< Jérémie 7 >

1 La parole qui fut adressée à Jérémie de la part de Yahweh, en ces termes:
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 " Tiens-toi à la porte de la maison de Yahweh, et là prononce cette parole et dis: Ecoutez la parole de Yahweh, vous tous, hommes de Juda, qui entrez par ces portes pour adorer Yahweh.
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 Ainsi parle Yahweh des armées, le Dieu d'Israël: Améliorez vos voies et vos œuvres, et je vous ferai habiter dans ce lieu.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 Ne vous fiez pas aux paroles de mensonge de ceux qui disent: " C'est ici le temple de Yahweh, le temple de Yahweh, le temple de Yahweh! "
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 Mais si vous améliorez vos voies et vos œuvres, si vous rendez fidèlement la justice entre un homme et son prochain;
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 Si vous n'opprimez pas l'étranger, l'orphelin et la veuve, si vous ne répandez pas en ce lieu le sang innocent, et si vous n'allez pas près d'autres dieux, pour votre malheur:
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 Alors je vous ferai habiter dans ce lieu, au pays que j'ai donné à vos pères, depuis les temps anciens et pour jamais.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 Mais voici que vous vous fiez à des paroles de mensonge, qui ne vous servent de rien!
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 Quoi! voler, tuer, commettre l'adultère, jurer faussement, encenser Baal et aller après d'autres dieux que, vous ne connaissez pas!...
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 Et vous venez, vous vous présentez devant moi, dans cette maison sur laquelle mon nom est invoqué, et vous dites: " Nous échapperons! " Et c'est afin de commettre toutes ces abominations!
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Est-ce donc à vos yeux une caverne de brigands, que cette maison sur laquelle mon nom est invoqué? Moi aussi, je l'ai vu, — oracle de Yahweh.
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 Allez donc à ma demeure qui était à Silo, où j'avais fait autrefois habiter mon nom, et voyez comment je l'ai traitée, à cause de la méchanceté de mon peuple d'Israël.
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 Et maintenant, puisque vous avez fait toutes ces actions, — oracle de Yahweh, et que je vous ai parlé, vous parlant dès le matin, et vous n'avez pas écouté, et que je vous ai appelés, et vous n'avez pas répondu,
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 je ferai de cette maison, sur laquelle mon nom a été invoqué, dans laquelle vous mettez votre confiance, et de ce lieu que j'ai donné à vous et à vos pères, ce que j'ai fait de Silo;
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 et je vous rejetterai de devant moi, comme j'ai rejeté tous vos frères, toute la race d'Ephraïm.
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 Et toi, n'intercède pas en faveur de ce peuple; n'élève pour lui ni plainte ni prière, et n'insiste pas auprès de moi, car je ne t'écouterai pas.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Ne vois-tu pas, ce qu'ils font dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 Les fils ramassent du bois, les pères allument le feu, les femmes pétrissent de la pâte pour faire des gâteaux à la reine du ciel, et répandre des libations à d'autres dieux, afin de m'offenser.
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 Est-ce moi qu'ils offensent, — oracle de Yahweh, n'est-ce pas eux-mêmes, à la honte de leur visage?
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 C'est pourquoi ainsi parle le Seigneur Yahweh: Voici que ma colère et ma fureur vont se répandre sur ce lieu, sur les hommes et sur les bêtes, sur l'arbre des champs et sur le fruit du sol; elle brûlera et ne s'éteindra point.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 Ainsi parle Yahweh des armées, Dieu d'Israël: Ajoutez vos holocaustes à vos sacrifices, et mangez-en la chair;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 car je n'ai pas parlé à vos pères ni ne leur ai rien prescrit, le jour où je les ai fait sortir du pays d'Egypte, en matière d'holocaustes et de sacrifices.
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 Mais quant au commandement que je leur ai donné, je leur ai dit: Ecoutez ma voix, et je serai votre Dieu, et vous serez mon peuple; marchez dans toutes les voies que je vous prescrirai, afin que vous soyez heureux.
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 Mais ils n'ont point écouté, et ils n'ont point prêté l'oreille et ils ont marché selon leurs conseils, selon l'endurcissement de leur mauvais cœur; ils sont allés en arrière, et non en avant.
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 Depuis le jour où vos pères sont sortis de la terre d'Egypte jusqu'à ce jour, je vous ai envoyé tous mes serviteurs les prophètes, les envoyant chaque jour dès le matin;
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 mais ils ne m'ont pas écouté, ils n'ont pas prêté l'oreille; ils ont raidi leur cou, ils ont fait pis que leurs pères.
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 Tu leur diras toutes ces choses, ils ne t'écouteront pas; tu les appelleras, ils ne te répondront pas.
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 Alors tu leur diras: C'est la nation qui n'a pas écouté la voix de Yahweh, son Dieu, et qui n'a pas accepté l'instruction; la fidélité a péri; elle a disparu de sa bouche.
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 Rase ta chevelure, et jette-la; et entonne sur les hauteurs un chant de deuil, car Yahweh a pris en dédain et rejeté la race objet de sa colère.
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 Car les fils de Juda ont fait ce qui est mal à mes yeux, — oracle de Yahweh; ils ont placé leurs abominations dans la maison sur laquelle mon nom a été invoqué, afin de la souiller;
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 et ils ont construit les hauts lieux de Topheth dans la vallée du fils de Hinnom, pour brûler au feu leurs fils et leurs filles, ce que je n'avais point commandé, et ce qui ne m'était pas venu à la pensée.
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 C'est pourquoi voici que des jours viennent, — oracle de Yahweh, où l'on ne dira plus " Topheth, " ni " Vallée du fils de Hinnom ", mais " Vallée du massacre ", et où l'on enterrera à Topheth, faute de place.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 Et les cadavres de ce peuple seront la pâture des oiseaux du ciel et des bêtes de la terre, sans qu'il y ait personne pour les chasser.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 Et je ferai cesser, dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem, les cris de réjouissance et les cris d'allégresse, le chant de l'époux et le chant de l'épouse, car le pays sera devenu un désert.
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< Jérémie 7 >