< Exode 38 >
1 Il fit l’autel des holocaustes en bois d’acacia; sa longueur était de cinq coudées, et sa largeur de cinq coudées; il était carré, et sa hauteur était de trois coudées.
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
2 À ses quatre coins, il fit des cornes qui sortaient de l’autel, et il le revêtit d’airain.
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
3 Il fit tous les ustensiles de l’autel, les vases à cendre, les pelles, les bassins, les fourchettes et les brasiers; il fit d’airain tous ces ustensiles.
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Il fit à l’autel une grille d’airain en forme de treillis; il la plaça sous la corniche de l’autel, par en bas, jusqu’à moitié de la hauteur.
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
5 Il fondit quatre anneaux, qu’il mit aux quatre coins de la grille d’airain, pour recevoir les barres.
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
6 Il fit les barres de bois d’acacia et les revêtit d’airain.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
7 Il passa les barres dans les anneaux, aux côtés de l’autel, pour qu’elles servent à le transporter. Il le fit creux, en planches.
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
8 Il fit la cuve d’airain et sa base d’airain, avec les miroirs des femmes qui s’assemblaient à l’entrée de la tente de réunion.
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
9 Il fit le parvis. Du côté du midi, à droite, les rideaux du parvis, en lin retors, avaient une longueur de cent coudées,
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 avec vingt colonnes et leurs vingt socles d’airain; les crochets des colonnes et leurs tringles étaient d’argent.
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Du côté du nord, les rideaux avaient cent coudées avec vingt colonnes et leurs vingt socles d’airain; les crochets des colonnes et leurs tringles étaient d’argent.
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Du côté de l’occident, les rideaux avaient cinquante coudées, avec dix colonnes et leurs dix socles.
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
13 Du côté de l’orient, sur le devant, il y avait cinquante coudées:
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
14 et il y avait quinze coudées de rideaux pour un côté de la porte, avec trois colonnes et leurs trois socles,
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
15 et pour le deuxième côté — d’un côté de la porte du parvis comme de l’autre, — quinze coudées de rideaux avec trois colonnes et leurs trois socles.
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Tous les rideaux formant l’enceinte du parvis étaient de lin retors.
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
17 Les socles pour les colonnes étaient d’airain, les crochets des colonnes et leurs tringles étaient d’argent, et leurs chapiteaux étaient revêtus d’argent. Toutes les colonnes du parvis étaient reliées par des tringles d’argent.
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
18 Le rideau de la porte du parvis était un ouvrage de dessin varié, en pourpre violette, pourpre écarlate, cramoisi, et lin retors; sa longueur était de vingt coudées, et sa hauteur de cinq coudées, comme la largeur des rideaux du parvis;
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
19 ses quatre colonnes et leurs quatre socles étaient d’airain, les crochets et leurs tringles d’argent, et leurs chapiteaux revêtus d’argent.
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
20 Tous les pieux pour la Demeure et pour l’enceinte du parvis étaient d’airain.
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
21 Voici le compte des choses qui ont été employées pour la Demeure, la Demeure du témoignage, compte dressé par le soin des Lévites sur l’ordre de Moïse et sous la direction d’Ithamar, fils du grand prêtre Aaron.
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
22 Béseléel, fils d’Uri, fils de Hur, de la tribu de Juda, fit tout ce que Yahweh avait ordonné à Moïse;
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
23 il eut pour aide Ooliab, fils Achisamech, de la tribu de Dan, habile à sculpter, à inventer, à tisser en dessin varié la pourpre violette, la pourpre écarlate, le cramoisi, et le fin lin.
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
24 Total de l’or employé à l’ouvrage, pour tout l’ouvrage du sanctuaire, or qui était le produit des offrandes: vingt-neuf talents et sept cent trente sicles, selon le sicle du sanctuaire.
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
25 L’argent de ceux de l’assemblée qui furent recensés s’élevait à cent talents et mille sept cent soixante-quinze sicles, selon le sicle du sanctuaire.
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
26 C’était un béka par tête, la moitié d’un sicle, selon le sicle du sanctuaire, pour chaque homme compris dans le recensement, depuis l’âge de vingt ans et au-dessus, soit pour six cent trois mille cinq cent cinquante hommes.
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
27 Les cent talents d’argent servirent à fondre les socles du sanctuaire et les socles du voile, cent socles pour les cent talents, un talent par socle.
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
28 Et avec les mille sept cent soixante-quinze sicles, on fit les crochets pour les colonnes, on revêtit les chapiteaux et on les joignit par des tringles.
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
29 L’airain des offrandes montait à soixante-dix talents et deux mille quatre cent sicles.
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
30 On en fit les socles de l’entrée de la tente de réunion, l’autel d’airain avec sa grille d’airain et tous les ustensiles de l’autel,
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31 les socles de l’enceinte du parvis et les socles de la porte du parvis, et tous les pieux de la Demeure et tous les pieux de l’enceinte du parvis.
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.