< 2 Chroniques 7 >
1 Lorsque Salomon eut achevé de prier, le feu descendit du ciel et consuma l’holocauste et les victimes, et la gloire de Yahweh remplit la maison.
Solomoni atamaliza kupemphera, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kutentha nsembe zopsereza ndi nsembe zina, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulunguyo.
2 Les prêtres ne pouvaient entrer dans la maison de Yahweh, car la gloire de Yahweh remplissait sa maison.
Ansembe sanathe kulowa mʼNyumba ya Mulungu chifukwa munadzaza ulemerero wa Yehova.
3 Tous les enfants d’Israël virent descendre le feu et la gloire de Yahweh sur la maison et, tombant le visage contre terre sur le pavé, ils se prosternèrent et louèrent Yahweh, en disant: « Car il est bon, car sa miséricorde dure à jamais! »
Aisraeli onse ataona moto ukuchokera kumwamba ndi ulemerero wa Yehova pamwamba pa Nyumba ya Mulungu, anagwada poyalidwa miyalapo ndipo anagunditsa nkhope zawo pansi, ndi kulambira ndi kutamanda Yehova, ponena kuti, “Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala chikhalire”
4 Le roi et tout le peuple offrirent des sacrifices devant Yahweh.
Tsono mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.
5 Le roi Salomon immola, pour le sacrifice, vingt deux mille bœufs et cent vingt mille brebis. C’est ainsi que le roi et tout le peuple firent la dédicace de la maison de Dieu.
Ndipo mfumu Solomoni anapereka nsembe ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Kotero mfumu ndi anthu onse anachita mwambo wopereka Nyumba kwa Mulungu.
6 Les prêtres se tenaient à leurs postes, et les lévites aussi avec les instruments de musique de Yahweh que le roi David avait faits pour louer Yahweh, « car sa miséricorde dure à jamais! « lorsqu’il célébra Yahweh par leur ministère. Les prêtres sonnaient des trompettes vis-à-vis d’eux, et tout Israël était debout.
Ansembe anayimirira mʼmalo mwawo, monganso anachitira Alevi ndi zida zoyimbira za Yehova, zimene Davide anapanga zotamandira Yehova ndipo zimagwiritsidwa ntchito pamene amatamanda, ponena kuti, “Chikondi chake chikhale chikhalire.” Moyangʼanizana ndi Alevi, ansembe amaliza malipenga, ndipo Aisraeli onse anali atayimirira.
7 Salomon consacra le milieu du parvis qui est devant la maison de Yahweh; car il offrit là les holocaustes et les graisses des sacrifices pacifiques, parce que l’autel d’airain qu’il avait fait ne pouvait contenir l’holocauste, l’oblation et les graisses.
Solomoni anapatula malo a pakati pa bwalo kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndipo pamenepo anapereka nsembe zopsereza ndi mafuta, zopereka za chiyanjano, chifukwa guwa lansembe lamkuwa limene anapanga panalibe malo woti nʼkuperekerapo nsembe zopsereza, nsembe za ufa ndi mafuta.
8 Salomon célébra la fête en ce temps-là pendant sept jours, et tout Israël avec lui, très grande multitude venue depuis l’entrée d’Émath jusqu’au torrent d’Égypte.
Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero kwa masiku asanu ndi awiri pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku chigwa cha ku Igupto.
9 Le huitième jour, ils tinrent l’assemblée de clôture; car ils avaient fait la dédicace de l’autel pendant sept jours, et la fête pendant sept jours.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panali msonkhano, pakuti anachita mwambo wopereka guwa lansembe kwa masiku asanu ndi awiri ndi masiku enanso asanu ndi awiri achikondwerero.
10 Et le vingt troisième jour du septième mois, Salomon renvoya dans ses tentes le peuple joyeux et le cœur content pour le bien que Yahweh avait fait à David, à Salomon et à Israël, son peuple.
Pa tsiku la 23 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Solomoni anawuza anthu aja kuti apite kwawo. Anthu anali achimwemwe ndi okondwa mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira Davide ndi Solomoni ndiponso anthu ake Aisraeli.
11 Salomon acheva la maison de Yahweh et la maison du roi, et il mena à bien tout ce qui lui était venu à l’esprit de faire dans la maison de Yahweh et dans la maison du roi.
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene zinali mu mtima mwake pa Nyumba ya Yehova ndi nyumba yake yaufumu,
12 Et Yahweh lui apparut pendant la nuit et lui dit: « J’ai exaucé ta prière et j’ai choisi ce lieu comme la maison où l’on m’offrira des sacrifices.
Yehova anamuonekera usiku ndipo anati: “Ine ndamva pemphero lako ndipo ndadzisankhira malo ano kukhala Nyumba yanga yoperekeramo nsembe.
13 Quand je fermerai le ciel et qu’il n’y aura pas de pluie, quand j’ordonnerai aux sauterelles de dévorer le pays, ou quand j’enverrai la peste dans mon peuple,
“Ine ndikatseka kumwamba kuti mvula isagwe, kapena kulamulira dzombe kuti liwononge dziko, kapena kutumiza mliri pakati pa anthu,
14 si mon peuple, sur lequel est invoqué mon nom, s’humilie, prie et cherche ma face, et s’il se détourne de ses mauvaises voies, je l’écouterai du ciel, je lui pardonnerai son péché et je guérirai son pays.
ngati anthu anga, amene amatchedwa ndi dzina langa adzichepetsa ndi kupemphera ndi kufunafuna nkhope yanga, nasiya njira zawo zoyipa, pamenepo Ine ndidzamva kumwamba ndipo ndidzakhululuka tchimo lawo ndi kuchiritsa dziko lawo.
15 Maintenant, mes yeux seront ouverts et mes oreilles attentives à la prière faite en ce lieu.
Ndipo maso anga adzatsekuka ndi makutu anga adzakhala tcheru kumva mapemphero a pamalo pano.
16 Maintenant je choisis et je sanctifie cette maison, pour que mon nom y réside à jamais, et là seront à jamais mes yeux et mon cœur.
Ine ndasankha ndipo ndapatula Nyumba yangayi kotero kuti ndidzakhala mʼmenemo kwamuyaya. Maso ndi mtima wanga zidzakhala pano nthawi zonse.
17 Et toi, si tu marches devant moi comme a marché David, ton père, mettant en pratique tout ce que je t’ai prescrit, et si tu observes mes lois et mes ordonnances,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula, ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
18 j’affermirai le trône de ta royauté, selon l’ alliance que j’ai conclue avec David, ton père, en disant: il ne te manquera jamais un descendant qui règne en Israël.
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu, monga ndinachitira pangano ndi abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu wolamulira Israeli.’
19 Mais si vous vous détournez, si vous abandonnez mes lois et mes commandements que j’ai mis devant vous, et si vous allez servir d’autres dieux et vous prosterner devant eux,
“Koma ngati iwe udzapatuka ndi kutaya malangizo ndi malamulo amene ndakupatsa ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
20 je les arracherai de mon pays que je leur ai donné; cette maison que j’ai consacrée à mon nom, je la rejetterai de devant ma face, et j’en ferai un sujet de sarcasme et de raillerie parmi tous les peuples.
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko langa limene ndinawapatsa, ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndadzipatulira. Ndipo udzakhala ngati mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
21 Cette maison qui était si haut placée sera un sujet de stupeur pour quiconque passera près d’elle, et il dira: Pourquoi Yahweh a-t-il ainsi traité ce pays et cette maison?
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
22 Et l’on répondra: Parce qu’ils ont abandonné Yahweh, le Dieu de leurs pères, qui les a fait sortir du pays d’Égypte, et que, s’attachant à d’autres dieux, ils se sont prosternés devant eux et les ont servis; voilà pourquoi il a fait venir sur eux tous ces maux. »
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova, Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa mʼdziko la Igupto ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”