< Ézéchiel 45 >

1 « Quand vous partagerez au sort le pays pour le posséder, vous prélèverez comme offrande à Yahweh une portion sainte du pays; sa longueur sera de vingt-cinq mille coudées, et sa largeur de dix mille; elle sera sainte dans toute son étendue, tout autour.
“‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
2 Il y en aura pour le sanctuaire, cinq cents sur cinq cents, en carré, tout autour, et cinquante coudées pour sa banlieue, tout autour.
Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
3 Sur cet espace mesuré, tu mesureras une longueur de vingt-cinq mille et une largeur de dix mille; c’est là que sera le sanctuaire, le Saint des saints.
Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
4 Ce sera une portion sainte du pays; elle sera pour les prêtres qui font le service du sanctuaire, qui s’approchent pour servir Yahweh; ce sera pour eux une place pour leurs maisons, et un lieu saint pour le sanctuaire.
Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
5 Vingt-cinq mille coudées en longueur et dix mille en largeur seront pour les lévites, qui font le service de la maison; ils y posséderont des villes pour y habiter.
Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
6 Comme possession de la ville, vous mettrez cinq mille coudées de largeur et une longueur de vingt-cinq mille, parallèlement à la portion sainte prélevée; cela appartiendra à la maison d’Israël.
“‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
7 Pour le prince, vous réserverez un espace des deux côtés de la portion sainte prélevée et de la possession de la ville, le long de la portion sainte et le long de la possession de la ville, du côté de l’occident vers l’occident, et du côté de l’orient vers l’orient, sur une longueur correspondante à l’une des parts, de la frontière occidentale à la frontière orientale.
“‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
8 Ce sera son domaine, sa possession en Israël; et mes princes n’opprimeront plus mon peuple, et ils laisseront le pays à la maison d’Israël, selon ses tribus.
Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
9 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: C’en est assez, princes d’Israël! Écartez la violence et la rapine! Faites droit et justice; ôtez vos exactions de dessus mon peuple, — oracle du Seigneur Yahweh.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
10 Ayez des balances justes, un épha juste et un bath juste.
Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
11 L’épha et le bath auront une même contenance, de sorte que l’épha contienne la dixième partie du homer, et le bath le dixième du homer; leur contenance sera d’après le homer.
Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
12 Le sicle vaudra vingt guéras. La mine aura chez vous vingt sicles, vingt-cinq sicles, quinze sicles.
Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
13 Voici l’offrande que vous prélèverez: le sixième d’un épha sur le homer de froment, et le sixième d’un épha sur le homer d’orge.
“‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
14 Règle pour l’huile, pour le bath d’huile: la dixième partie d’un bath sur un cor, lequel est égal à un homer de dix baths, car un homer fait dix baths.
Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
15 Une brebis du troupeau sera donnée sur deux cents des gras pâturages d’Israël, pour l’oblation, l’holocauste et les sacrifices pacifiques, afin de faire propitiation pour eux, — oracle du Seigneur Yahweh.
Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Tout le peuple du pays devra prélever cette offrande pour le prince d’Israël.
Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
17 Mais le prince sera chargé des holocaustes, des oblations et des libations, aux fêtes, aux nouvelles lunes et aux sabbats, dans toutes les solennités de la maison d’Israël; c’est lui qui pourvoira aux sacrifices pour le péché, à l’oblation, à l’holocauste et aux sacrifices d’actions de grâces, afin de faire propitiation pour la maison d’Israël. »
Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
18 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: « Le premier mois, le premier du mois, tu prendras un jeune taureau sans défaut, et tu feras l’expiation du sanctuaire.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
19 Le prêtre prendra du sang de la victime pour le péché et en mettra sur le poteau de la maison, sur les quatre coins du cadre de l’autel et sur le poteau du portique du parvis intérieur.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
20 Tu feras de même le sept du mois pour celui qui pèche par erreur ou par simplicité, et vous ferez propitiation pour la maison.
Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
21 Le premier mois, le quatorzième jour du mois, vous aurez la Pâque, fête d’une semaine de jours. On mangera des pains sans levain.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
22 Le prince offrira ce jour-là, pour lui et pour tout le peuple du pays, un taureau en sacrifice pour le péché.
Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
23 Et pendant les sept jours de la fête, il offrira un holocauste à Yahweh, sept taureaux et sept béliers sans défaut, chacun des sept jours, et un bouc en sacrifice pour le péché chaque jour.
Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
24 Il fera aussi l’oblation, un épha de farine par taureau et un épha par bélier, avec un hin d’huile par épha.
Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
25 Le septième mois, le quinzième jour du mois, pendant la fête, il offrira pendant sept jours les mêmes sacrifices pour le péché, les mêmes holocaustes, les mêmes oblations et la même quantité d’huile. »
“‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”

< Ézéchiel 45 >