< Proverbes 17 >
1 Mieux vaut un morceau de pain sec avec la paix, qu’une maison pleine de viande avec la discorde.
Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere, kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.
2 Un serviteur prudent l’emporte sur le fils qui fait honte, et il partagera l’héritage avec les frères.
Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi, ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.
3 Le creuset éprouve l’argent et le fourneau l’or; celui qui éprouve les cœurs, c’est le Seigneur.
Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo, koma Yehova amayesa mitima.
4 Le méchant écoute la lèvre inique, le menteur prête l’oreille à la mauvaise langue.
Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa; munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.
5 Celui qui se moque du pauvre outrage celui qui l’a fait; celui qui se réjouit d’un malheur ne restera pas impuni.
Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake; amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.
6 Les enfants des enfants sont la couronne des vieillards, et les pères sont la gloire de leurs enfants.
Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba, ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.
7 Des paroles distinguées ne conviennent pas à l’insensé; mais bien moins à un noble les paroles mensongères!
Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru, nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?
8 Un présent est une pierre précieuse aux yeux de qui le possède; partout où il se tourne, il a du succès.
Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo; kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.
9 Celui qui couvre une faute cherche l’amitié, et celui qui la rappelle en ses paroles divise les amis.
Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi; wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.
10 Un blâme fait plus d’impression sur l’homme intelligent que cent coups sur l’insensé.
Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha, munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.
11 Le méchant ne cherche que rébellion, mais un messager cruel sera envoyé contre lui.
Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi; ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.
12 Mieux vaut rencontrer une ourse privée de ses petits qu’un insensé pendant sa folie.
Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.
13 Celui qui rend le mal pour le bien ne verra jamais le malheur quitter sa maison.
Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino, ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.
14 C’est ouvrir une digue que de commencer une querelle; avant que la dispute s’allume, retire-toi.
Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi, choncho uzichokapo mkangano usanayambe.
15 Celui qui absout le coupable et celui qui condamne le juste sont tous deux en abomination à Yahweh.
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.
16 À quoi sert l’argent dans la main de l’insensé? À acheter la sagesse? Il n’a pas le sens pour le faire.
Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?
17 L’ami aime en tout temps; dans le malheur il devient un frère.
Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse, ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.
18 L’homme sans intelligence prend des engagements, il se fait caution pour son prochain.
Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.
19 Celui qui aime les querelles aime le péché; celui qui élève sa parole aime sa ruine.
Wokonda zolakwa amakonda mkangano, ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.
20 Qui a un cœur faux ne trouve pas le bonheur, et qui a une langue perverse tombe dans le malheur.
Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino; ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.
21 Celui qui donne naissance à un insensé en aura du chagrin; le père d’un fou ne sera pas joyeux.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake, abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.
22 Un cœur joyeux est un excellent remède; un esprit abattu dessèche les os.
Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino, koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.
23 Le méchant reçoit des présents cachés dans le pli du manteau, pour pervertir les sentiers de la justice.
Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri kuti apotoze chiweruzo cholungama.
24 L’homme intelligent a devant lui la sagesse, mais les yeux de l’insensé sont à l’extrémité de la terre.
Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru, koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.
25 Un fils insensé fait le chagrin de son père, et l’amertume de sa mère.
Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.
26 Il n’est pas bon de frapper le juste d’amende, ni de condamner les nobles à cause de leur droiture.
Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa, kapena kulanga anthu osalakwa.
27 Celui qui contient ses paroles possède la science, et celui qui est calme d’esprit est un homme d’intelligence.
Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu, ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.
28 L’insensé lui-même, quand il se tait, passe pour un sage, pour intelligent, quand il ferme ses lèvres.
Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete; ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.