< Zacharie 5 >

1 Je levai de nouveau les yeux et je vis: Et voici un rouleauqui volait.
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
2 Il me dit: « Que vois-tu? » Je dis: « Je vois un rouleau qui vole; sa longueur est de vingt coudées et sa largeur de dix coudées. »
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
3 Et il me dit: C’est la malédiction qui sort sur la face de tout le pays; car, selon ce qui y est écrit, quiconque dérobe sera balayé d’ici, et, selon ce qui y est écrit, quiconque jure sera balayé d’ici.
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
4 Je l’ai déchaînée, — oracle de Yahweh des armées, — et elle arrivera à la maison du voleur et à la maison de celui qui jure par mon nom en mentant; elle se logera au milieu de sa maison et la consumera, le bois et les pierres.
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
5 L’ange qui parlait avec moi parut et me dit: « Lève les yeux et regarde ce qui apparaît. » Je dis: « Qu’est-ce? »
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
6 Il dit: « C’est l’épha qui apparaît ». Et il ajouta: « C’est à cela que s’attache leur regard dans tout le pays. »
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
7 Et voici qu’un disque de plomb fut soulevé, et il y avait une femme assise au milieu de l’épha.
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
8 Il dit: « Cette femme est l’improbité. » Et il la repoussa au milieu de l’épha et jeta sur l’ouverture de celui-ci la masse de plomb.
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
9 Et je levai les yeux, et je vis. Et voici que deux femmes apparurent; du vent soufflait dans leurs ailes; elles avaient des ailes pareilles aux ailes de la cigogne. Et elles enlevèrent l’épha entre le ciel et la terre.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
10 Je dis à l’ange qui parlait avec moi: « Où emportent-elles l’épha? »
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
11 Il me répondit: « Elles l’emportent pour lui bâtir une maison au pays de Sennaar; et, quand elle aura été fondée, on le placera là en son lieu.
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

< Zacharie 5 >