< Job 23 >

1 Alors Job prit la parole et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Oui, aujourd’hui ma plainte est amère, et pourtant ma main retient mes soupirs.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Oh! Qui me donnera de savoir où le trouver, d’arriver jusqu’à son trône!
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 Je plaiderais ma cause devant lui, et je remplirais ma bouche d’arguments.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 Je saurais les raisons qu’il peut m’opposer, je verrais ce qu’il peut avoir à me dire.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 M’opposerait-il la grandeur de sa puissance? Ne jetterait-il pas au moins les yeux sur moi?
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 Alors l’innocent discuterait avec lui, et je m’en irais absous pour toujours par mon juge.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 Mais si je vais à l’orient, il n’y est pas; à l’occident, je ne l’aperçois pas.
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 Est-il occupé au septentrion, je ne le vois pas; se cache-t-il au midi, je ne puis le découvrir.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 Cependant il connaît les sentiers où je marche; qu’il m’examine, je sortirai pur comme l’or.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 Mon pied a toujours foulé ses traces; je me suis tenu dans sa voie sans dévier.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Je ne me suis pas écarté des préceptes de ses lèvres; j’ai fait plier ma volonté aux paroles de sa bouche.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Mais il a une pensée: qui l’en fera revenir? Ce qu’il désire, il l’exécute.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 Il accomplira donc ce qu’il a décrété à mon sujet, et de pareils desseins, il en a beaucoup.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Voilà pourquoi je me trouble en sa présence; quand j’y pense, j’ai peur de lui.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 Dieu fait fondre mon cœur; le Tout-Puissant me remplit d’effroi.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Car ce ne sont pas les ténèbres qui me consument, ni l’obscurité dont ma face est voilée.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Job 23 >