à jamais ta demeure.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Car Yahweh aime la justice, et il n’abandonne pas ses fidèles. Ils sont toujours sous sa garde, mais la postérité des méchants sera retranchée.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Les justes posséderont le pays, et ils y habiteront à jamais. PHÉ.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 La bouche du juste annonce la sagesse, et sa langue proclame la justice.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 La loi de son Dieu est dans son cœur; ses pas ne chancellent point. TSADÉ.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Le méchant épie le juste, et il cherche à le faire mourir.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Yahweh ne l’abandonne pas entre ses mains, et il ne le condamne pas quand vient son jugement. QOPH.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Attends Yahweh et garde sa voie, et il t’élèvera et tu posséderas le pays; quand les méchants seront retranchés, tu le verras. RESCH.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 J’ai vu l’impie au comble de la puissance; il s’étendait comme un arbre verdoyant.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 J’ai passé, et voici qu’il n’était plus; je l’ai cherché, et on ne l’a plus trouvé. SCHIN.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Observe celui qui est intègre, et regarde celui qui est droit; car il y a une postérité pour l’homme de paix.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Mais les rebelles seront tous anéantis, la postérité des méchants sera retranchée. THAV.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 De Yahweh vient le salut des justes; il est leur protecteur au temps de la détresse.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Yahweh leur vient en aide et les délivre; il les délivre des méchants et les sauve, parce qu’ils ont mis en lui leur confiance.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psaumes 37 >