< Psaumes 3 >

1 Chant de David. A l'occasion de sa fuite devant Absalon, son fils Yahweh, que mes ennemis sont nombreux! Quelle multitude se lève contre moi!
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 Nombreux sont ceux qui disent à mon sujet: " Plus de salut pour lui auprès de Dieu! " — Séla.
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Mais toi, Yahweh, tu es mon bouclier; tu es ma gloire, et tu relèves ma tête.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 De ma voix je crie vers Yahweh, et il me répond de sa montagne sainte. — Séla.
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Je me suis couché et me suis endormi; je me suis réveillé, car Yahweh est mon soutien.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 je ne crains pas devant le peuple innombrable, qui m'assiège de toutes parts.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Lève-toi, Yahweh! Sauve-moi, mon Dieu! Car tu frappes à la joue tous mes ennemis, tu brises les dents des méchants.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 A Yahweh le salut! Que ta bénédiction soit sur ton peuple! — Séla.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Psaumes 3 >