< Psaumes 53 >

1 Au maître de chant. Sur le ton plaintif. Cantique de David. L’insensé dit dans son cœur: « il n’y a pas de Dieu! » Ils sont corrompus, ils commettent des crimes abominables; il n’en est aucun qui fasse le bien.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Dieu, du haut des cieux, regarde les fils de l’homme, pour voir s’il se trouve quelqu’un d’intelligent, quelqu’un qui cherche Dieu.
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Tous sont égarés, tous sont pervertis; il n’en est aucun qui fasse le bien, pas même un seul.
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 N’ont-ils pas de connaissance ceux qui commettent l’iniquité? Ils dévorent mon peuple comme ils mangent du pain, ils n’invoquent pas Dieu!
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Ils trembleront tout à coup d’épouvante, sans qu’il y ait sujet d’épouvante; car Dieu a dispersé les os de celui qui campait contre toi; tu les as confondus, car Dieu les a rejetés.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Oh! puisse venir de Sion la délivrance d’Israël! Quand Dieu ramènera les captifs de son peuple, Jacob se réjouira, Israël sera dans l’allégresse.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!

< Psaumes 53 >