< 1 Samuel 25 >

1 Cependant Samuel mourut et tout Israël s’assembla; on le pleura, et on l’enterra dans sa demeure, à Rama. Alors David se leva et descendit au désert de Pharan.
Samueli anamwalira, ndipo Aisraeli onse anasonkhana kudzalira maliro ake ndipo anamuyika mʼmanda ku mudzi kwawo ku Rama. Ndipo Davide anapita ku chipululu cha Parani.
2 Il y avait à Maon un homme ayant ses biens à Carmel; c’était un homme très riche, il avait trois mille brebis et mille chèvres, et il se trouvait à Carmel pour la tonte de ses brebis.
Kunali munthu wina wolemera kwambiri ku Maoni amene malo ake a ntchito anali ku Karimeli. Iyeyu anali ndi mbuzi 1,000 ndi nkhosa 3,000.
3 Le nom de cet homme était Nabal, et le nom de sa femme Abigaïl. La femme était pleine de sens, et de belle figure; mais l’homme était dur et méchant en actes; il était de la race de Caleb.
Dzina lake linali Nabala ndipo anali wa fuko la Kalebe. Dzina la mkazi wake linali Abigayeli. Anali mkazi wanzeru ndi wokongola, koma mwamuna wake, wa banja la Kalebe, anali wowuma mtima ndi wamwano pa zochita zake.
4 David apprit au désert que Nabal tondait ses brebis.
Davide anamva akanali ku chipululu kuti Nabala akumeta nkhosa.
5 David envoya dix jeunes gens, et David dit aux jeunes gens: « Montez à Carmel et allez trouver Nabal; vous le saluerez en mon nom,
Choncho anatuma anyamata khumi nawawuza kuti, “Pitani kwa Nabala ku Karimeli ndipo mukamulonjere mʼdzina langa.
6 et vous lui parlerez ainsi: Pour la vie! Que la paix soit avec toi, que la paix soit avec ta maison et que la paix soit avec tout ce qui t’appartient.
Mukamuwuze kuti, ‘Mtendere ukhale ndi inu, banja lanu pamodzi ndi zonse zimene muli nazo.
7 Et maintenant, j’ai appris que tu as les tondeurs. Or, tes bergers ont été avec nous; nous ne leur avons causé aucune peine, et rien du troupeau ne leur a été enlevé pendant tout le temps qu’ils ont été à Carmel.
“‘Tsono ndamva kuti muli ndi anthu ometa nkhosa. Pamene abusa anu anali nafe kuno, sitinawachite china chilichonse choyipa, ndipo sanasowe kanthu pa nthawi yonse imene anali ku Karimeli.
8 Interroge tes serviteurs, et ils te le diront. Que les jeunes gens trouvent donc grâce à tes yeux, puisque nous venons dans un jour de joie. Donne, je te prie, à tes serviteurs et à ton fils David ce que ta main pourra trouver. »
Muwafunse antchito anu ndipo akuwuzani. Kotero akomereni mtima anyamata anga, pakuti tabwera pa nthawi yachikondwerero. Chonde apatseniko antchito anuwo ndi mwana wanu Davide chilichonse chimene mungakhale nacho.’”
9 Lorsque les jeunes gens de David furent arrivés, ils répétèrent toutes ces paroles à Nabal au nom de David, et ils se reposèrent.
Anyamata a Davide aja atafika, anamuwuza Nabala zonse zimene Davide anayankhula. Ndipo anadikira yankho.
10 Nabal répondit aux serviteurs de David et dit: « Qui est David, et qui est le fils d’Isaï? Ils sont nombreux aujourd’hui les serviteurs qui s’échappent de chez leurs maîtres.
Nabala anayankha anyamata a Davide kuti, “Kodi Davide ndi ndani? Mwana wa Yese ndi ndani? Masiku ano pali antchito ambiri amene akuthawa kwa mabwana awo.
11 Et je prendrais mon pain et mon eau, et mon bétail que j’ai tué pour mes tondeurs, et je les donnerais à des gens qui viennent je ne sais d’où? »
Nditengerenji buledi, madzi ndi nyama zimene ndaphera anthu anga ometa nkhosa ndi kuzipereka kwa anthu amene sindikudziwa kumene achokera?”
12 Les jeunes gens de David, rebroussant chemin, s’en retournèrent et, lorsqu’ils furent arrivés, ils lui redirent toutes ces paroles.
Choncho anyamata a Davide aja anatembenuka nabwerera. Atafika anafotokozera Davide mawu onse a Nabala.
13 Alors David dit à ses hommes: « Que chacun de vous ceigne son épée! » Et ils ceignirent chacun leur épée, et David, lui aussi, ceignit son épée; environ quatre cents hommes montèrent à la suite de David; il en resta deux cents près des bagages.
Davide anawuza anthu ake kuti, “Aliyense amangirire lupanga lake!” Choncho aliyense anamangirira lupanga lake. Davidenso anamangirira lupanga lake. Anthu pafupifupi 400 ndiwo anapita ndi Davide, pamene anthu 200 anatsala ndi katundu.
14 Un des serviteurs de Nabal vint apporter la nouvelle à Abigaïl en disant: « Voici que David a envoyé du désert des messagers pour saluer notre maître, qui s’est jeté sur eux.
Tsono mmodzi mwa antchito anawuza Abigayeli mkazi wa Nabala kuti, “Davide anatumiza amithenga kuchokera ku chipululu kudzalonjera mbuye wathu, koma iye anawalalatira.
15 Et pourtant ces gens ont été bons pour nous; ils ne nous ont causé aucune peine, et rien ne nous a été enlevé tout le temps que nous avons cheminé avec eux, lorsque nous étions dans la campagne.
Komatu anthuwa anatichitira zabwino kwambiri. Sanatizunze, ndipo nthawi yonse imene tinali nawo ku busa sitinasowe kanthu.
16 Ils nous ont servi de rempart, aussi bien la nuit que le jour, tout le temps que nous avons été avec eux, paissant les troupeaux.
Ankatitchinjiriza ngati mpanda usiku ndi usana nthawi yonse tinkaweta nkhosa.
17 Reconnais maintenant et vois ce que tu as à faire; car le mal est résolu contre notre maître et contre toute sa maison; pour lui, c’est un fils de Bélial, et on ne peut lui parler. »
Tsono onani chimene mungachite, chifukwa zimenezi zingadzetse tsoka pa mbuye wathu pamodzi ndi nyumba yake. Paja mbuye athu aja ndi munthu wa khalidwe loyipa moti palibe amene angathe kuyankhula naye.”
18 Aussitôt Abigaïl prit deux cents pains, deux outres de vin, cinq moutons apprêtés, cinq mesures de grain rôti, cent masses de raisin sec et deux cents de figues sèches et, les ayant mis sur des ânes,
Ndipo Abigayeli sanataye nthawi. Iye anatenga malofu a buledi 200, matumba a chikopa awiri a vinyo, nkhosa zisanu zowotcheratu, makilogalamu 17 a tirigu wokazinga, makeke a mphesa zowuma 100, ndiponso makeke a nkhuyu 200, ndipo anazisenzetsa abulu.
19 elle dit à ses jeunes gens: « Passez devant moi, je vous suis. » Mais elle ne dit rien à Nabal, son mari.
Kenaka anawuza antchito ake kuti, “Tsogolani, ine ndikutsatirani.” Koma sanawuze mwamuna wake Nabala.
20 Comme elle descendait, montée sur un âne, en un endroit couvert de la montagne, voici que David et ses hommes descendaient en face d’elle, et elle les rencontra. —
Mayi uja atakwera pa bulu wake ndi kufika pa tsinde la phiri, anangoona Davide ndi ankhondo ake akubwera kunali iye. Choncho anakumana nawo.
21 David disait: « C’est bien en vain que j’ai surveillé tout ce que cet homme a dans le désert, et que rien n’a été enlevé de tout ce qu’il possède; il me rend le mal pour le bien!
Nthawiyi nʼkuti Davide atanena kuti, “Kani ndinalondera pachabe katundu wa munthu uyu mʼchipululu muja! Ndipotu palibe kanthu nʼkamodzi komwe kake kamene kanasowa. Tsono wandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino.
22 Que Dieu traite dans toute sa rigueur les ennemis de David! De tout ce qui appartient à Nabal, je ne laisserai rien subsister jusqu’au lever du jour, pas même celui qui urine contre le mur. »
Mulungu andilange kwambiri ngati pofika mmawa nditakhale nditasiyako ngakhale munthu mmodzi mwa onse amene ali nawo.”
23 Dès qu’Abigaïl aperçut David, elle s’empressa de descendre de l’âne et, tombant sur sa face devant David, elle se prosterna contre terre.
Abigayeli ataona Davide, anatsika pa bulu wake mofulumira ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pa Davide.
24 Puis elle se jeta à ses pieds, en disant: « Que sur moi, mon seigneur, sur moi soit la faute! Permets à ta servante de parler à tes oreilles, et écoute les paroles de ta servante!
Ali chigonere choncho pa mapazi a Davide anati, “Mbuye wanga, kulakwa kukhale pa ine ndekha. Chonde lolani kuti mdzakazi wanune ndiyankhule nanu, ndipo mumve mawu a ine mdzakazi wanu.
25 Que mon seigneur ne prenne pas garde à cet homme de Bélial, à Nabal, car il est ce que son nom indique; son nom est Le Fou, et il y a chez lui de la folie. Mais moi, ta servante, je n’ai pas vu les gens de mon seigneur, que tu as envoyés.
Mbuye wanga musasamale za mwamuna wanga Nabala, munthu wa khalidwe loyipa. Iyeyu ali monga dzina lake liliri. Monga dzina lake litanthauza kuti chitsiru, ndiye kuti zake zonse ndi zauchitsiru basi. Koma ine mdzakazi wanu, sindinawaone anthu amene mbuye wanga munawatuma.
26 Maintenant, mon seigneur, aussi vrai que Yahweh est vivant et que ton âme est vivante, Yahweh t’a préservé de répandre le sang et de te venger de ta main. Et maintenant, que tes ennemis et ceux qui veulent du mal à mon seigneur soient comme Nabal!
Tsono mbuye wanga muli apa, ndikulumbira pali Yehova wamoyo amene wakuletsani kuti musakhetse magazi a munthu ndi kulipsira nokha, kuti adani anu amene afuna kukuchitani zoyipa adzakhale ngati Nabala.
27 Accepte donc ce présent que ta servante apporte à mon seigneur, et qu’il soit distribué aux jeunes gens qui marchent à la suite de mon seigneur.
Choncho, nazi mphatso zimene mdzakazi wanu ndabwera nazo kwa mbuye wanga kuti zipatsidwe kwa anyamata amene muli nawo.
28 Pardonne, je te prie, la faute de ta servante, car Yahweh fera certainement à mon seigneur une maison stable; car mon seigneur soutient les guerres de Yahweh, et on ne trouvera pas de mal en toi tout le temps de ta vie.
Chonde khululukani zolakwa za ine mdzakazi wanu. Ndithu Yehova adzakhazikitsa banja la mbuye wanga mu ufumu, popeza mukumenya nkhondo ya Yehova. Choncho choyipa sichidzapezeka mwa inu masiku onse a moyo wanu.
29 S’il s’élève quelqu’un pour te poursuivre et en vouloir à ta vie, la vie de mon seigneur sera liée dans le faisceau des vivants auprès de Yahweh, ton Dieu, et la vie de tes ennemis, il la lancera au loin du creux de la fronde.
Ngati munthu wina akuwukirani ndi kukulondani, Yehova Mulungu wanu adzateteza moyo wa mbuye wanga monga mmene munthu asungira chuma mʼphukusi, koma moyo wa adani anu adzawutaya kutali monga momwe munthu amaponyera mwala ndi legeni.
30 Lorsque Yahweh aura fait à mon seigneur selon tout le bien qu’il a dit à ton sujet et qu’il t’aura établi chef sur Israël,
Yehova adzakuchitirani mbuye wanga zabwino zonse zimene anakulonjezani. Adzakuyikani kukhala wolamulira Aisraeli.
31 ce ne sera pas pour toi un sujet de remords ni pour mon seigneur une souffrance de cœur d’avoir répandu le sang sans motif et s’être vengé lui-même. Et lorsque Yahweh aura fait du bien à mon seigneur, souviens-toi de ta servante. »
Zikadzatero, inu mbuye wanga simudzakhala ndi chikumbumtima choti munakhetsa magazi kapena kulipsira popanda chifukwa. Koma Yehova akadzakuchitirani zabwino zonsezi musadzandiyiwale ine mdzakazi wanu.”
32 David dit à Abigaïl: « Béni soit Yahweh, le Dieu d’Israël, qui t’a envoyée, aujourd’hui à ma rencontre! Béni soit ton grand sens,
Tsono Davide anawuza Abigayeli kuti, “Alemekezeke Yehova Mulungu wa Israeli, amene wakutuma iwe lero kuti ukumane nane.
33 et bénie sois-tu, toi qui m’as empêché en ce jour de répandre le sang et de me venger de ma main!
Yehova akudalitseni chifukwa cha nzeru zanu pondiletsa lero kuti ndisakhetse magazi ndi kubwezera adani anga ndi manja anga.
34 Autrement, aussi vrai que Yahweh, le Dieu d’Israël, qui m’a empêché de te faire du mal, est vivant, si tu ne t’étais pas hâtée de venir au-devant de moi, il ne fût rien resté à Nabal d’ici au lever du jour, pas même celui qui urine contre le mur. »
Kunena zoona, pali Yehova Wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene wandiletsa kuti ndisakupwetekeni, mukanapanda kubwera msanga kudzakumana nane, palibe munthu aliyense wamwamuna wa Nabala akanasiyidwa wamoyo pakucha mmawa.”
35 David prit de la main d’ Abigaïl ce qu’elle lui avait apporté, et lui dit: « Monte en paix dans ta maison; vois, j’ai écouté ta voix et relevé ton visage! »
Ndipo Davide analandira kwa mayiyo zimene anamutengera ndipo anati, “Pitani kwanu mu mtendere. Ine ndamva mawu anu ndipo ndavomera zimene mwapempha.”
36 Abigaïl retourna vers Nabal, et voici qu’il faisait dans sa maison un festin comme un festin de roi; et le cœur de Nabal était joyeux, et il était complètement ivre. Elle ne lui apprit ni peu, ni beaucoup, jusqu’au lever du jour.
Abigayeli atabwerera kwa Nabala anamupeza ali mʼnyumba akuchita mphwando ngati la mfumu. Iye anali atakondwa kwambiri popeza anali ataledzera kwambiri. Choncho mkazi wakeyo sanamuwuze kalikonse mpaka mmawa kutacha.
37 Mais le matin, quand Nabal fut revenu de son ivresse, sa femme lui raconta ces choses, et son cœur en reçut un coup mortel, et il devint comme une pierre.
Tsono mmawa, mowa utamuchoka Nabala, mkazi wake anamuwuza zonse. Pomwepo mtima wake unaleka kugunda ndipo unawuma gwaa ngati mwala.
38 Environ dix jours après, Yahweh frappa Nabal, et il mourut.
Patapita masiku khumi, Yehova anakantha Nabala ndipo anafa.
39 Lorsque David apprit la mort de Nabal, il dit: « Béni soit Yahweh qui a défendu ma cause et m’a vengé de l’outrage que j’ai reçu de la main de Nabal, et qui a empêché son serviteur de faire le mal! Yahweh a fait retomber la méchanceté de Nabal sur sa tête. » Ensuite David envoya dire à Abigaïl qu’il voulait la prendre pour femme.
Pamene Davide anamva kuti Nabala wamwalira, iye anati, “Alemekezeke Yehova, walipsira Nabala chipongwe chimene anandichita ndipo anandiletsa ine mtumiki wake kuti ndisachite choyipa. Yehova wabwezera pamutu pa Nabala choyipa chimene iye anachita.” Kenaka Davide anatumiza mawu kwa Abigayeli, kumupempha kuti akhale mkazi wake.
40 Arrivés chez Abigaïl à Carmel, les serviteurs de David lui parlèrent ainsi: « David nous a envoyés vers toi, afin de te prendre pour sa femme. »
Anyamata a Davide atafika ku Karimeli anawuza Abigayeli kuti, “Davide watituma kwa iwe kuti tikutenge ukhale mkazi wake.”
41 Elle se leva et, s’étant prosternée le visage contre terre, elle dit: « Voici que ta servante est comme une esclave pour laver les pieds des serviteurs de mon seigneur! »
Abigayeli anagwada nagunditsa nkhope yake pansi ndipo anati, “Ine mdzakazi wa mbuye wanga ndakonzeka kutumikira ngakhale kusambitsa mapazi a anyamata ake.”
42 Aussitôt Abigaïl se leva et monta sur un âne, et cinq de ses jeunes filles allaient sur ses pas; elle suivit les messagers de David, et elle devint sa femme.
Motero Abigayeli ananyamuka mofulumira nakwera bulu wake. Tsono iye pamodzi ndi anamwali ake asanu amene ankamutumikira, anatsagana ndi amithenga a Davide aja ndipo anakakhala mkazi wake wa Davide.
43 David prit aussi Achinoam de Jezraël, et toutes les deux furent ses femmes.
Davide nʼkuti atakwatiranso Ahinoamu wa ku Yezireeli ndipo onse awiri anali akazi ake.
44 Mais Saül avait donné sa fille Michol, femme de David, à Phalti de Gallim, fils de Laïs.
Koma Sauli anali atakwatitsa Mikala, mkazi wa Davide kwa Paliti mwana wa Laisi wa ku Galimu.

< 1 Samuel 25 >