< Psaumes 12 >
1 Au maître de chant. Sur l’octave. Chant de David. Sauve, Yahweh! car les hommes pieux s’en vont, les fidèles disparaissent d’entre les enfants des hommes.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
2 On se dit des mensonges les uns aux autres; on parle avec des lèvres flatteuses et un cœur double.
Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
3 Que Yahweh retranche toutes les lèvres flatteuses, la langue qui discourt avec jactance,
Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
4 ceux qui disent: « Par notre langue nous sommes forts; nous avons avec nous nos lèvres: qui serait notre maître? »
Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
5 « À cause de l’oppression des affligés, du gémissement des pauvres, je veux maintenant me lever, dit Yahweh; je leur apporterai le salut après lequel ils soupirent. »
“Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
6 Les paroles de Yahweh sont des paroles pures, un argent fondu dans un creuset sur la terre, sept fois purifié.
Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
7 Toi, Yahweh, tu les garderas; tu les préserveras à jamais de cette génération.
Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
8 Autour d’eux les méchants se promènent avec arrogance: autant ils s’élèvent, autant seront humiliés les enfants des hommes.
Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.