< Job 37 >

1 À ce spectacle, mon cœur est tout tremblant, il bondit hors de sa place.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Écoutez, écoutez le fracas de sa voix, le grondement qui sort de sa bouche!
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 Il lui donne libre carrière sous l’immensité des cieux, et son éclair brille jusqu’aux extrémités de la terre.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 Puis éclate un rugissement, il tonne de sa voix majestueuse; il ne retient plus les éclairs, quand on entend sa voix;
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 Dieu tonne de sa voix, d’une manière merveilleuse. Il fait de grandes choses que nous ne comprenons pas.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 Il dit à la neige: « Tombe sur la terre; » il commande aux ondées et aux pluies torrentielles.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 Il met un sceau sur la main de tous les hommes, afin que tout mortel reconnaisse son Créateur.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Alors l’animal sauvage rentre dans son repaire, et demeure dans sa tanière.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 L’ouragan sort de ses retraites cachées, l’aquilon amène les frimas.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Au souffle de Dieu se forme la glace, et la masse des eaux est emprisonnée.
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Il charge de vapeurs les nuages, il disperse ses nuées lumineuses.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 On les voit, selon ses décrets, errer en tous sens, pour exécuter tout ce qu’il leur commande, sur la face de la terre habitée.
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 C’est tantôt pour le châtiment de sa terre, et tantôt en signe de faveur qu’il les envoie.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Job, sois attentif à ces choses; arrête-toi, et considère les merveilles de Dieu.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Sais-tu comment il les opère, et fait briller l’éclair dans la nue?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Comprends-tu le balancement des nuages, les merveilles de celui dont la science est parfaite,
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 toi dont les vêtements sont chauds, quand la terre se repose au souffle du midi?
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 Peux-tu, comme lui, étendre les nuées, et les rendre solides comme un miroir d’airain?
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 Fais-nous connaître ce que nous devons lui dire: nous ne saurions lui parler, ignorants que nous sommes.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Ah! qu’on ne lui rapporte pas mes discours! Un homme a-t-il jamais dit qu’il désirait sa perte?
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 On ne peut voir maintenant la lumière du soleil, qui luit derrière les nuages; qu’un vent passe, il les dissipe.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 L’or vient du septentrion; mais Dieu, que sa majesté est redoutable!
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Le Tout-Puissant, nous ne pouvons l’atteindre: il est grand en force, et en droit, et en justice, il ne répond à personne!
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Que les hommes donc le révèrent! Il ne regarde pas ceux qui se croient sages.
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< Job 37 >