< Juges 9 >
1 Abimélech, fils de Jérobaal, se rendit à Sichem vers les frères de sa mère, et il leur adressa ces paroles, ainsi qu’à toute la famille de la maison du père de sa mère:
Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
2 « Dites, je vous prie, aux oreilles de tous les habitants de Sichem: Lequel vaut mieux pour vous que soixante-dix hommes, tous fils de Jérobaal, dominent sur vous, ou qu’un seul homme domine sur vous? Souvenez-vous que je suis vos os et votre chair. »
“Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
3 Les frères de sa mère ayant répété à son sujet toutes ces paroles aux oreilles de tous les habitants de Sichem, le cœur de ces derniers s’inclina vers Abimélech, car ils se disaient: « C’est notre frère. »
Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
4 Ils lui donnèrent soixante-dix sicles d’argent, tirés de la maison de Baal-Berith, et Abimélech s’en servit pour soudoyer des gens de rien et des aventuriers, qui s’attachèrent à lui.
Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
5 Il vint dans la maison de son père à Ephra, et il tua ses frères, fils de Jérobaal, au nombre de soixante-dix, sur une même pierre; il n’échappa que Joatham, le plus jeune fils de Jerobaal, parce qu’il s’était caché.
Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
6 Alors tous les habitants de Sichem et toute la maison de Mello s’assemblèrent; ils vinrent et proclamèrent roi Abimélech, prés du térébinthe du monument qui se trouve à Sichem.
Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
7 Lorsque Joatham en eut été informé, il alla se placer sur le sommet du mont Garizim et, élevant la voix, il leur cria en disant: « Écoutez-moi, habitants de Sichem, afin que Dieu vous écoute!
Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
8 Les arbres se mirent en chemin pour oindre un roi qui les commandât. Ils dirent à l’olivier: Règne sur nous.
Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
9 Mais l’olivier leur dit: Renoncerais-je à mon huile, qui fait ma gloire devant Dieu et devant les hommes, pour aller me balancer au-dessus des autres arbres?
“Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
10 Et les arbres dirent au figuier: Viens, toi, règne sur nous.
Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
11 Mais le figuier leur dit: Renoncerais-je à ma douceur et à mon excellent fruit, pour aller me balancer au-dessus des autres arbres?
Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
12 Et les arbres dirent à la vigne: Viens, toi, règne sur nous.
Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
13 Mais la vigne leur dit: Renoncerais-je à mon vin, qui réjouit Dieu et les hommes, pour aller me balancer au-dessus des autres arbres?
Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
14 Alors tous les arbres dirent au buisson d’épines: Viens, toi, règne sur nous.
Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
15 Et le buisson d’épines dit aux arbres: Si vraiment vous voulez m’oindre pour votre roi, venez, confiez-vous à mon ombrage; sinon, qu’un feu sorte du buisson d’épines et dévore les cèdes du Liban!…
Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
16 Maintenant, si c’est avec équité et droiture que vous avez agi en faisant roi Abimélech, si vous vous êtes bien conduits envers Jérobaal et sa maison, et si vous l’avez traité selon le mérite de ses mains,
Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
17 — car mon père a combattu pour vous, il a exposé sa vie et vous a délivrés de la main de Madian;
Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
18 et vous, vous vous êtes levés aujourd’hui contre la maison de mon père, vous avez tué ses fils, au nombre de soixante-dix, sur une même pierre, et vous avez établi roi sur les hommes de Sichem Abimélech, fils de sa servante, parce qu’il est votre frère, —
Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
19 si c’est avec équité et droiture que vous avez agi en ce jour envers Jérobaal et sa maison, eh bien, qu’Abimélech fasse votre joie, et que vous fassiez la sienne aussi!
Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
20 Sinon, qu’un feu sorte d’Abimélech et dévore les habitants de Sichem et la maison de Mello, et qu’un feu sorte des habitants de Sichem et de la maison de Mello et dévore Abimélech! »
Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
21 Joatham se retira et prit la fuite; il se rendit à Béra et il y demeura, par crainte d’Abimélech, son frère.
Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
22 Abimélech domina trois ans sur Israël.
Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
23 Et Dieu envoya un esprit mauvais entre Abimélech et les habitants de Sichem, et les habitants de Sichem devinrent infidèles à Abimélech:
Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
24 afin que le crime commis sur les soixante-dix fils de Jérobaal fût vengé et que leur sang retombe sur Abimélech, leur frère, qui les avait tués, et sur les hommes de Sichem qui l’avaient aidé à tuer ses frères.
Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
25 Les hommes de Sichem placèrent en embuscade contre lui, sur les sommets des montagnes, des gens qui dépouillaient tous ceux qui passaient près d’eux sur le chemin; et cela fut rapporté à Abimélech.
Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
26 Gaal, fils d’Obed, vint avec ses frères, et ils passèrent à Sichem. Les hommes de Sichem prirent confiance en lui.
Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
27 Ils sortirent dans la campagne, vendangèrent leurs vignes, foulèrent les raisins et firent une fête; puis, étant entrés dans la maison de leur dieu, ils mangèrent et burent, et ils maudirent Abimélech.
Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
28 Et Gaal, fils d’Obed, dit: « Qui est Abimélech, et qui est Sichem, pour que nous le servions? N’est-il pas fils de Jérobaal, et Zébul n’est-il pas son officier? Servez les hommes d’Emor, père de Sichem; mais nous, pourquoi servirions-nous Abimélech?
Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
29 Ah! que ne suis-je le chef de ce peuple! Je chasserais Abimélech. » Et il dit à Abimélech: « Renforce ton armée et sors! »
Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
30 Zébul, gouverneur de la ville, apprit les propos de Gaal, fils d’Obed, et sa colère s’enflamma.
Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
31 Il envoya secrètement des messagers à Abimélech, pour lui dire: « Voici que Gaal, fils d’Obed, est venu à Sichem avec ses frères, et voici qu’ils soulèvent la ville contre toi.
Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
32 Lève-toi de nuit, toi et le peuple qui est avec toi, et mets-toi en embuscade dans la campagne.
Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
33 Le matin, au lever du soleil, lève-toi et fonds sur la ville; et lorsque Gaal et le peuple qui est avec lui sortiront contre toi, tu lui feras selon ce que l’occasion te permettra. »
Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
34 Abimélech et tout le peuple qui était avec lui se levèrent de nuit, et ils se mirent en embuscade près de Sichem, divisés en quatre corps.
Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
35 Gaal, fils d’Obed, sortit, et il se plaça à l’entrée de la porte de la ville. Aussitôt Abimélech et tout le peuple qui était avec lui se levèrent de l’embuscade.
Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
36 En voyant le peuple, Gaal dit à Zébul: « Voici des gens qui descendent du sommet des montagnes. » Zébul lui répondit: « C’est l’ombre des montagnes que tu prends pour des hommes. »
Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
37 Gaal reprit la parole et dit: « Voici une troupe qui descend du milieu du pays, et un corps qui arrive par le chemin du chêne des devins. »
Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
38 Zébul lui répondit: « Où donc est ta bouche avec laquelle tu disais: Qui est Abimélech, pour que nous le servions? N’est-ce point là le peuple que tu méprisais? Sors maintenant et livre-lui bataille! »
Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
39 Gaal fit une sortie, à la tête des hommes de Sichem, et livra bataille à Abimélech.
Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
40 Abimélech le poursuivit, et Gaal s’enfuit devant lui, et beaucoup de ses hommes tombèrent morts jusqu’à l’entrée de la porte.
Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
41 Abimélech s’arrêta à Ruma; et Zébul chassa Gaal et ses frères, qui ne purent plus rester à Sichem.
Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
42 Le lendemain, le peuple sortit dans la campagne. Abimélech en ayant été informé,
Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
43 prit sa troupe, la partagea en trois corps, et se mit en embuscade dans la campagne. Dès qu’il aperçut le peuple sortant de la ville, il se leva contre eux et les battit.
Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
44 Abimélech et les corps qui étaient avec lui se jetèrent en avant et se placèrent à l’entrée de la porte de la ville; deux de ces corps se jetèrent sur tous ceux qui étaient dans la campagne et les battirent.
Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
45 Et Abimélech donna l’assaut à la ville pendant toute la journée; il s’en empara et tua le peuple qui s’y trouvait; puis il rasa la ville et y sema du sel.
Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
46 À cette nouvelle, tous les hommes de la tour de Sichem se rendirent dans la forteresse de la maison du dieu Berith.
Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
47 Dès qu’on eut annoncé à Abimélech que tous les habitants de la tour de Sichem s’y étaient rassemblés,
Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
48 Abimélech monta sur le mont Selmon, lui et tout le peuple qui était avec lui. Abimélech prit en main une hache, coupa une branche d’arbre, la souleva et la mit sur son épaule. Il dit au peuple qui était avec lui: « Ce que vous m’avez vu faire, hâtez-vous de le faire comme moi. »
Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
49 Et tous les gens aussi coupèrent chacun une branche et suivirent Abimélech; ils placèrent les branches contre la forteresse, et ils la livrèrent au feu avec ceux qu’elle renfermait. Et tous les gens de la tour de Sichem périrent aussi, mille environ, hommes et femmes.
Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
50 De là, Abimélech marcha contre Thébés; il assiégea Thébés et s’en empara.
Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
51 Il y avait au milieu de la ville une forte tour où se réfugièrent tous les habitants de la ville, hommes et femmes; ayant fermé la porte sur eux, ils montèrent sur le toit de la tour.
Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
52 Abimélech vint jusqu’à la tour; il l’attaqua et s’approcha de la porte de la tour pour y mettre le feu.
Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
53 Alors une femme lança sur la tête d’Abimélech un morceau de meule de moulin et lui brisa le crâne.
Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
54 Il appela aussitôt le jeune homme qui portait ses armes, et lui dit: « Tire ton épée et donne-moi la mort, afin qu’on ne dise pas de moi: C’est une femme qui l’a tué. » Le jeune homme le transperça, et il mourut.
Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
55 Quand les hommes d’Israël virent qu’Abimélech était mort, ils s’en allèrent chacun dans sa maison.
Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
56 Ainsi Dieu fit retomber sur Abimélech le mal qu’il avait fait à son père, en tuant ses soixante-dix frères;
Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
57 et Dieu fit retomber sur la tête des gens de Sichem toute leur méchanceté. Ainsi s’accomplit sur eux la malédiction de Joatham, fils de Jérobaal.
Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.