< 1 Samuel 4 >

1 La parole de Samuel fut adressée à tout Israël. Israël sortit au devant des Philistins, pour combattre; ils campèrent près d’Eben-Ezer, et les Philistins étaient campés à Aphec.
Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse. Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki.
2 Les Philistins, s’étant rangés en bataille contre Israël, le combat s’engagea, et Israël fut battu par les Philistins, et ils tuèrent environ quatre mille hommes en bataille rangée dans la plaine.
Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo.
3 Le peuple rentra au camp, et les anciens d’Israël dirent: « Pourquoi Yahweh nous a-t-il battus aujourd’hui devant les Philistins? Faisons venir vers nous de Silo l’arche de l’Alliance de Yahweh; qu’elle vienne au milieu de nous, et qu’elle nous délivre de la main de nos ennemis. »
Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”
4 Le peuple envoya à Silo, et l’on apporta de cette ville l’arche de l’alliance de Yahweh des armées, qui est assis sur les Chérubins. Les deux fils d’Héli, Ophni et Phinées, étaient là avec l’arche de l’alliance de Dieu.
Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
5 Lorsque l’arche de l’alliance de Yahweh entra dans le camp, tout Israël poussa de si grands cris de joie que la terre en retentit.
Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka.
6 Le bruit de ces clameurs fut entendu des Philistins, et ils dirent: « Que signifie le bruit de ces grands cris de joie au camp des Hébreux? » Et ils apprirent que l’arche de Yahweh était venue au camp.
Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?” Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako,
7 Les Philistins eurent peur, parce qu’ils disaient: « Dieu est venu dans le camps. » Et ils dirent: « Malheur à nous! car chose pareille n’a jamais eu lieu jusqu’à présent.
Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe.
8 Malheur à nous! Qui nous délivrera de la main de ces dieux puissants? Ce sont ces dieux qui ont frappé les Égyptiens de toutes sortes de plaies dans le désert.
Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu.
9 Montrez-vous forts et agissez en hommes, Philistins, de peur que vous ne soyez asservis aux Hébreux, comme ils vous sont asservis. Soyez des hommes et combattez. »
Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’”
10 Les Philistins livrèrent bataille, et Israël fut battu, et chacun s’enfuit dans sa tente; il y eut une très grande défaite, et il tomba du côté d’Israël trente mille hommes de pied.
Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa.
11 L’arche de Dieu fut prise, et les deux fils d’Héli, Ophni et Phinées, périrent.
Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.
12 Un homme de Benjamin accourut du champ de bataille, et vint à Silo le même jour, les vêtements déchirés et la tête couverte de poussière.
Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni.
13 Lorsqu’il arriva, Héli était assis sur un siège près du chemin, dans l’attente, car son cœur tremblait à cause de l’arche de Dieu. Cet homme étant entré dans la ville pour porter ces nouvelles, toute la ville poussa une clameur.
Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.
14 En entendant le bruit de cette clameur, Héli dit: « Quel est ce bruit de tumulte? » Et aussitôt l’homme vint apporter la nouvelle à Héli.
Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?” Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera.
15 Or Héli était âgé de quatre-vingt-dix-huit ans; il avait les yeux fixes et ne pouvait plus voir.
Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona.
16 L’homme dit à Héli: « J’arrive du champ de bataille, et c’est du champ de bataille que je me suis enfui aujourd’hui. » Héli dit: « Que s’est-il passé mon fils? »
Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.” Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”
17 Le messager répondit: « Israël a fui devant les Philistins, et il y a eu un grand massacre parmi le peuple; et même tes deux fils, Ophni et Phinées, sont morts, et l’arche de Dieu a été prise. »
Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”
18 À peine eut-il nommé l’arche de Dieu, qu’Héli tomba de son siège à la renverse, à côté de la porte; il se rompit la nuque et mourut; car c’était un homme vieux et pesant. Il avait jugé Israël pendant quarante ans.
Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.
19 Sa belle-fille, femme de Phinées, était enceinte et sur le point d’accoucher. Lorsqu’elle entendit la nouvelle de la prise de l’arche de Dieu, de la mort de son beau-père et de son mari, elle se courba et enfanta, car les douleurs lui survinrent.
Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana.
20 Comme elle allait mourir, les femmes qui se trouvaient près d’elle lui dirent: « Ne crains point, car tu as enfanté un fils. » Mais elle ne répondit pas et n’y fit pas attention.
Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.
21 Elle appela l’enfant Ichabod, en disant: « La gloire est emportée d’Israël à cause de la prise de l’arche de Dieu et à cause de la mort de son beau-père et de son mari.
Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake.
22 Elle dit: « La gloire est emportée d’Israël, car l’arche de Dieu est prise! »
Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”

< 1 Samuel 4 >