< Psaumes 133 >

1 Cantique des montées. De David. Ah! Qu’il est bon, qu’il est doux pour des frères d’habiter ensemble!
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!
2 C’est comme l’huile précieuse qui, répandue sur la tête, coule sur la barbe, sur la barbe d’Aaron, qui descend sur le bord de son vêtement.
Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu, otsikira ku ndevu, ku ndevu za Aaroni, oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.
3 C’est comme la rosée de l’Hermon, qui descend sur les sommets de Sion. Car c’est là que Yahweh a établi la bénédiction, la vie, pour toujours.
Zili ngati mame a ku Heremoni otsikira pa Phiri la Ziyoni. Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso, ndiwo moyo wamuyaya.

< Psaumes 133 >